Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Saba’   Vers:

Saba’

ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ ٱلَّذِي لَهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَهُ ٱلۡحَمۡدُ فِي ٱلۡأٓخِرَةِۚ وَهُوَ ٱلۡحَكِيمُ ٱلۡخَبِيرُ
Kuyamikidwa konse ndikwa Allah Yemwe zakumwamba ndi zapansi nzake. Ndipo kutamandidwa konse pa tsiku la chimaliziro Nkwake. ndiponso Iye Ngwanzeru zakuya, Ngodziwa chilichonse.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَعۡلَمُ مَا يَلِجُ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَمَا يَخۡرُجُ مِنۡهَا وَمَا يَنزِلُ مِنَ ٱلسَّمَآءِ وَمَا يَعۡرُجُ فِيهَاۚ وَهُوَ ٱلرَّحِيمُ ٱلۡغَفُورُ
Akudziwa zimene zikulowa m’nthaka ndi zimene zikutulukamo; ndi zimene zikutsika kumwamba ndi zimene zikukwera kumeneko. Ndipo Iye Ngwachifundo kwabasi, Ngokhululuka kwambiri.[332]
[332] M’ndime iyi Allah akutidziwitsa kuti akudziwa zonse zimene zikulowa m’nthaka monga madzi, mitembo ndi zina zotero. Ndipo akudziwanso zimene zikutuluka m’menemo - monga mmera tizirombo, miyala yamtengo wapatali ndi madzi. Ndi zomwe zikutsika kumwamba monga mvula, matalala, mphenzi, madalitso, angelo Ake ndi mabuku Ake. Ndipo akudziwanso zimene zikukwera kumwamba - monga ntchito za akapolo Ake ndi zina zotero.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَا تَأۡتِينَا ٱلسَّاعَةُۖ قُلۡ بَلَىٰ وَرَبِّي لَتَأۡتِيَنَّكُمۡ عَٰلِمِ ٱلۡغَيۡبِۖ لَا يَعۡزُبُ عَنۡهُ مِثۡقَالُ ذَرَّةٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَلَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَآ أَصۡغَرُ مِن ذَٰلِكَ وَلَآ أَكۡبَرُ إِلَّا فِي كِتَٰبٖ مُّبِينٖ
Ndipo osakhulupirira adanena: “Siizatidzera nthawi (Qiyâma).” Nena: “Iyayi! Ndikulumbira Mbuye wanga, ndithu ikudzerani. (Mbuye wanga) Wodziwa zobisika (zonse), sichingabisike kwa Iye cholemera ngati nyelere; chakumwamba, chapansi, ngakhale chochepa kuposa chimenecho; ngakhalenso chokulirapo, koma (zonsezo) zili m’buku (Lake) losonyeza poyera (chilichonse).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لِّيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِۚ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُم مَّغۡفِرَةٞ وَرِزۡقٞ كَرِيمٞ
Kuti adzawalipire amene akhulupirira ndi kuchita zabwino; iwo adzapeza chikhululuko ndi zopatsidwa zaulemu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلَّذِينَ سَعَوۡ فِيٓ ءَايَٰتِنَا مُعَٰجِزِينَ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ عَذَابٞ مِّن رِّجۡزٍ أَلِيمٞ
Koma amene alimbika kutsutsana ndi Ayah Zathu pomaganiza kuti atigonjetsa, pa iwo pali chilango chopweteka.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَيَرَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡعِلۡمَ ٱلَّذِيٓ أُنزِلَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَ هُوَ ٱلۡحَقَّ وَيَهۡدِيٓ إِلَىٰ صِرَٰطِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَمِيدِ
Koma amene apatsidwa (dalitso la) kudziwa akuzindikira kuti zimene zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako nzoona, ndipo zikuongolera ku njira ya Mwini mphamvu zoposa, Wotamandidwa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ هَلۡ نَدُلُّكُمۡ عَلَىٰ رَجُلٖ يُنَبِّئُكُمۡ إِذَا مُزِّقۡتُمۡ كُلَّ مُمَزَّقٍ إِنَّكُمۡ لَفِي خَلۡقٖ جَدِيدٍ
Ndipo osakhulupirira akunena (pouzana pakati pawo mwachipongwe): “Kodi Tikusonyezeni za munthu yemwe akukuuzani kuti (m’kadzafa) ndi kudukaduka m’dzakhala m’kalengedwe katsopano?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَفۡتَرَىٰ عَلَى ٱللَّهِ كَذِبًا أَم بِهِۦ جِنَّةُۢۗ بَلِ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ فِي ٱلۡعَذَابِ وَٱلضَّلَٰلِ ٱلۡبَعِيدِ
(Allah akunena): “Kodi (akum’ganizira Muhammad kuti) wamupekera Allah bodza, kapena wagwidwa ndi misala? Iyayi, koma osakhulupirira za tsiku la chimaliziro adzakhala m’chilango ndi m’kusokera kwakukulu.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَفَلَمۡ يَرَوۡاْ إِلَىٰ مَا بَيۡنَ أَيۡدِيهِمۡ وَمَا خَلۡفَهُم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِۚ إِن نَّشَأۡ نَخۡسِفۡ بِهِمُ ٱلۡأَرۡضَ أَوۡ نُسۡقِطۡ عَلَيۡهِمۡ كِسَفٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّكُلِّ عَبۡدٖ مُّنِيبٖ
Kodi (agwidwa ndi khungu) saona zomwe zili patsogolo pawo ndi pambuyo pawo monga thambo ndi nthaka (kuti adziwe kukhoza Kwathu kuchita zimene tafuna)? Tikadafuna tikadawakwilira ndi nthaka kapena kuwagwetsera zidutswa za thambo. Ndithu m’zimenezo muli malingaliro kwa kapolo aliyense wotembenukira (kwa Allah).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
۞ وَلَقَدۡ ءَاتَيۡنَا دَاوُۥدَ مِنَّا فَضۡلٗاۖ يَٰجِبَالُ أَوِّبِي مَعَهُۥ وَٱلطَّيۡرَۖ وَأَلَنَّا لَهُ ٱلۡحَدِيدَ
Ndithudi, Daud tidampatsa chisomo chachikulu chochokera kwa Ife. (Ndipo tidauza mapiri kuti akhale akuvomereza mapemphero a Daud pothandizana naye. Tidati): “E inu mapiri pamodzi ndi iye Daud, lemekezani (Allah), ndi inunso mbalame.” Ndipo tidamufewetsera chitsulo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَنِ ٱعۡمَلۡ سَٰبِغَٰتٖ وَقَدِّرۡ فِي ٱلسَّرۡدِۖ وَٱعۡمَلُواْ صَٰلِحًاۖ إِنِّي بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ
(Tidati kwa iye:) “Panga zovala (za chitsulo) zophanuka (zokwana thupi lonse, zodzitetezera pa nkhondo), ndipo linga bwino m’kulumikiza ndi poluka. Potero chitani zabwino. Ndithu Ine ndikuona zonse zimene mukuchita.”[333]
[333] Allah Wapamwambamwamba adamfewetsera Daud chitsulo kotero kuti adachisungunula nkusanduka ngati phala, napanga kuchokera m’phala limenelo zovala zodzitetezera pa nkhondo, ndiponso ziwiya zina zothandiza pa umoyo. Ichi chidali chisomo chachikulu chimene Allah adamdalitsa nacho iye pamodzi ndi ife tonse.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلِسُلَيۡمَٰنَ ٱلرِّيحَ غُدُوُّهَا شَهۡرٞ وَرَوَاحُهَا شَهۡرٞۖ وَأَسَلۡنَا لَهُۥ عَيۡنَ ٱلۡقِطۡرِۖ وَمِنَ ٱلۡجِنِّ مَن يَعۡمَلُ بَيۡنَ يَدَيۡهِ بِإِذۡنِ رَبِّهِۦۖ وَمَن يَزِغۡ مِنۡهُمۡ عَنۡ أَمۡرِنَا نُذِقۡهُ مِنۡ عَذَابِ ٱلسَّعِيرِ
Nayenso Sulaiman tidamgonjetsera mphepo (yomwe inkayenda mwa lamulo lake). Mayendedwe amphepoyo inkayenda kuyambira m’mawa mpaka masana ntunda wofanana ndi waulendo wa mwezi umodzi, ndiponso kuyambira masana mpaka madzulo inkayenda ntunda wofanana ndi waulendo wa mwezi umodzi. Ndipo tidamsungunulira kasupe wa mtovu. Ndiponso m’ziwanda (majini) zidaliponso zimene tidam’gonjetsera zomwe zinkam’gwilira ntchito mwa chilolezo cha Mbuye wake (Allah). Ndipo yense mwa iwo wonyoza lamulo Lathu (posiya kumumvera Sulaiman) timulawitsa chilango cha Moto woyaka.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَعۡمَلُونَ لَهُۥ مَا يَشَآءُ مِن مَّحَٰرِيبَ وَتَمَٰثِيلَ وَجِفَانٖ كَٱلۡجَوَابِ وَقُدُورٖ رَّاسِيَٰتٍۚ ٱعۡمَلُوٓاْ ءَالَ دَاوُۥدَ شُكۡرٗاۚ وَقَلِيلٞ مِّنۡ عِبَادِيَ ٱلشَّكُورُ
Ziwandazi zimampangira zimene wafuna, monga: misikiti, zithunzi zokhala ndi matupi, ndi mabeseni onga madamu ndi midenga yokhazikika. (Tidawauza:) “Chitani ntchito zabwino, E inu akubanja la Daud! Pothokoza (madalitso amene mwapatsidwa). Komatu ndiochepa othokoza mwa akapolo Anga.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَلَمَّا قَضَيۡنَا عَلَيۡهِ ٱلۡمَوۡتَ مَا دَلَّهُمۡ عَلَىٰ مَوۡتِهِۦٓ إِلَّا دَآبَّةُ ٱلۡأَرۡضِ تَأۡكُلُ مِنسَأَتَهُۥۖ فَلَمَّا خَرَّ تَبَيَّنَتِ ٱلۡجِنُّ أَن لَّوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ ٱلۡغَيۡبَ مَا لَبِثُواْ فِي ٱلۡعَذَابِ ٱلۡمُهِينِ
Pamene tidalamula imfa yake (Sulaiman), palibe chimene chidawasonyeza za imfa yake koma kachirombo ka m’nthaka (chiswe) kamene kadadya ndodo yake. Choncho pamene adagwa, ziwanda zidazindikira kuti zikadakhala zikudziwa zobisika sizidakakhala m’chilango chosambulacho.[334]
[334] Kalelo anthu adali ndi chikhulupiliro chakuti ziwanda zimadziwa zamseri; monga kudziwa zam’tsogolo. Ndipo kudapezeka kuti Sulaiman adaimilira kupemphera ku chipinda chake chopemphelera uku atatsamira ndodo yake, imfa niimpeza ali chiimilire, choncho adakhala chaka chathunthu ali chomwecho uku atafa kale. Mmenemo nkuti ziwanda zikugwira ntchito yotopetsa, osadziwa kuti Sulaiman adafa, mpaka pamene chiswe chidadya ndodo imene adatsamira, nagwa pansi. Apo mpomwe imfa yake idadziwika. Potero anthu adadziwa tsopano kuti ziwanda sizidziwa zam’tsogolo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَقَدۡ كَانَ لِسَبَإٖ فِي مَسۡكَنِهِمۡ ءَايَةٞۖ جَنَّتَانِ عَن يَمِينٖ وَشِمَالٖۖ كُلُواْ مِن رِّزۡقِ رَبِّكُمۡ وَٱشۡكُرُواْ لَهُۥۚ بَلۡدَةٞ طَيِّبَةٞ وَرَبٌّ غَفُورٞ
Ndithu padali phunziro pa anthu a dziko la Saba mokhala mwawo: (Padali) minda iwiri, kumanja ndi kumanzere. (Tidati:) “Idyani zakudya zaulere zochokera kwa Mbuye wanu, ndipo mthokozeni. Mudzi wabwino ndi Mbuye Wokhululuka.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَأَعۡرَضُواْ فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ سَيۡلَ ٱلۡعَرِمِ وَبَدَّلۡنَٰهُم بِجَنَّتَيۡهِمۡ جَنَّتَيۡنِ ذَوَاتَيۡ أُكُلٍ خَمۡطٖ وَأَثۡلٖ وَشَيۡءٖ مِّن سِدۡرٖ قَلِيلٖ
Koma adanyozera (lamulo la Allah); choncho tidawatumizira chigumula champhamvu chamadzi otchingidwa (chomwe chidawamiza ndi kuononga minda yawo). Ndipo tidawasinthira minda yawo (yabwino) kukhala minda iwiri yazipatso zowawa, ndi mitengo ya bwemba ndi mitengo pang’ono ya masawu.[335]
[335] Anthu am’mudzi wa Saba’a komwe nkudziko la Yemeni, Allah adawapatsa madalitso ambiri pamene iwo amatsatira malamuio Ake ndi kumthokoza. Adawadalitsa ndi minda ya zipatso zokoma zomwe zidalibe nyengo yeniyeni yobalira, kotero kuti azimayi ankangosenza madengu nkumangoyenda pansi pa mitengo ndipo mwadzidzidzi ankangoona madengu ali odzaza ndi zipatso zoyoyoka m’mitengoyo. Koma pamene adasiya kumuyamika Allah ndi kutsatira malamulo Ake, adawaonongera mindayo ndi chigumula ndi kuwasinthitsira zipatso zawo ndi zipatso zopanda pake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ذَٰلِكَ جَزَيۡنَٰهُم بِمَا كَفَرُواْۖ وَهَلۡ نُجَٰزِيٓ إِلَّا ٱلۡكَفُورَ
Amenewo ndiwo malipiro tidawalipira chifukwa cha kusathokoza kwawo (mtendere wa Allah). Ndipo Ife sitilipira zoterezi koma kwa okhawo osathokoza.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَجَعَلۡنَا بَيۡنَهُمۡ وَبَيۡنَ ٱلۡقُرَى ٱلَّتِي بَٰرَكۡنَا فِيهَا قُرٗى ظَٰهِرَةٗ وَقَدَّرۡنَا فِيهَا ٱلسَّيۡرَۖ سِيرُواْ فِيهَا لَيَالِيَ وَأَيَّامًا ءَامِنِينَ
Ndipo pakati pawo ndi pakati pa midzi imene tidaidalitsa, tidaikapo midzi imene idali yoonekera; ndipo tidapima m’menemo malo apaulendo. (kotero kuti amachoka malo nkufika malo ena mosavutika. Tidawauza): “Yendani m’menemo usiku ndi usana mwamtendere.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَقَالُواْ رَبَّنَا بَٰعِدۡ بَيۡنَ أَسۡفَارِنَا وَظَلَمُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ فَجَعَلۡنَٰهُمۡ أَحَادِيثَ وَمَزَّقۡنَٰهُمۡ كُلَّ مُمَزَّقٍۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَٰتٖ لِّكُلِّ صَبَّارٖ شَكُورٖ
Koma (adauda mtendere umenewu;) adati: “E Mbuye wathu! Talikitsani ntunda pakati pa maulendo athu; (kuyandikirana kwa midzi, sikukutisonyeza kuti tili pa ulendo).” Ndipo adadzichitira okha zoipa. Choncho tidawachita kukhala miyambi (imene anthu a pambuyo ankauzana pakati pawo), ndipo tidawabalalitsa; kubalalikana zedi. (Ena adathawira dziko ili, ena dziko lina). Ndithu m’zimenezo muli malingaliro kwa yense wopirira kwabasi ndi wothokoza kwambiri.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَقَدۡ صَدَّقَ عَلَيۡهِمۡ إِبۡلِيسُ ظَنَّهُۥ فَٱتَّبَعُوهُ إِلَّا فَرِيقٗا مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndipo ndithu Iblis adatsimikiza ganizo lake pa iwo choncho adamtsatira kupatula gulu la okhulupirira (moona).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَا كَانَ لَهُۥ عَلَيۡهِم مِّن سُلۡطَٰنٍ إِلَّا لِنَعۡلَمَ مَن يُؤۡمِنُ بِٱلۡأٓخِرَةِ مِمَّنۡ هُوَ مِنۡهَا فِي شَكّٖۗ وَرَبُّكَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٍ حَفِيظٞ
Ndipo iye adalibe nyonga pa iwo, koma chifukwa chakuti tionetse poyera ndani wokhulupirira tsiku la chimaliziro ndiponso ndani amene akulikaikira. Ndipo Mbuye wako Ngosunga chilichonse.[336]
[336] Pamene satana adatha kumsokeretsa Adam adaganizanso kuti adzatha kuwasokeretsa ana ake. Ndipo ana a Adam adamtsatiradi satanayo monga momwe iye ankaganizira. Komatu satana alibe mphamvu zomkakamizira mwana wa Adam kuti amtsate koma amangomuitana kupyolera m’kukometsera zilakolako zoipa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلِ ٱدۡعُواْ ٱلَّذِينَ زَعَمۡتُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ لَا يَمۡلِكُونَ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَلَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَمَا لَهُمۡ فِيهِمَا مِن شِرۡكٖ وَمَا لَهُۥ مِنۡهُم مِّن ظَهِيرٖ
Nena: “Itanani amene mukuwatcha kuti ndi milungu kusiya Allah (kuti akuthandizeni. Koma sangakuthandizeni chilichonse; pakuti iwo) alibe ngakhale kachinthu ka kumwamba ndi pansi kolemera ngati nyelere yaing’ono kwambiri; m’menemo iwo alibe gawo lililonse (lothandizana ndi Allah), ndipo ngakhale Iyenso alibe mthandizi wochokera mwa iwo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَا تَنفَعُ ٱلشَّفَٰعَةُ عِندَهُۥٓ إِلَّا لِمَنۡ أَذِنَ لَهُۥۚ حَتَّىٰٓ إِذَا فُزِّعَ عَن قُلُوبِهِمۡ قَالُواْ مَاذَا قَالَ رَبُّكُمۡۖ قَالُواْ ٱلۡحَقَّۖ وَهُوَ ٱلۡعَلِيُّ ٱلۡكَبِيرُ
Ndipo uwomboli sudzathandiza kwa Iye (Allah) kupatula amene wamuloleza. Kufikira pamene mantha adzachotsedwa m’mitima mwawo (popatsidwa chilolezo choti apulumutse ena), adzanena pakati pawo (mosangalala): “Kodi wanena chiyani Mbuye wanu?” (Adzayankha): “Ndithu Iye wanena choona; Iye Ngotukuka Ngwamkulu.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
۞ قُلۡ مَن يَرۡزُقُكُم مِّنَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ قُلِ ٱللَّهُۖ وَإِنَّآ أَوۡ إِيَّاكُمۡ لَعَلَىٰ هُدًى أَوۡ فِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Nena (kwa iwo, iwe Mneneri {s.a.w}): “Kodi ndani amakupatsani rizq (zaulere) kuchokera kumwamba ndi pansi?” (Ngati sakuyankha chifukwa chodzitukumula), nena (kwa iwo): “Ndi Allah (Mmodzi, amene akukupatsani zopatsa zaulere zochokera kumwamba ndi pansi); ndipo ife kapena inu, tili pachiongoko kapena mkusokera koonekera.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُل لَّا تُسۡـَٔلُونَ عَمَّآ أَجۡرَمۡنَا وَلَا نُسۡـَٔلُ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Nena: “Simudzafunsidwa pa zimene (ife) talakwa, nafenso sitidzafunsidwa pazimene mukuchita.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ يَجۡمَعُ بَيۡنَنَا رَبُّنَا ثُمَّ يَفۡتَحُ بَيۡنَنَا بِٱلۡحَقِّ وَهُوَ ٱلۡفَتَّاحُ ٱلۡعَلِيمُ
Nena (kwa iwo): “Mbuye wathu adzatisonkhanitsa pakati pathu (pa tsiku la chiweruziro). Kenako adzaweruza pakati pathu mwa choonadi; Iye ndi Muweruzi Wodziwa kwambiri.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ أَرُونِيَ ٱلَّذِينَ أَلۡحَقۡتُم بِهِۦ شُرَكَآءَۖ كَلَّاۚ بَلۡ هُوَ ٱللَّهُ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
Nena (kwa iwo): “Ndisonyezeni amene mwawalumikiza ndi Iye monga othandizana Naye; iyayi, sizingatheke (Iye kukhala ndi anzake), koma Iye (Yekha) ndiye Allah, Mwini Mphamvu zoposa, Wanzeru zakuya.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَٰكَ إِلَّا كَآفَّةٗ لِّلنَّاسِ بَشِيرٗا وَنَذِيرٗا وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo sitidakutumize (iwe, Mtumiki{s.a.w} kwa Arabu okha) koma kwa anthu onse, kuti ukhale wouza (okhulupirira) nkhani zabwino ndi wochenjeza otsutsa. Koma anthu ambiri sadziwa (za uthenga wako).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَيَقُولُونَ مَتَىٰ هَٰذَا ٱلۡوَعۡدُ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Eti akunena: “Nliti lidzakwaniritsidwe lonjezo ili (lakudza kwa chiweruziro) ngati mukunenadi zoona?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُل لَّكُم مِّيعَادُ يَوۡمٖ لَّا تَسۡتَـٔۡخِرُونَ عَنۡهُ سَاعَةٗ وَلَا تَسۡتَقۡدِمُونَ
Nena: “Muli nalo pangano (lotsimikizika) la tsiku limene simungathe kulichedwetsa ngakhale ola limodzi, kapena kulifulumizitsa.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَن نُّؤۡمِنَ بِهَٰذَا ٱلۡقُرۡءَانِ وَلَا بِٱلَّذِي بَيۡنَ يَدَيۡهِۗ وَلَوۡ تَرَىٰٓ إِذِ ٱلظَّٰلِمُونَ مَوۡقُوفُونَ عِندَ رَبِّهِمۡ يَرۡجِعُ بَعۡضُهُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٍ ٱلۡقَوۡلَ يَقُولُ ٱلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ لَوۡلَآ أَنتُمۡ لَكُنَّا مُؤۡمِنِينَ
Ndipo amene sadakhulupirire akunena: “Sitiikhulupirira Qur’an iyi, ngakhalenso (mabuku) aja apatsogolo pake.” Ndipo ukadawaona achinyengo pamene azikaimiritsidwa pamaso pa Mbuye wawo, (ukadaona zoopsa zazikulu), uku pakati pawo akubwezerana mawu. Amene adaponderezedwa adzanena kwa amene adadzikweza: “Kukadapanda inu (kutipondereza), tikadakhala okhulupirira.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُوٓاْ أَنَحۡنُ صَدَدۡنَٰكُمۡ عَنِ ٱلۡهُدَىٰ بَعۡدَ إِذۡ جَآءَكُمۖ بَلۡ كُنتُم مُّجۡرِمِينَ
Amene adadzikweza adzanena kwa amene adaponderezedwa: “Ha, kodi ife tidakutsekerezani ku chiongoko chitakudzerani? Iyayi, koma mudali oipa.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ بَلۡ مَكۡرُ ٱلَّيۡلِ وَٱلنَّهَارِ إِذۡ تَأۡمُرُونَنَآ أَن نَّكۡفُرَ بِٱللَّهِ وَنَجۡعَلَ لَهُۥٓ أَندَادٗاۚ وَأَسَرُّواْ ٱلنَّدَامَةَ لَمَّا رَأَوُاْ ٱلۡعَذَابَۚ وَجَعَلۡنَا ٱلۡأَغۡلَٰلَ فِيٓ أَعۡنَاقِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۖ هَلۡ يُجۡزَوۡنَ إِلَّا مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo amene adaponderezedwa adzanena kwa amene adadzikweza: “Iyayi, koma (mumachita) ndale za usiku ndi usana (zotitsekereza nazo ku chikhulupiliro) pamene mumatilamula kuti tinkanire Allah ndikumpangira Iye milungu inzake.” Iwo adzabisa madandaulo pamene adzaona chilango. Ndipo tidzaika magoli m’makosi mwa amene sadakhulupirire; kodi angalipidwe china, osati zija ankachita?[337]
[337] M’ndime iyi, Allah akutifotokozera kuti pa tsiku la chimaliziro padzakhala kukangana pakati pa atsogeleri ndi anthu otsogoleredwa. Izi zidzachitika pamene otsogoleredwa adzatsimikiza kuti atsogoleri awo amawasokeza; ankangowalangiza zachabe. Potero adzakhala ndi madandaulo aakulu chifukwa chotsatira anthu osokera. Komatu madandaulo oterewa sadzawapindulira chilichonse popeza mwayi udzakhala utatha kale. Choncho nkofunika kuti potsata mtsogoleri aliyense tiyambe taganizira komwe akunka nafe; tisangokokedwa ngati nyama pakuti Allah adatipatsa dalitso lanzeru. Choncho tigwiritse ntchito bwino nzeru tsoka lisanatigwere.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا فِي قَرۡيَةٖ مِّن نَّذِيرٍ إِلَّا قَالَ مُتۡرَفُوهَآ إِنَّا بِمَآ أُرۡسِلۡتُم بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Palibe pamene tidatuma mchenjezi m’mudzi uliwonse koma opeza bwino a m’mudzimo ankanena: “Ndithu ife tikuzikana zimene mwatumidwa nazozi.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالُواْ نَحۡنُ أَكۡثَرُ أَمۡوَٰلٗا وَأَوۡلَٰدٗا وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
Ndipo ankanena (monyada): “Ife tili ndi chuma chambiri ndi ana (amhiri); choncho ife sitidzalangidwa (pa tsiku la chimaliziro).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ إِنَّ رَبِّي يَبۡسُطُ ٱلرِّزۡقَ لِمَن يَشَآءُ وَيَقۡدِرُ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Nena: “Ndithu Mbuye wanga amamchulukitsira rizq (zopatsa) laulere amene wamfuna (ngakhale ali woipa), ndipo amamchepetsera (amene wamfuna ngakhale kuti ndi munthu wabwino). Koma anthu ambiri sazindikira (zimenezi).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَآ أَمۡوَٰلُكُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُكُم بِٱلَّتِي تُقَرِّبُكُمۡ عِندَنَا زُلۡفَىٰٓ إِلَّا مَنۡ ءَامَنَ وَعَمِلَ صَٰلِحٗا فَأُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ جَزَآءُ ٱلضِّعۡفِ بِمَا عَمِلُواْ وَهُمۡ فِي ٱلۡغُرُفَٰتِ ءَامِنُونَ
Ndipo sichuma chanu ndi ana anu zomwe zingakuyandikitseni kwa Ife ulemelero, koma (chikhulupiliro cha) amene wakhulupirira ndi kuchita zabwino. Iwo adzapeza malipiro owonjezeka kwambiri pa zomwe adachita. Iwo adzakhala mwamtendere m’zipinda za ku Minda ya mtendere.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلَّذِينَ يَسۡعَوۡنَ فِيٓ ءَايَٰتِنَا مُعَٰجِزِينَ أُوْلَٰٓئِكَ فِي ٱلۡعَذَابِ مُحۡضَرُونَ
Ndipo amene akuchita khama kulimbana ndi zizindikiro Zathu ndi cholinga choti alepheretse (zofuna Zathu,) iwowo adzabweretsedwa ku chilango (cha Moto).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ إِنَّ رَبِّي يَبۡسُطُ ٱلرِّزۡقَ لِمَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦ وَيَقۡدِرُ لَهُۥۚ وَمَآ أَنفَقۡتُم مِّن شَيۡءٖ فَهُوَ يُخۡلِفُهُۥۖ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلرَّٰزِقِينَ
Nena (iwe Mneneri): “Ndithu Mbuye wanga amamchulukitsira rizq (zaulere) amene wamfuna mwa akapolo Ake; ndiponso amamchepetsera (amene wamfuna). Ndipo chilichonse chimene mupereka, Iye adzakupatsani china m’malo mwake; Iye Ngwabwino popatsa zaulere, kuposa opatsa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَيَوۡمَ يَحۡشُرُهُمۡ جَمِيعٗا ثُمَّ يَقُولُ لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ أَهَٰٓؤُلَآءِ إِيَّاكُمۡ كَانُواْ يَعۡبُدُونَ
Ndipo (kumbuka iwe Mneneri) tsiku limene (Allah) adzawasonkhanitsa onse ndi kunena kwa angelo: “Kodi awa amapembedza inu?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قَالُواْ سُبۡحَٰنَكَ أَنتَ وَلِيُّنَا مِن دُونِهِمۖ بَلۡ كَانُواْ يَعۡبُدُونَ ٱلۡجِنَّۖ أَكۡثَرُهُم بِهِم مُّؤۡمِنُونَ
Adzanena: “Kuyera konse Nkwanu (simungakhale limodzi ndi milungu ina!) Inu ndinu Mtetezi wathu, osati iwo. Koma amagwadira majini (ziwanda); ambiri mwa iwo (anthu) adakhulupirira izo (ziwanda).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَٱلۡيَوۡمَ لَا يَمۡلِكُ بَعۡضُكُمۡ لِبَعۡضٖ نَّفۡعٗا وَلَا ضَرّٗا وَنَقُولُ لِلَّذِينَ ظَلَمُواْ ذُوقُواْ عَذَابَ ٱلنَّارِ ٱلَّتِي كُنتُم بِهَا تُكَذِّبُونَ
(Allah adzawauza iwo:) “Lero aliyense mwa inu sangathe kudzetsa zabwino ngakhale masautso pa ena.” Ndipo tidzawauza amene adadzichitira okha zoipa: “Lawani chilango cha Moto chimene munkachitsutsa.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتُنَا بَيِّنَٰتٖ قَالُواْ مَا هَٰذَآ إِلَّا رَجُلٞ يُرِيدُ أَن يَصُدَّكُمۡ عَمَّا كَانَ يَعۡبُدُ ءَابَآؤُكُمۡ وَقَالُواْ مَا هَٰذَآ إِلَّآ إِفۡكٞ مُّفۡتَرٗىۚ وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لِلۡحَقِّ لَمَّا جَآءَهُمۡ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ مُّبِينٞ
Ndipo Ayah Zathu zofotokoza momveka zikamawerengedwa kwa iwo, amanena, “Sichina uyu (Muhammad {s.a.w}) koma ndi munthu yemwe akufuna kukutsekerezani mapemphero amene amapemphera makolo anu.” Ndipo akunena: “Sichina iyi (Qur’an) koma ndibodza lopekedwa.” Ndipo amene sadakhulupirire akunena pa choona pamene chawadzera: “Sikanthu ichi, koma ndi matsenga woonekera.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَآ ءَاتَيۡنَٰهُم مِّن كُتُبٖ يَدۡرُسُونَهَاۖ وَمَآ أَرۡسَلۡنَآ إِلَيۡهِمۡ قَبۡلَكَ مِن نَّذِيرٖ
Ndipo (ngakhale awa Arabu) sitidawapatse mabuku oti aziwawerenga (buku ili lisanadze); ndipo sitidawatumizirenso mchenjezi patsogolo pako. (Nanga akudziwa bwanji kuti Qur’an iyi ndiyonama?)
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَكَذَّبَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ وَمَا بَلَغُواْ مِعۡشَارَ مَآ ءَاتَيۡنَٰهُمۡ فَكَذَّبُواْ رُسُلِيۖ فَكَيۡفَ كَانَ نَكِيرِ
Ndipo amene adalipo iwowo kulibe, adatsutsa, ndipo (awa Arabu) sadapeze gawo limodzi m’magawo khumi a zomwe tidawapatsa iwowo, koma adatsutsa atumiki Anga (pa zomwe adawabweretsera). Nanga chidali bwanji chilango Changa (pa iwo)?
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
۞ قُلۡ إِنَّمَآ أَعِظُكُم بِوَٰحِدَةٍۖ أَن تَقُومُواْ لِلَّهِ مَثۡنَىٰ وَفُرَٰدَىٰ ثُمَّ تَتَفَكَّرُواْۚ مَا بِصَاحِبِكُم مِّن جِنَّةٍۚ إِنۡ هُوَ إِلَّا نَذِيرٞ لَّكُم بَيۡنَ يَدَيۡ عَذَابٖ شَدِيدٖ
Nena: “Ndithu ndikukulangizani chinthu chimodzi, kuti muimilire chifukwa cha Allah; awiriawiri ndi mmodzimmodzi, ndipo kenako mulingalire; (muona kuti uyu Muhammad {s.a.w} chilichonse chomwe akunena nchoona. Ndiponso muona kuti) mnzanuyu alibe misala. Iye, sichina, koma ndimchenjezi wanu chisanadze chilango chaukali.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ مَا سَأَلۡتُكُم مِّنۡ أَجۡرٖ فَهُوَ لَكُمۡۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَى ٱللَّهِۖ وَهُوَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدٞ
Nena: “Chilichonse ndakupemphani kukhala malipiro (othandizira kufikitsa uthenga kwa anthu) ndichanu, malipiro anga ali kwa Allah basi. Ndipo Iye ndi Mboni pachilichonse.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ إِنَّ رَبِّي يَقۡذِفُ بِٱلۡحَقِّ عَلَّٰمُ ٱلۡغُيُوبِ
Nena: “Ndithu Mbuye wanga amaponya choonadi (ponseponse kotero kuti chonama chimathawa). Ngodziwa zedi (zinthu) zobisika.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ جَآءَ ٱلۡحَقُّ وَمَا يُبۡدِئُ ٱلۡبَٰطِلُ وَمَا يُعِيدُ
Nena: “Choonadi chadza (chisilamu); ndipo chabodza (chipembedzo cha mafano) sichidzetsa zachilendo, ndiponso sichibwerera (kukhala ndi nyonga monga kale).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ إِن ضَلَلۡتُ فَإِنَّمَآ أَضِلُّ عَلَىٰ نَفۡسِيۖ وَإِنِ ٱهۡتَدَيۡتُ فَبِمَا يُوحِيٓ إِلَيَّ رَبِّيٓۚ إِنَّهُۥ سَمِيعٞ قَرِيبٞ
Nena: “Ngati ndasokera, ndiye kuti ndadzisokeretsa ndekha (ndadziyika ndekha m’mavuto). Koma ngati ndaongoka, ndichifukwa cha zimene akundivumbulutsira Mbuye wanga. Ndithu Iye Ngwakumva; ali pafupi (ndi aliyense).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَوۡ تَرَىٰٓ إِذۡ فَزِعُواْ فَلَا فَوۡتَ وَأُخِذُواْ مِن مَّكَانٖ قَرِيبٖ
Ndipo ukadaona pamene adzanjenjemera (akadzachiona chilango cha Allah, adzayesera kuthawa), koma sipadzapezeka pothawira, ndipo adzagwidwa pamtunda wapafupi (asanafike kutali).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِهِۦ وَأَنَّىٰ لَهُمُ ٱلتَّنَاوُشُ مِن مَّكَانِۭ بَعِيدٖ
Ndipo adzanena (mophuphaphupha): “Tachikhulupirira (tsopano chipembedzo cha Chisilamu).” Koma iwo angaulandire chotani (Usilamu) kumeneko (komwe) ndikumalo akutali.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَقَدۡ كَفَرُواْ بِهِۦ مِن قَبۡلُۖ وَيَقۡذِفُونَ بِٱلۡغَيۡبِ مِن مَّكَانِۭ بَعِيدٖ
Pomwe chikhalirenicho adachikana kale (Chisilamu). Ndipo chobisika ankachigenda (ndi bodza) kuchokera kumalo akutali.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَحِيلَ بَيۡنَهُمۡ وَبَيۡنَ مَا يَشۡتَهُونَ كَمَا فُعِلَ بِأَشۡيَاعِهِم مِّن قَبۡلُۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ فِي شَكّٖ مُّرِيبِۭ
Ndipo padzatsekeka pakati pawo ndi zimene akuzilakalaka, monga momwe adachitidwira anzawo akale. Ndithu iwo adali m’chikaiko chowakaikitsa (uthenga wa Allah).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Saba’
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen