Check out the new design

ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمه‌ى چوایی - خالد ابراهیم بيتالا * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: حج   آیه:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ سَخَّرَ لَكُم مَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَٱلۡفُلۡكَ تَجۡرِي فِي ٱلۡبَحۡرِ بِأَمۡرِهِۦ وَيُمۡسِكُ ٱلسَّمَآءَ أَن تَقَعَ عَلَى ٱلۡأَرۡضِ إِلَّا بِإِذۡنِهِۦٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِٱلنَّاسِ لَرَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Kodi sudaone kuti Allah wakufewetserani zonse zam’nthaka ndi zombo zomwe zikuyenda panyanja mwa lamulo Lake? Ndipo wagwira thambo kuti lisagwe panthaka koma kupyolera m’chilolezo Chake; ndithu Allah Ngodekha kwa anthu Ngwachifundo.
تفسیرهای عربی:
وَهُوَ ٱلَّذِيٓ أَحۡيَاكُمۡ ثُمَّ يُمِيتُكُمۡ ثُمَّ يُحۡيِيكُمۡۗ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَكَفُورٞ
Ndipo Iye ndi Amene adakupatsani moyo; kenako adzakupatsani imfa, ndipo kenako adzakuukitsani; ndithu munthu ngosathokoza.
تفسیرهای عربی:
لِّكُلِّ أُمَّةٖ جَعَلۡنَا مَنسَكًا هُمۡ نَاسِكُوهُۖ فَلَا يُنَٰزِعُنَّكَ فِي ٱلۡأَمۡرِۚ وَٱدۡعُ إِلَىٰ رَبِّكَۖ إِنَّكَ لَعَلَىٰ هُدٗى مُّسۡتَقِيمٖ
Mpingo uliwonse tidauikira machitidwe amapemphero omwe akuwatsata; choncho asatsutsane nawe pachinthu ichi, ndipo itanira anthu ku chipembedzo cha Mbuye wako. Ndithu iwe uli pachiongoko changwilo.
تفسیرهای عربی:
وَإِن جَٰدَلُوكَ فَقُلِ ٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِمَا تَعۡمَلُونَ
Ndipo ngati atsutsana nawe, nena: “Allah Ngodziwa koposa zimene mukuchita.”
تفسیرهای عربی:
ٱللَّهُ يَحۡكُمُ بَيۡنَكُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ فِيمَا كُنتُمۡ فِيهِ تَخۡتَلِفُونَ
“Allah adzaweruza pakati panu tsiku la Qiyâma pa zimene mudali kusiyana.”
تفسیرهای عربی:
أَلَمۡ تَعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُ مَا فِي ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِۚ إِنَّ ذَٰلِكَ فِي كِتَٰبٍۚ إِنَّ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٞ
Kodi sudziwa kuti Allah akudziwa zakumwamba ndi zapansi? Ndithu zonsezo zili m’kaundula (Wake), ndithu (kudziwika kwa) zimenezo kwa Allah nzosavuta.
تفسیرهای عربی:
وَيَعۡبُدُونَ مِن دُونِ ٱللَّهِ مَا لَمۡ يُنَزِّلۡ بِهِۦ سُلۡطَٰنٗا وَمَا لَيۡسَ لَهُم بِهِۦ عِلۡمٞۗ وَمَا لِلظَّٰلِمِينَ مِن نَّصِيرٖ
Ndipo akupembedza milungu yabodza, kusiya Allah, yomwe (Allah) sadaitumizire umboni wakuti (ipembedzedwe) yomwenso iwo sakuidziwa bwino. Ndipo anthu osalungama sadzakhala ndi owathandiza.
تفسیرهای عربی:
وَإِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتُنَا بَيِّنَٰتٖ تَعۡرِفُ فِي وُجُوهِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱلۡمُنكَرَۖ يَكَادُونَ يَسۡطُونَ بِٱلَّذِينَ يَتۡلُونَ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتِنَاۗ قُلۡ أَفَأُنَبِّئُكُم بِشَرّٖ مِّن ذَٰلِكُمُۚ ٱلنَّارُ وَعَدَهَا ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
Koma Ayah Zathu zomveka zikawerengedwa kwa iwo, uona kunyansidwa pankhope za amene sadakhulupirire. Ndipo amakhala pafupi kuwamenya amene amawawerengera Ayah Zathu. Nena: “Kodi ndikuuzeni zoipa kwambiri kuposa izi? Ndi Moto (wa Allah) umene wawalonjeza amene sadakhulupirire (Allah ndi Mtumiki Wake) amenewo ndi mabwelero oipa zedi.”
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: حج
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمه‌ى چوایی - خالد ابراهیم بيتالا - لیست ترجمه ها

مترجم: خالد ابراهیم بیتالا.

بستن