Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (1) Surah / Kapitel: Al-Ahzâb

Al-Ahzâb

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ ٱتَّقِ ٱللَّهَ وَلَا تُطِعِ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
E iwe Mneneri! Muope Allah, ndipo usamvere osakhulupirira ndi achiphamaso. Ndithu Allah Ngodziwa kwambiri; Wanzeru zakuya (m’zoyankhula ndi m’zochita Zake).[316]
[316] Sura iyi ikutchedwa Sura ya Ahzab kutanthauza kuti namtindi wa anthu. Zimenezi zidali chonchi kuti pamene Chisilamu chimafala mu mzinda wa Madina momwe mumakhalanso Ayuda, adachita nsanje yaikulu Ayudawo. Ndipo akuluakulu awo adaganiza zopita ku Makka kukakopa Arabu akumeneko kuti athandizane kuthira nkhondo Asilamu. Choncho Arabu a ku Makka adauza mitundu yonse yopembedza mafano kuti akamthire nkhondo Muhammad (s.a.w) ndi kuthetseratu chipembedzo cha Chisilamu. Tero adagwirizana ndipo adauzinga mzinda wa Madina mbali zonse. Koma Allah adatumiza angelo ndi chimphepo chamkuntho chomwe chidamwazamwaza katundu wawo. Pachifukwa ichi, onse adathawa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (1) Surah / Kapitel: Al-Ahzâb
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen