E inu amene mwakhulupirira! Musadye chuma chanu mwachinyengo koma m’njira yamalonda ndi moyanjana pakati panu. Ndipo musadziphe nokha (ngakhale kupha anzanu). Ndithudi, Allah ali Wachisoni pa inu.[118]
Ndipo musazilakelake (mwadumbo) zomwe Allah wawadalitsa nazo ena mwa inu. Amuna ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Nawonso akazi ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Ndipo mpempheni Allah zabwino zake. Ndithudi, Allah Ngodziwa chilichonse.[120]
[120] Apa akuletsa anthu kuchitirana dumbo. Koma chofunika nkuti munthu alimbike kugwira ntchito kuti nayenso apeze chomwe mnzake wapeza. Osati kumchitira dumbo ndi kumuda, pakuti iye palibe chimene wakulanda. Adagwira ntchito molimbika ndipo Allah wampatsa. Iwenso limbikira kugwira ntchito Allah akupatsa. Wopemphedwa ndi kupatsa ndiyemweyo Allah wathu.
Ndipo anthu tawaikira alowa mmalo pa zomwe asiya makolo awiri ndi achibale. Ndipo amene mudagwirizana nawo chipangano, apatseni gawo lawo. Ndithudi, Allah Ndimboni pa chilichonse.[121]
[121] Nthawi ya umbuli, munthu ankati akatenga mwana wa munthu wina nkumulera ankamuyesa mwana wake weniweni pomulowera chokolo pa chilichonse ngati mwanayo atafa. Ngakhale makolo ake enieni ndi abale ake atakhalapo sadali kuwagawira chilichonse. Tsono Chisilamu chidathetsa mchitidwe umenewu ponena kuti munthu aliyense azimlowa chokolo ndi abale ake.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
搜索结果:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".