Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 尼萨仪   段:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ سَنُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ وَعۡدَ ٱللَّهِ حَقّٗاۚ وَمَنۡ أَصۡدَقُ مِنَ ٱللَّهِ قِيلٗا
Ndipo omwe akhulupirira ndi kumachita zabwino, tidzawalowetsa ku Minda yomwe pansi (ndi patsogolo) pake mitsinje ikuyenda. Adzakhala m’menemo muyaya. Ili ndilonjezo loona la Allah. Kodi ndani woona ponena kuposa Allah?
阿拉伯语经注:
لَّيۡسَ بِأَمَانِيِّكُمۡ وَلَآ أَمَانِيِّ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِۗ مَن يَعۡمَلۡ سُوٓءٗا يُجۡزَ بِهِۦ وَلَا يَجِدۡ لَهُۥ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
(Kulowa ku Munda wamtendere) sikuli pa kukhumba kwanu ngakhalenso pa kukhumba kwa anthu a buku (Ayuda ndi Akhrisitu). Amene angachite choipa, adzalipidwa (nacho), ndipo sadzapeza mtetezi ngakhale mpulumutsi kupatula Allah.
阿拉伯语经注:
وَمَن يَعۡمَلۡ مِنَ ٱلصَّٰلِحَٰتِ مِن ذَكَرٍ أَوۡ أُنثَىٰ وَهُوَ مُؤۡمِنٞ فَأُوْلَٰٓئِكَ يَدۡخُلُونَ ٱلۡجَنَّةَ وَلَا يُظۡلَمُونَ نَقِيرٗا
Ndipo amene angachite ntchito zabwino, mwamuna kapena mkazi, pomwe iye ali wokhulupirira, iwo ndiamene adzalowa ku Munda wamtendere. Ndipo sadzaponderezedwa pa chilichonse, ngakhale chochepetsetsa kwambiri ngati kamphako ka nthangala ya tende.
阿拉伯语经注:
وَمَنۡ أَحۡسَنُ دِينٗا مِّمَّنۡ أَسۡلَمَ وَجۡهَهُۥ لِلَّهِ وَهُوَ مُحۡسِنٞ وَٱتَّبَعَ مِلَّةَ إِبۡرَٰهِيمَ حَنِيفٗاۗ وَٱتَّخَذَ ٱللَّهُ إِبۡرَٰهِيمَ خَلِيلٗا
Kodi ndani yemwe ali ndi chipembedzo chabwino choposa yemwe walunjika nkhope yake kwa Allah, iye ali wochita zabwino ndipo akutsata njira ya Ibrahim woona pa chikhulupiliro. Ndipo Allah adasankha Ibrahim kukhala bwenzi.
阿拉伯语经注:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٖ مُّحِيطٗا
Ndipo zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah; ndipo Allah ndi amene wazungulira chinthu chilichonse kuchidziwa.
阿拉伯语经注:
وَيَسۡتَفۡتُونَكَ فِي ٱلنِّسَآءِۖ قُلِ ٱللَّهُ يُفۡتِيكُمۡ فِيهِنَّ وَمَا يُتۡلَىٰ عَلَيۡكُمۡ فِي ٱلۡكِتَٰبِ فِي يَتَٰمَى ٱلنِّسَآءِ ٱلَّٰتِي لَا تُؤۡتُونَهُنَّ مَا كُتِبَ لَهُنَّ وَتَرۡغَبُونَ أَن تَنكِحُوهُنَّ وَٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلۡوِلۡدَٰنِ وَأَن تَقُومُواْ لِلۡيَتَٰمَىٰ بِٱلۡقِسۡطِۚ وَمَا تَفۡعَلُواْ مِنۡ خَيۡرٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِهِۦ عَلِيمٗا
Ndipo akukufunsa zomwe zikukhudza azimayi nena: “Allah akukuuzani nkhani za iwo ndi zomwe zikuwerengedwa kwa inu m’buku (ili) za akazi amasiye omwe simukuwapatsa (chiwongo chawo) chomwe chidalamulidwa kwa iwo, komabe mukufuna kuwakwatira, ndi za ana omwe ali ofooka ndi oponderezedwa; ndipo (akukuuzani) kuti limbikirani kuwayang’anira ana amasiye mwachilungamo. Ndipo chabwino chilichonse chimene muchita, Allah akuchidziwa.[150]
[150] Mukuuzidwa nkhanizi zomwe akuwerengerani mu ndime ya 2 ndi 12 M’sura yomweyi.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭