Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Umurongo: (37) Isura: Al Im’ran (Umuryango Wa Imurani)
فَتَقَبَّلَهَا رَبُّهَا بِقَبُولٍ حَسَنٖ وَأَنۢبَتَهَا نَبَاتًا حَسَنٗا وَكَفَّلَهَا زَكَرِيَّاۖ كُلَّمَا دَخَلَ عَلَيۡهَا زَكَرِيَّا ٱلۡمِحۡرَابَ وَجَدَ عِندَهَا رِزۡقٗاۖ قَالَ يَٰمَرۡيَمُ أَنَّىٰ لَكِ هَٰذَاۖ قَالَتۡ هُوَ مِنۡ عِندِ ٱللَّهِۖ إِنَّ ٱللَّهَ يَرۡزُقُ مَن يَشَآءُ بِغَيۡرِ حِسَابٍ
Choncho Mbuye wake adamulandira, kulandira kwabwino; namkulitsa, kukulitsa kwabwino. Adampatsa Zakariya kuti amulere. Nthawi iliyonse Zakariya akamulowera mchipinda mwake (mwa Mariya) m’kachisimo, amampeza ali ndi chakudya. Amati: “Iwe Mariya! Ukuzipeza kuti izi?” (Iye) amati: “Izi zikuchokera kwa Allah. Ndipo Allah amampatsa yemwe wamfuna popanda chiyembekezo (mwini wakeyo).”[68]
[68] Bambo Imran, tate wake wa Mariya, adali munthu wamkulu mwa anthu akuluakulu owopa Allah panthawiyo. Atamubala mwana wakeyu iye adamwalira. Choncho akuluakulu amene adali naye pamodzi, anapikisana pankhani yolera Mariya. Kenako adagwirizana kuti achite mayere. Amene amgwere ndiyemwe alere Mariya. Tero mayerewo adakomera mneneri Zakariya, mwamuna wa mayi wake wamng’ono wa Mariya. Ndipo Allah adamsonyeza Zakariya zododometsa zambiri kwa mwanayo. Zina mwa zododometsa ndiko kupeza chakudya pamalo pomwe ankakhala mwanayo chomwe chidali chosadziwika kwa anthu kumene chachokera. Ndipo akamufunsa amati Allah ndiye wampatsa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Umurongo: (37) Isura: Al Im’ran (Umuryango Wa Imurani)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga