Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Versículo: (118) Capítulo: Sura Al-‘Imrán
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ بِطَانَةٗ مِّن دُونِكُمۡ لَا يَأۡلُونَكُمۡ خَبَالٗا وَدُّواْ مَا عَنِتُّمۡ قَدۡ بَدَتِ ٱلۡبَغۡضَآءُ مِنۡ أَفۡوَٰهِهِمۡ وَمَا تُخۡفِي صُدُورُهُمۡ أَكۡبَرُۚ قَدۡ بَيَّنَّا لَكُمُ ٱلۡأٓيَٰتِۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite omwe sali mwa inu kukhala abwenzi; owauza chinsinsi, iwo sasiya kukuchitirani choipa. Amakonda zimene zikukuvutitsani. Chidani chawo (pa inu) chaonekera m’milomo yawo. Ndipo zimene zikubisa zifuwa zawo, nzazikulu zedi. Ndithudi, takufotokozerani zizindikiro zonse ngati inu muli anthu ozindikira.[81]
[81] Chimodzi mwa zinthu zazikulu chomwe chimachititsa kuti zochita za anthu zitheke kapena kuti zilongosoke, ndiko kuzikonza zinthuzo mwa chinsinsi. Zioneke pamaso pa anthu zili zothaitha kuzikonza. Chifukwa pali anthu ambiri oipa maganizo omwe safuna kuti zinthu za anzawo zilongosoke. Iwo amafunitsitsa kuti aziononge zisanachitike. Ndipo nchifukwa chake apa akuletsa kuwaululira zachinsinsi anthu omwe sali Asilamu, kapena kuwachita kukhala abwenzi enieni.
Komatu sikuti apa akuletsa ubwenzi wakuti: “Muli bwanji? Tili bwino”. Ndiponso sakuletsa kuwachitira zabwino ndi zachilungamo, monga momwe afotokozera pandime yachisanu nchitatu yam’surat Mumtahina. (Qur’an 60:8)
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Versículo: (118) Capítulo: Sura Al-‘Imrán
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar