Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Versículo: (258) Capítulo: Sura Al-Baqara
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِي حَآجَّ إِبۡرَٰهِـۧمَ فِي رَبِّهِۦٓ أَنۡ ءَاتَىٰهُ ٱللَّهُ ٱلۡمُلۡكَ إِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّيَ ٱلَّذِي يُحۡيِۦ وَيُمِيتُ قَالَ أَنَا۠ أُحۡيِۦ وَأُمِيتُۖ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ فَإِنَّ ٱللَّهَ يَأۡتِي بِٱلشَّمۡسِ مِنَ ٱلۡمَشۡرِقِ فَأۡتِ بِهَا مِنَ ٱلۡمَغۡرِبِ فَبُهِتَ ٱلَّذِي كَفَرَۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi sudamve za yemwe adatsutsana ndi Ibrahim pa za Mbuye wake (Allah)? (Ankanyada) pachifukwa chakuti Allah adampatsa ufumu. Ibrahim adati: “Mbuye wanga ndi yemwe amapereka moyo ndi imfa.” Iye adati: “Inenso ndimapereka moyo ndi imfa.” Ibrahim Adati: “Ndithu Allah amatulutsa dzuwa ku vuma, choncho iwe ulitulutse ku zambwe.” Ndipo uja wosakhulupirira adangoti kakasi, (kusowa chonena). Ndipo Allah satsogolera anthu ochita zoipa.[50]
[50] M’nthawi ya mneneri Ibrahim padali mfumu ina yodzikuza yomwe inkadzitcha kuti ndimulungu ndipo anthu ake adali kuipembedza. Pamene mneneri Ibrahim adadza nayamba kuphunzitsa chipembedzo choona ndikuti iyeyo si mulungu, mfumuyo idati kwa mneneri Ibrahim: “Kodi Mulungu wako woonayo amachita chiyani?” Iye adati “Amapereka moyo ndi kuperekanso imfa.” Mfumuyo idachita ngati sidamvetse cholinga cha mawu a mneneri Ibrahim. Idati: “Nanenso ndimachita zimenezo. Taona mmene ndimachitira.” Pompo adalamula kuti abwere nawo anthu awiri omwe adawalamula kuti aphedwe. Iye adalamula kuti mmodzi aphedwe ndipo winayo amsiye. Choncho zidachitika. Tsono adamuuza Ibrahim: “Waona bwanji? Kodi wina sindidampatse moyo ndipo winayo imfa?” Mneneri Ibrahim pomwe anaona kuti mfumuyo ikungodzipusitsa daladala adaiuza chinthu chomwe iyo sikadatha kuchichita. Adati: “Allah amatulutsa dzuwa ku vuma ndipo iwe ulitulutse ku zambwe.” Pamenepo mfumuyo idangoti kakasi, sidachite chilichonse ndiponso sidanene chilichonse.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Versículo: (258) Capítulo: Sura Al-Baqara
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar