Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (29) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ إِلَّآ أَن تَكُونَ تِجَٰرَةً عَن تَرَاضٖ مِّنكُمۡۚ وَلَا تَقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُمۡ رَحِيمٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musadye chuma chanu mwachinyengo koma m’njira yamalonda ndi moyanjana pakati panu. Ndipo musadziphe nokha (ngakhale kupha anzanu). Ndithudi, Allah ali Wachisoni pa inu.[118]
[118] Apa akuletsa kudyerana chuma m’njira yachinyengo. Koma kugulitsana malonda mwachimvano onse awiri nkomwe kukuloledwa. Ndipo Allah pomwe wanena kuti musadziphe, m’mawu amenewa mukutanthauza munthu kudzipha yekha, ndi kupha msilamu mnzake poti msilamu ndi msilamu mnzake ali ngati thupi limodzi. Ndipo ngakhale yemwe sali msilamu saloledwa kumupha. Mawu oti “kupha” akutanthauza kupha munthu nkuferatu nthawi yomweyo. Mawuwa akutanthauzanso kuchita chinthu chomwe chingamchititse munthu uja kuonongeka mwapang’onopang’ono mpaka mathero ake nkuferatu. Izi zili monga amene akumwa mowa wakachasu kapena wina uliwonse, akudzipha yekha. Kapenanso kuchita chinthu china chilichonse chomwe mathero ake chimamupha munthu. Ndipo nayenso amene akuthandizira zimenezi, ali m’gulu lakupha munthu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (29) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen