Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (58) Surah: An-Nisā’
۞ إِنَّ ٱللَّهَ يَأۡمُرُكُمۡ أَن تُؤَدُّواْ ٱلۡأَمَٰنَٰتِ إِلَىٰٓ أَهۡلِهَا وَإِذَا حَكَمۡتُم بَيۡنَ ٱلنَّاسِ أَن تَحۡكُمُواْ بِٱلۡعَدۡلِۚ إِنَّ ٱللَّهَ نِعِمَّا يَعِظُكُم بِهِۦٓۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ سَمِيعَۢا بَصِيرٗا
Ndithudi, Allah akukulamulani kubweza kwa eni zomwe mwakhulupirika nazo. Ndipo pamene mukuweruza pakati pa anthu, weruzani mwachilungamo. Ndithu malangizo amene Allah akukulangizani, ngabwino kwambiri. Ndithudi, Allah Ngwakumva, Ngoona.[130]
[130] Pali anthu ena amene amati anzawo akawasungitsa zinthu kuti akhulupirike pa zimenezo, mwini zinthu uja akafa kapena kuti panalibe umboni wokwanira, amazitenga zinthuzo poganizira kuti palibe chomwe chingawavute popeza mwini zinthuzo adamwalira ndipo umboni wokwanira palibe. Chikhalidwe chotere si cha Chisilamu, Chisilamu sichifuna machitidwe otere.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (58) Surah: An-Nisā’
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close