Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (29) Chương: Chương Al-Nisa'
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ إِلَّآ أَن تَكُونَ تِجَٰرَةً عَن تَرَاضٖ مِّنكُمۡۚ وَلَا تَقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُمۡ رَحِيمٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musadye chuma chanu mwachinyengo koma m’njira yamalonda ndi moyanjana pakati panu. Ndipo musadziphe nokha (ngakhale kupha anzanu). Ndithudi, Allah ali Wachisoni pa inu.[118]
[118] Apa akuletsa kudyerana chuma m’njira yachinyengo. Koma kugulitsana malonda mwachimvano onse awiri nkomwe kukuloledwa. Ndipo Allah pomwe wanena kuti musadziphe, m’mawu amenewa mukutanthauza munthu kudzipha yekha, ndi kupha msilamu mnzake poti msilamu ndi msilamu mnzake ali ngati thupi limodzi. Ndipo ngakhale yemwe sali msilamu saloledwa kumupha. Mawu oti “kupha” akutanthauza kupha munthu nkuferatu nthawi yomweyo. Mawuwa akutanthauzanso kuchita chinthu chomwe chingamchititse munthu uja kuonongeka mwapang’onopang’ono mpaka mathero ake nkuferatu. Izi zili monga amene akumwa mowa wakachasu kapena wina uliwonse, akudzipha yekha. Kapenanso kuchita chinthu china chilichonse chomwe mathero ake chimamupha munthu. Ndipo nayenso amene akuthandizira zimenezi, ali m’gulu lakupha munthu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (29) Chương: Chương Al-Nisa'
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại