Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (71) Surah: Al-Kahf
فَٱنطَلَقَا حَتَّىٰٓ إِذَا رَكِبَا فِي ٱلسَّفِينَةِ خَرَقَهَاۖ قَالَ أَخَرَقۡتَهَا لِتُغۡرِقَ أَهۡلَهَا لَقَدۡ جِئۡتَ شَيۡـًٔا إِمۡرٗا
Choncho onse awiri adanyamuka kufikira pamene adakakwera m’chombo adachiboola. (Mûsa) adati: “Kodi wachiboola kuti uwamize ali m’menemo? Ndithu wachita chinthu chachikulu choipa.”[260]
[260] Tanthauzo lake nkuti pamene onse awiri adanyamuka adali kuyenda m’mphepete mwanyanja kufikira chombo chidawadutsa. Eni chombowo adamdziwa Khidhiru nawakweza onse awiri popanda malipiro. Atakwera m’chombomo Khidhiru adatenga nkhwangwa ndi kuzula thabwa limodzi la m’chombomo pomwe chombocho chidali pakatikati pa nyanja.
Musa ataona anati: “Bwanji ukuboola chombo pomwe anthuwa atinyamula mwaulere?” Ndipo adatenga kasanza nkuika pomwe panachotsedwa thabwapo.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (71) Surah: Al-Kahf
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close