Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (159) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَكۡتُمُونَ مَآ أَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡبَيِّنَٰتِ وَٱلۡهُدَىٰ مِنۢ بَعۡدِ مَا بَيَّنَّٰهُ لِلنَّاسِ فِي ٱلۡكِتَٰبِ أُوْلَٰٓئِكَ يَلۡعَنُهُمُ ٱللَّهُ وَيَلۡعَنُهُمُ ٱللَّٰعِنُونَ
Ndithudi, amene akubisa zimene tavumbulutsa zomwe ndi zisonyezo zoonekera poyera, ndi chiongoko pambuyo pozifotokoza mwatsatanetsatane kwa anthu m’Buku, Allah akuwatembelera iwo. Ndiponso akuwatembelera otembelera.[9]
[9] Nkofunika kwa munthu aliyense amene wachidziwa choona kuchita izi:-
a) Kuchivomereza choonacho.
b) Kuchitsata.
c) Kuchifalitsa.
d) Kuchiphunzitsa.
Choncho, masheikh ndi maulama ali ndi mwawi pokhala ndi ntchito yapamwambayi. Achite ntchitoyi modzipereka kwatunthu, mwaulere kapena molandira malipiro ngati alipo. Apitirize kuigwira ntchitoyi pamoyo wawo wonse ngakhale atakumana ndi zovuta pa ntchitoyi. Ntchitoyi njomwe aneneri a Allah adali kugwira. Tero aigwire motsanzira momwe aneneri a Allah adali kuigwilira ntchitoyi pamakhalidwe awo ndi machitidwe awo onse. Kubisa komwe kwanenedwa m’ndimeyi sikubisa mawu a Allah kokha, komanso kubisa maphunziro a zam’dziko ofunika kwa anthu.
Chisilamu chikulimbikitsa kuti ngati munthu akudziwa chilichonse chomwe chili ndi phindu kwa anthu awaphunzitse anzake, asawabisire chifukwa choopa kuti nzeruyo angaitulukire anthu ambiri ndi kuti iye sadzapatsidwa ulemu kapena kuopa kuti ena angampose. Maganizo otere ngosafunika m’Chisilamu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (159) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen