Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (37) Surah / Kapitel: Al -I-‘Imrân
فَتَقَبَّلَهَا رَبُّهَا بِقَبُولٍ حَسَنٖ وَأَنۢبَتَهَا نَبَاتًا حَسَنٗا وَكَفَّلَهَا زَكَرِيَّاۖ كُلَّمَا دَخَلَ عَلَيۡهَا زَكَرِيَّا ٱلۡمِحۡرَابَ وَجَدَ عِندَهَا رِزۡقٗاۖ قَالَ يَٰمَرۡيَمُ أَنَّىٰ لَكِ هَٰذَاۖ قَالَتۡ هُوَ مِنۡ عِندِ ٱللَّهِۖ إِنَّ ٱللَّهَ يَرۡزُقُ مَن يَشَآءُ بِغَيۡرِ حِسَابٍ
Choncho Mbuye wake adamulandira, kulandira kwabwino; namkulitsa, kukulitsa kwabwino. Adampatsa Zakariya kuti amulere. Nthawi iliyonse Zakariya akamulowera mchipinda mwake (mwa Mariya) m’kachisimo, amampeza ali ndi chakudya. Amati: “Iwe Mariya! Ukuzipeza kuti izi?” (Iye) amati: “Izi zikuchokera kwa Allah. Ndipo Allah amampatsa yemwe wamfuna popanda chiyembekezo (mwini wakeyo).”[68]
[68] Bambo Imran, tate wake wa Mariya, adali munthu wamkulu mwa anthu akuluakulu owopa Allah panthawiyo. Atamubala mwana wakeyu iye adamwalira. Choncho akuluakulu amene adali naye pamodzi, anapikisana pankhani yolera Mariya. Kenako adagwirizana kuti achite mayere. Amene amgwere ndiyemwe alere Mariya. Tero mayerewo adakomera mneneri Zakariya, mwamuna wa mayi wake wamng’ono wa Mariya. Ndipo Allah adamsonyeza Zakariya zododometsa zambiri kwa mwanayo. Zina mwa zododometsa ndiko kupeza chakudya pamalo pomwe ankakhala mwanayo chomwe chidali chosadziwika kwa anthu kumene chachokera. Ndipo akamufunsa amati Allah ndiye wampatsa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (37) Surah / Kapitel: Al -I-‘Imrân
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen