Check out the new design

Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Isrāʾ   Vers:
ذَٰلِكَ مِمَّآ أَوۡحَىٰٓ إِلَيۡكَ رَبُّكَ مِنَ ٱلۡحِكۡمَةِۗ وَلَا تَجۡعَلۡ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَ فَتُلۡقَىٰ فِي جَهَنَّمَ مَلُومٗا مَّدۡحُورًا
Izi ndi zina mwa za nzeru zomwe Mbuye wako wakuvumbulutsira. Usakhale ndi mulungu wina ndi kumphatikiza kwa Allah, kuti ungadzaponyedwe ku Jahannam uli wodzudzulidwa ndi wopirikitsidwa apa ndi apo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَفَأَصۡفَىٰكُمۡ رَبُّكُم بِٱلۡبَنِينَ وَٱتَّخَذَ مِنَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ إِنَٰثًاۚ إِنَّكُمۡ لَتَقُولُونَ قَوۡلًا عَظِيمٗا
Kodi Mbuye wanu wakusankhirani ana aamuna, ndipo mwini wadzipangira ana aakazi achingelo? Ndithu inu mukunena liwu lalikulu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَقَدۡ صَرَّفۡنَا فِي هَٰذَا ٱلۡقُرۡءَانِ لِيَذَّكَّرُواْ وَمَا يَزِيدُهُمۡ إِلَّا نُفُورٗا
Ndipo ndithu talongosola lamulo la chinthu chilichonse mwatsatanetsatane m’Qur’an iyi kuti akumbukire, ndipo (oipa) siikuwaonjezera (china) koma kuida ndi kuithawa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُل لَّوۡ كَانَ مَعَهُۥٓ ءَالِهَةٞ كَمَا يَقُولُونَ إِذٗا لَّٱبۡتَغَوۡاْ إِلَىٰ ذِي ٱلۡعَرۡشِ سَبِيلٗا
Nena: “Pakadakhala milungu ina pamodzi ndi Allah, monga momwe akunenera, ikadafuna njira yomufikira (Mbuye) Mwini Arsh (Mpando wa chifumu, ndi kumthira nkhondo).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
سُبۡحَٰنَهُۥ وَتَعَٰلَىٰ عَمَّا يَقُولُونَ عُلُوّٗا كَبِيرٗا
Wayera ndipo watukuka Allah ku zimene akunenazo; kutukuka kwakukulu (kwabasi).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
تُسَبِّحُ لَهُ ٱلسَّمَٰوَٰتُ ٱلسَّبۡعُ وَٱلۡأَرۡضُ وَمَن فِيهِنَّۚ وَإِن مِّن شَيۡءٍ إِلَّا يُسَبِّحُ بِحَمۡدِهِۦ وَلَٰكِن لَّا تَفۡقَهُونَ تَسۡبِيحَهُمۡۚ إِنَّهُۥ كَانَ حَلِيمًا غَفُورٗا
Zonse zakumitambo isanu ndi iwiri ndi nthaka ndi zam’menemo, zikulemekeza Iye; ndipo palibe chilichonse koma chikumlememekeza ndi kumtamanda; koma inu simuzindikira kulemekeza kwawo! Ndithudi Iye (Allah) Ngodekha, Ngokhululuka.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِذَا قَرَأۡتَ ٱلۡقُرۡءَانَ جَعَلۡنَا بَيۡنَكَ وَبَيۡنَ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ حِجَابٗا مَّسۡتُورٗا
Ndipo ukamawerenga Qur’an (zikukhala ngati) taika chotchinga chosaonekera pakati pako ndi pakati pa amene sadakhulupirire za tsiku la chimaliziro.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَجَعَلۡنَا عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ أَكِنَّةً أَن يَفۡقَهُوهُ وَفِيٓ ءَاذَانِهِمۡ وَقۡرٗاۚ وَإِذَا ذَكَرۡتَ رَبَّكَ فِي ٱلۡقُرۡءَانِ وَحۡدَهُۥ وَلَّوۡاْ عَلَىٰٓ أَدۡبَٰرِهِمۡ نُفُورٗا
Ndipo (ngati) taika zitsekelero m’mitima mwawo kuti angaizindikire, ndipo (ngati) mmakutu mwawo muli kulemera kwa ugonthi. Ndiponso ukamtchula m’Qur’an Mbuye wako Yekha, iwo akutembenuka ndi misana yawo moipidwa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
نَّحۡنُ أَعۡلَمُ بِمَا يَسۡتَمِعُونَ بِهِۦٓ إِذۡ يَسۡتَمِعُونَ إِلَيۡكَ وَإِذۡ هُمۡ نَجۡوَىٰٓ إِذۡ يَقُولُ ٱلظَّٰلِمُونَ إِن تَتَّبِعُونَ إِلَّا رَجُلٗا مَّسۡحُورًا
Ife tikudziwa chifukwa chomwe akuimvetsera (Qur’an), pamene akukumvetsera ndi pamene akunong’onezana awo achinyengo, pamene akunena awo oyipa (kuuza Asilamu kuti): “Inu simutsatira (wina) koma munthu wolodzedwa.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ٱنظُرۡ كَيۡفَ ضَرَبُواْ لَكَ ٱلۡأَمۡثَالَ فَضَلُّواْ فَلَا يَسۡتَطِيعُونَ سَبِيلٗا
Ona momwe akukufanizira ndi mafanizo abodza. (Nthawi zina akuti ndiwe wolodzedwa, nthawi zina akuti ndiwe mfiti!) Choncho asokera, ndipo sangathe kupeza njira (yeniyeni).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالُوٓاْ أَءِذَا كُنَّا عِظَٰمٗا وَرُفَٰتًا أَءِنَّا لَمَبۡعُوثُونَ خَلۡقٗا جَدِيدٗا
Ndipo akunena: “Kodi tikadzakhala mafupa odukaduka, tidzaukitsidwanso kukhala zolengedwa zatsopano?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Isrāʾ
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. - Übersetzungen

Übersetzung von Khalid Ibrahim Bitala.

Schließen