Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 尼萨仪   段:
وَٱللَّهُ يُرِيدُ أَن يَتُوبَ عَلَيۡكُمۡ وَيُرِيدُ ٱلَّذِينَ يَتَّبِعُونَ ٱلشَّهَوَٰتِ أَن تَمِيلُواْ مَيۡلًا عَظِيمٗا
Ndiponso Allah akufuna kulandira kulapa kwanu. Koma amene akutsata zilakolako zawo akufuna mupotoke; kupotoka kwakukulu.
阿拉伯语经注:
يُرِيدُ ٱللَّهُ أَن يُخَفِّفَ عَنكُمۡۚ وَخُلِقَ ٱلۡإِنسَٰنُ ضَعِيفٗا
Allah akufuna kukupeputsirani, pakuti munthu adalengedwa wofooka (alibe mphamvu za thupi ngakhale zolimbana ndi zilakolako za moyo).
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ إِلَّآ أَن تَكُونَ تِجَٰرَةً عَن تَرَاضٖ مِّنكُمۡۚ وَلَا تَقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُمۡ رَحِيمٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musadye chuma chanu mwachinyengo koma m’njira yamalonda ndi moyanjana pakati panu. Ndipo musadziphe nokha (ngakhale kupha anzanu). Ndithudi, Allah ali Wachisoni pa inu.[118]
[118] Apa akuletsa kudyerana chuma m’njira yachinyengo. Koma kugulitsana malonda mwachimvano onse awiri nkomwe kukuloledwa. Ndipo Allah pomwe wanena kuti musadziphe, m’mawu amenewa mukutanthauza munthu kudzipha yekha, ndi kupha msilamu mnzake poti msilamu ndi msilamu mnzake ali ngati thupi limodzi. Ndipo ngakhale yemwe sali msilamu saloledwa kumupha. Mawu oti “kupha” akutanthauza kupha munthu nkuferatu nthawi yomweyo. Mawuwa akutanthauzanso kuchita chinthu chomwe chingamchititse munthu uja kuonongeka mwapang’onopang’ono mpaka mathero ake nkuferatu. Izi zili monga amene akumwa mowa wakachasu kapena wina uliwonse, akudzipha yekha. Kapenanso kuchita chinthu china chilichonse chomwe mathero ake chimamupha munthu. Ndipo nayenso amene akuthandizira zimenezi, ali m’gulu lakupha munthu.
阿拉伯语经注:
وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ عُدۡوَٰنٗا وَظُلۡمٗا فَسَوۡفَ نُصۡلِيهِ نَارٗاۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرًا
Ndipo amene achite izi molumpha malire ndi mopanda chilungamo, iyeyo tidzamulowetsa kumoto. Ndipo zimenezo nzopepuka kwa Allah.
阿拉伯语经注:
إِن تَجۡتَنِبُواْ كَبَآئِرَ مَا تُنۡهَوۡنَ عَنۡهُ نُكَفِّرۡ عَنكُمۡ سَيِّـَٔاتِكُمۡ وَنُدۡخِلۡكُم مُّدۡخَلٗا كَرِيمٗا
Ngati mudzitalikitsa kumachimo akuluakulu omwe mukuletsedwa, ndiye kuti tikufafanizirani zolakwa zanu (zing’onozing’ono) ndipo tidzakulowetsani malo aulemu.[119]
[119] Apa akuti ngati tipewa machimo akuluakulu, Allah adzatikhululukira timachimo ting’onoting’ono. Munthu nkovuta kuupewa uchimo ung’onoung’ono. Uchimotu suli wofanana. Pali wina waukulu. Palinso wina wokulitsitsa. Ndipo pali waung’ono ndi wina wochepetsetsa.
Machimo akuluakulu ali ngati awa: (a) Kuphatikiza Allah ndi mafano. (b) Kupha munthu wosalakwa. (c) Kuba. (d) Kuchita malonda akatapira (riba). (e) Kumwa zoledzeretsa. (f) Kuchita chiwerewere ndi zina zotero.
Tsono uchimo waung’ono uli monga: Kunena mawu osafunika ndi kuchiyang’ana chinthu choletsedwa ndi zina zotero zomwe nzovuta munthu kuzipewa. Choncho, munthu akapewa machimo akuluakulu ndiye kuti adzamkhululukira machimo ang’onoang’ono ngati sakuwachita mochulukitsa.
Enanso mwa machimo akuluakulu ndikusiya kutsata malamulo a Allah, monga (a) Kusiya kupemphera Swala zisanu. (b) Kusiya kupereka Zakaat ndi zithandizo zina zofunika. (c) Kusiya kumanga m’mwezi wa Ramadan. (d) Kusiya kuchita Hajj. (e) Kusiya kuyang’anira makolo ndi zina zotero.
阿拉伯语经注:
وَلَا تَتَمَنَّوۡاْ مَا فَضَّلَ ٱللَّهُ بِهِۦ بَعۡضَكُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖۚ لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا ٱكۡتَسَبُواْۖ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا ٱكۡتَسَبۡنَۚ وَسۡـَٔلُواْ ٱللَّهَ مِن فَضۡلِهِۦٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٗا
Ndipo musazilakelake (mwadumbo) zomwe Allah wawadalitsa nazo ena mwa inu. Amuna ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Nawonso akazi ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Ndipo mpempheni Allah zabwino zake. Ndithudi, Allah Ngodziwa chilichonse.[120]
[120] Apa akuletsa anthu kuchitirana dumbo. Koma chofunika nkuti munthu alimbike kugwira ntchito kuti nayenso apeze chomwe mnzake wapeza. Osati kumchitira dumbo ndi kumuda, pakuti iye palibe chimene wakulanda. Adagwira ntchito molimbika ndipo Allah wampatsa. Iwenso limbikira kugwira ntchito Allah akupatsa. Wopemphedwa ndi kupatsa ndiyemweyo Allah wathu.
阿拉伯语经注:
وَلِكُلّٖ جَعَلۡنَا مَوَٰلِيَ مِمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَۚ وَٱلَّذِينَ عَقَدَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡ فَـَٔاتُوهُمۡ نَصِيبَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدًا
Ndipo anthu tawaikira alowa mmalo pa zomwe asiya makolo awiri ndi achibale. Ndipo amene mudagwirizana nawo chipangano, apatseni gawo lawo. Ndithudi, Allah Ndimboni pa chilichonse.[121]
[121] Nthawi ya umbuli, munthu ankati akatenga mwana wa munthu wina nkumulera ankamuyesa mwana wake weniweni pomulowera chokolo pa chilichonse ngati mwanayo atafa. Ngakhale makolo ake enieni ndi abale ake atakhalapo sadali kuwagawira chilichonse. Tsono Chisilamu chidathetsa mchitidwe umenewu ponena kuti munthu aliyense azimlowa chokolo ndi abale ake.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭