ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: سوره سجده   آیه:

سوره سجده

الٓمٓ
Alif-Lâm-Mîm.
تفسیرهای عربی:
تَنزِيلُ ٱلۡكِتَٰبِ لَا رَيۡبَ فِيهِ مِن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Chivumbulutso cha buku (la Qur’an) chilibe chikaiko mkati mwake chochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.
تفسیرهای عربی:
أَمۡ يَقُولُونَ ٱفۡتَرَىٰهُۚ بَلۡ هُوَ ٱلۡحَقُّ مِن رَّبِّكَ لِتُنذِرَ قَوۡمٗا مَّآ أَتَىٰهُم مِّن نَّذِيرٖ مِّن قَبۡلِكَ لَعَلَّهُمۡ يَهۡتَدُونَ
Kapena akunena kuti: “Walipeka yekha (bukulo)?” Iyayi, ichi nchoona chimene chachokera kwa Mbuye wako kuti uwachenjeze anthu ndi chimenechi, amene sadawadzere mchenjezi iwe usadadze. Kuti aongoke (ndi kutsatira njira yolungama).
تفسیرهای عربی:
ٱللَّهُ ٱلَّذِي خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ وَمَا بَيۡنَهُمَا فِي سِتَّةِ أَيَّامٖ ثُمَّ ٱسۡتَوَىٰ عَلَى ٱلۡعَرۡشِۖ مَا لَكُم مِّن دُونِهِۦ مِن وَلِيّٖ وَلَا شَفِيعٍۚ أَفَلَا تَتَذَكَّرُونَ
Allah ndi Yemwe adalenga thambo ndi nthaka ndi zapakati pake m’masiku asanu ndi limodzi; kenako adakhazikika pa Arsh (Mpando Wake wachifumu); (kukhazikika kolingana ndi ulemelero Wake, kumene Iye Mwini wake akukudziwa). Inu mulibe mtetezi ngakhale muomboli kupatula Iye. Nanga kodi bwanji simulingalira?[315]
[315] M’ndime iyi Allah akutiuza kuti adalenga thambo ndi nthaka ndi zapakati pake m’masiku asanu ndi limodzi. Komatu nthawi ya masiku amenewa, palibe amene akudziwa tsatanetsatane wake koma Allah Yekha. Choncho tisaganizire kuti masikuwo adali olingana ndi masiku a moyo uno wadziko lapansi.
تفسیرهای عربی:
يُدَبِّرُ ٱلۡأَمۡرَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ ثُمَّ يَعۡرُجُ إِلَيۡهِ فِي يَوۡمٖ كَانَ مِقۡدَارُهُۥٓ أَلۡفَ سَنَةٖ مِّمَّا تَعُدُّونَ
(Iye) akuyendetsa zinthu (zonse) kuchokera kumwamba kupita pansi. Kenako zidzakwera kubwerera kwa Iye, pa tsiku lolingana ndi zaka chikwi chimodzi (poyerekeza ndi zaka zadziko lapansi) mzomwe inu mumawerengera.
تفسیرهای عربی:
ذَٰلِكَ عَٰلِمُ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ameneyo (ndi Allah), Wodziwa zobisika ndi zoonekera; Mwini mphamvu zoposa Wachisoni chosatha.
تفسیرهای عربی:
ٱلَّذِيٓ أَحۡسَنَ كُلَّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥۖ وَبَدَأَ خَلۡقَ ٱلۡإِنسَٰنِ مِن طِينٖ
Yemwe adakonza bwino chilichonse (chomwe) adalenga. Ndipo adayambitsa chilengedwe cha munthu (Adam) kuchokera ku dongo.
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ جَعَلَ نَسۡلَهُۥ مِن سُلَٰلَةٖ مِّن مَّآءٖ مَّهِينٖ
Kenako adachita mbumba yake kuti ipangike kuchokera m’madzi enieni onyozeka.
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ سَوَّىٰهُ وَنَفَخَ فِيهِ مِن رُّوحِهِۦۖ وَجَعَلَ لَكُمُ ٱلسَّمۡعَ وَٱلۡأَبۡصَٰرَ وَٱلۡأَفۡـِٔدَةَۚ قَلِيلٗا مَّا تَشۡكُرُونَ
Kenako adamkonza ndi kuuziramo mzimu Wake. Ndipo adakuikirani kumva, kupenya ndi mitima. Kuthokoza kwanu mpang’ono ndithu.
تفسیرهای عربی:
وَقَالُوٓاْ أَءِذَا ضَلَلۡنَا فِي ٱلۡأَرۡضِ أَءِنَّا لَفِي خَلۡقٖ جَدِيدِۭۚ بَلۡ هُم بِلِقَآءِ رَبِّهِمۡ كَٰفِرُونَ
Ndipo (otsutsa kuuka ku imfa) akunena: “Kodi tikadzatayika m’nthaka (ndi kusakanikirana ndi dothi), tidzakhalanso mkalengedwe katsopano?” (Iyayi), koma iwo sakhulupirira za kukumana ndi Mbuye wawo.
تفسیرهای عربی:
۞ قُلۡ يَتَوَفَّىٰكُم مَّلَكُ ٱلۡمَوۡتِ ٱلَّذِي وُكِّلَ بِكُمۡ ثُمَّ إِلَىٰ رَبِّكُمۡ تُرۡجَعُونَ
Nena: “Adzachotsa mizimu yanu Mngelo wa imfa yemwe wapatsidwa udindo umenewu pa inu. Kenako mudzabwerera kwa Mbuye wanu.”
تفسیرهای عربی:
وَلَوۡ تَرَىٰٓ إِذِ ٱلۡمُجۡرِمُونَ نَاكِسُواْ رُءُوسِهِمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ رَبَّنَآ أَبۡصَرۡنَا وَسَمِعۡنَا فَٱرۡجِعۡنَا نَعۡمَلۡ صَٰلِحًا إِنَّا مُوقِنُونَ
Ndipo ukadawaona oipa atazolikitsa mitu yawo kwa Mbuye wawo (uku akunena): “E Mbuye wathu! Taona, ndipo tamva. Choncho tibwezeni tikachita ntchito zabwino. Ndithu tsopano tatsimikiza (kukhulupirira).”
تفسیرهای عربی:
وَلَوۡ شِئۡنَا لَأٓتَيۡنَا كُلَّ نَفۡسٍ هُدَىٰهَا وَلَٰكِنۡ حَقَّ ٱلۡقَوۡلُ مِنِّي لَأَمۡلَأَنَّ جَهَنَّمَ مِنَ ٱلۡجِنَّةِ وَٱلنَّاسِ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tikadafuna, tikadaupatsa mzimu ulionse chiongoko chake (moukakamiza monga momwe tidawachitira angelo, koma mzimu udapatsidwa mphamvu ndi ufulu wodzisankhira chimene ufuna; chabwino kapena choipa). Koma mawu atsimikizika ochokera kwa Ine: “Ndithu ndizadzazitsa Jahannam ziwanda ndi anthu; onse pamodzi (amene ali oipa).”
تفسیرهای عربی:
فَذُوقُواْ بِمَا نَسِيتُمۡ لِقَآءَ يَوۡمِكُمۡ هَٰذَآ إِنَّا نَسِينَٰكُمۡۖ وَذُوقُواْ عَذَابَ ٱلۡخُلۡدِ بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
“Choncho, lawani chifukwa cha kuyiwala (kusalabadila) kwanu kukumana ndi tsiku lanu ili. Ifenso tikusiyani (ku chilango monga ngati takuiwalani). Tero lawani chilango chamuyaya, chifukwa cha zomwe munkachita.”
تفسیرهای عربی:
إِنَّمَا يُؤۡمِنُ بِـَٔايَٰتِنَا ٱلَّذِينَ إِذَا ذُكِّرُواْ بِهَا خَرُّواْۤ سُجَّدٗاۤ وَسَبَّحُواْ بِحَمۡدِ رَبِّهِمۡ وَهُمۡ لَا يَسۡتَكۡبِرُونَ۩
Ndithu amene akukhulupirira Ayah Zathu, ndiamene akuti pamene akukumbutsidwa ndi Ayazo, amagwetsa nkhope zawo pansi (kusujudu) ndi kulemekeza Mbuye wawo pamodzi ndi kumthokoza. Ndipo iwo sadzitukumula.
تفسیرهای عربی:
تَتَجَافَىٰ جُنُوبُهُمۡ عَنِ ٱلۡمَضَاجِعِ يَدۡعُونَ رَبَّهُمۡ خَوۡفٗا وَطَمَعٗا وَمِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ يُنفِقُونَ
Nthiti zawo zimalekana ndi malo ogona (usiku), uku akumpempha Mbuye wawo, moopa ndi mwachiyembekezo. Ndipo amapereka (Zakaat ndi sadaka) mzimene tawapatsa.
تفسیرهای عربی:
فَلَا تَعۡلَمُ نَفۡسٞ مَّآ أُخۡفِيَ لَهُم مِّن قُرَّةِ أَعۡيُنٖ جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Mzimu uliwonse sudziwa zimene aubisira zotonthoza diso (zosangalatsa moyo ku Munda wa mtendere) monga mphoto pa zimene unkachita.
تفسیرهای عربی:
أَفَمَن كَانَ مُؤۡمِنٗا كَمَن كَانَ فَاسِقٗاۚ لَّا يَسۡتَوُۥنَ
Kodi yemwe ali okhulupirira angafanane ndi wotuluka m’chilamulo cha Allah? Sangafanane.
تفسیرهای عربی:
أَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ فَلَهُمۡ جَنَّٰتُ ٱلۡمَأۡوَىٰ نُزُلَۢا بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Tsono amene akhulupirira ndi kumachita zabwino, adzalandira Minda yokhalamo yokongola, monga phwando lawo pa zimene ankachita.
تفسیرهای عربی:
وَأَمَّا ٱلَّذِينَ فَسَقُواْ فَمَأۡوَىٰهُمُ ٱلنَّارُۖ كُلَّمَآ أَرَادُوٓاْ أَن يَخۡرُجُواْ مِنۡهَآ أُعِيدُواْ فِيهَا وَقِيلَ لَهُمۡ ذُوقُواْ عَذَابَ ٱلنَّارِ ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
Koma kwa amene adachita zoipa potuluka m’chilamulo cha Allah, malo awo ndi ku Moto. Nthawi iliyonse akafuna kutulukamo, azikabwezedwamo ndipo azidzauzidwa: “Lawani chilango cha Moto, chomwe munkachitsutsa.”
تفسیرهای عربی:
وَلَنُذِيقَنَّهُم مِّنَ ٱلۡعَذَابِ ٱلۡأَدۡنَىٰ دُونَ ٱلۡعَذَابِ ٱلۡأَكۡبَرِ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo ndithudi, tiwalawitsa chilango chocheperapo (pa dziko lapansi) chisanafike chilango chachikulu (cha tsiku lachimaliziro), kuti atembenuke, (alape).
تفسیرهای عربی:
وَمَنۡ أَظۡلَمُ مِمَّن ذُكِّرَ بِـَٔايَٰتِ رَبِّهِۦ ثُمَّ أَعۡرَضَ عَنۡهَآۚ إِنَّا مِنَ ٱلۡمُجۡرِمِينَ مُنتَقِمُونَ
Kodi ndani wachinyengo kwambiri, woposa yemwe akukumbutsidwa Ayah za Mbuye wake, kenako nkuzikana? Ndithu Ife, tidzawabwezera zoipa anthu oipa.
تفسیرهای عربی:
وَلَقَدۡ ءَاتَيۡنَا مُوسَى ٱلۡكِتَٰبَ فَلَا تَكُن فِي مِرۡيَةٖ مِّن لِّقَآئِهِۦۖ وَجَعَلۡنَٰهُ هُدٗى لِّبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Ndipo ndithu Mûsa tidampatsa buku. Choncho usakhale ndi chikaiko pa zakukumana Naye (Allah). Ndipo tidalichita (bukulo) kukhala chiongoko cha ana a Israyeli.
تفسیرهای عربی:
وَجَعَلۡنَا مِنۡهُمۡ أَئِمَّةٗ يَهۡدُونَ بِأَمۡرِنَا لَمَّا صَبَرُواْۖ وَكَانُواْ بِـَٔايَٰتِنَا يُوقِنُونَ
Ndipo ena mwa iwo tidawachita kukhala atsogoleri oongola (anthu) mwa lamulo lathu, pamene adapirira; ndipo adali kuvomereza motsimikiza Ayah Zathu.
تفسیرهای عربی:
إِنَّ رَبَّكَ هُوَ يَفۡصِلُ بَيۡنَهُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ فِيمَا كَانُواْ فِيهِ يَخۡتَلِفُونَ
Ndithudi Mbuye wako ndi Yemwe adzaweruze pakati pawo tsiku la Qiyâma pazimene amatsutsana.
تفسیرهای عربی:
أَوَلَمۡ يَهۡدِ لَهُمۡ كَمۡ أَهۡلَكۡنَا مِن قَبۡلِهِم مِّنَ ٱلۡقُرُونِ يَمۡشُونَ فِي مَسَٰكِنِهِمۡۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَٰتٍۚ أَفَلَا يَسۡمَعُونَ
Kodi sizidadziwike kwa iwo kuti ndimibadwo ingati imene tidaiononga patsogolo pawo; (chikhalirecho iwo) akudutsa mokhala mwawo? Ndithu m’zimenezo, muli zizindikiro, kodi sakumva?
تفسیرهای عربی:
أَوَلَمۡ يَرَوۡاْ أَنَّا نَسُوقُ ٱلۡمَآءَ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ ٱلۡجُرُزِ فَنُخۡرِجُ بِهِۦ زَرۡعٗا تَأۡكُلُ مِنۡهُ أَنۡعَٰمُهُمۡ وَأَنفُسُهُمۡۚ أَفَلَا يُبۡصِرُونَ
Kodi sakuona kuti timapereka madzi ku nthaka youma; ndipo ndi madziwo tikumeretsa mrnera umene ziweto zawo zimadya ndi iwo omwe; kodi sakupenya?
تفسیرهای عربی:
وَيَقُولُونَ مَتَىٰ هَٰذَا ٱلۡفَتۡحُ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Ndipo akunena: “Kulamulidwa kumeneku (kwa tsiku la chimaliziro) kudzachitika liti, ngati mukunenadi zoona?”
تفسیرهای عربی:
قُلۡ يَوۡمَ ٱلۡفَتۡحِ لَا يَنفَعُ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ إِيمَٰنُهُمۡ وَلَا هُمۡ يُنظَرُونَ
Nena: “Tsiku la chiweruzirolo, amene sadakhulupirire, chikhulupiriro chawo sichidzawathandiza. Ndipo sadzapatsidwa nthawi yoyembekezera (kuti mizimu yawo isachoke ayambe akhulupirira kaye, mngero wa imfa akadzawadzera).”
تفسیرهای عربی:
فَأَعۡرِضۡ عَنۡهُمۡ وَٱنتَظِرۡ إِنَّهُم مُّنتَظِرُونَ
Choncho apatuke; ndipo yembekezera (zimene Allah wakulonjeza). Ndithu nawonso akuyembekezera (zimene Allah wawalonjeza).
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: سوره سجده
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن