Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Aja (Korano eilutė): (1) Sūra: Sūra Al-Ahzab

Sūra Al-Ahzab

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ ٱتَّقِ ٱللَّهَ وَلَا تُطِعِ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
E iwe Mneneri! Muope Allah, ndipo usamvere osakhulupirira ndi achiphamaso. Ndithu Allah Ngodziwa kwambiri; Wanzeru zakuya (m’zoyankhula ndi m’zochita Zake).[316]
[316] Sura iyi ikutchedwa Sura ya Ahzab kutanthauza kuti namtindi wa anthu. Zimenezi zidali chonchi kuti pamene Chisilamu chimafala mu mzinda wa Madina momwe mumakhalanso Ayuda, adachita nsanje yaikulu Ayudawo. Ndipo akuluakulu awo adaganiza zopita ku Makka kukakopa Arabu akumeneko kuti athandizane kuthira nkhondo Asilamu. Choncho Arabu a ku Makka adauza mitundu yonse yopembedza mafano kuti akamthire nkhondo Muhammad (s.a.w) ndi kuthetseratu chipembedzo cha Chisilamu. Tero adagwirizana ndipo adauzinga mzinda wa Madina mbali zonse. Koma Allah adatumiza angelo ndi chimphepo chamkuntho chomwe chidamwazamwaza katundu wawo. Pachifukwa ichi, onse adathawa.
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Aja (Korano eilutė): (1) Sūra: Sūra Al-Ahzab
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti