Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (118) Surah / Kapitel: Al -I-‘Imrân
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ بِطَانَةٗ مِّن دُونِكُمۡ لَا يَأۡلُونَكُمۡ خَبَالٗا وَدُّواْ مَا عَنِتُّمۡ قَدۡ بَدَتِ ٱلۡبَغۡضَآءُ مِنۡ أَفۡوَٰهِهِمۡ وَمَا تُخۡفِي صُدُورُهُمۡ أَكۡبَرُۚ قَدۡ بَيَّنَّا لَكُمُ ٱلۡأٓيَٰتِۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite omwe sali mwa inu kukhala abwenzi; owauza chinsinsi, iwo sasiya kukuchitirani choipa. Amakonda zimene zikukuvutitsani. Chidani chawo (pa inu) chaonekera m’milomo yawo. Ndipo zimene zikubisa zifuwa zawo, nzazikulu zedi. Ndithudi, takufotokozerani zizindikiro zonse ngati inu muli anthu ozindikira.[81]
[81] Chimodzi mwa zinthu zazikulu chomwe chimachititsa kuti zochita za anthu zitheke kapena kuti zilongosoke, ndiko kuzikonza zinthuzo mwa chinsinsi. Zioneke pamaso pa anthu zili zothaitha kuzikonza. Chifukwa pali anthu ambiri oipa maganizo omwe safuna kuti zinthu za anzawo zilongosoke. Iwo amafunitsitsa kuti aziononge zisanachitike. Ndipo nchifukwa chake apa akuletsa kuwaululira zachinsinsi anthu omwe sali Asilamu, kapena kuwachita kukhala abwenzi enieni.
Komatu sikuti apa akuletsa ubwenzi wakuti: “Muli bwanji? Tili bwino”. Ndiponso sakuletsa kuwachitira zabwino ndi zachilungamo, monga momwe afotokozera pandime yachisanu nchitatu yam’surat Mumtahina. (Qur’an 60:8)
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (118) Surah / Kapitel: Al -I-‘Imrân
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen