Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Versículo: (10) Capítulo: Sura Al-Mumtahana
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا جَآءَكُمُ ٱلۡمُؤۡمِنَٰتُ مُهَٰجِرَٰتٖ فَٱمۡتَحِنُوهُنَّۖ ٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِإِيمَٰنِهِنَّۖ فَإِنۡ عَلِمۡتُمُوهُنَّ مُؤۡمِنَٰتٖ فَلَا تَرۡجِعُوهُنَّ إِلَى ٱلۡكُفَّارِۖ لَا هُنَّ حِلّٞ لَّهُمۡ وَلَا هُمۡ يَحِلُّونَ لَهُنَّۖ وَءَاتُوهُم مَّآ أَنفَقُواْۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ أَن تَنكِحُوهُنَّ إِذَآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ أُجُورَهُنَّۚ وَلَا تُمۡسِكُواْ بِعِصَمِ ٱلۡكَوَافِرِ وَسۡـَٔلُواْ مَآ أَنفَقۡتُمۡ وَلۡيَسۡـَٔلُواْ مَآ أَنفَقُواْۚ ذَٰلِكُمۡ حُكۡمُ ٱللَّهِ يَحۡكُمُ بَيۡنَكُمۡۖ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Akakudzerani okhulupirira aakazi osamuka, ayeseni mayeso (kuti mudziwe chikhulupiliro chawo); Allah ali wodziwa kwambiri za chikhulupiliro chawo; ngati mutawadziwa kuti ndiokhulupirira musawabwezere kwa osakhulupirira. Akaziwo saloledwa kukwatiwa ndi osakhulupirira, iwonso saloledwa kuwakwatira. Abwezereni chiwongo chimene adapereka amuna osakhulupirirawo. Ndipo palibe tchimo kwa inu kuwakwatira, (ngakhale adasiya amuna awo achikafiri (ku Makka) ngati muwapatsa chiwongo chawo. Musakakamire maukwati ndi akazi achikafiri (osakhulupirira amene adatsalira ku Makka). Itanitsani zimene mudapereka kwa akazi anu (achikafiriwo), naonso Akafiri aitanitse zimene adapereka (kwa akazi awo akalowa m’Chisilamu). Limeneli ndi lamulo la Allah limene akulamula pakati panu. Allah ndiwodziwa kwambiri ndiponso Ngwanzeru (poika malamulo).
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Versículo: (10) Capítulo: Sura Al-Mumtahana
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar