ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی آیه: (17) سوره: سوره نساء
إِنَّمَا ٱلتَّوۡبَةُ عَلَى ٱللَّهِ لِلَّذِينَ يَعۡمَلُونَ ٱلسُّوٓءَ بِجَهَٰلَةٖ ثُمَّ يَتُوبُونَ مِن قَرِيبٖ فَأُوْلَٰٓئِكَ يَتُوبُ ٱللَّهُ عَلَيۡهِمۡۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Ndithudi kulapa kovomerezeka ndi Allah nkwa omwe amachita zoipa mwa umbuli kenako nkulapa mwachangu. Amenewo ndiomwe Allah amawalandira kulapa kwawo. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru zakuya.[115]
[115] Ndime iyi ikusonyeza kuti Allah amalandira kulapa kuchokera kwa aliyense amene walapa. Komatu kuti kulapako kuvomerezeke, pafunika zinthu ziwiri:-
a) Akachita uchimo alape mwachangu. Osati azingopitiriza kulakwako mpaka akadzaona kuti ali pafupi kufa ndiye nkuyamba kulapa, zoterezi iyayi.
b) Uchimowo ukhale kuti adauchita chifukwa cha umbuli. Apa zikutanthauza kuti panthawiyo iye adadzazidwa ndi zilakolako za uchimo ndipo zidamchititsa kuti achimwe. Koma osati tchimolo likhale lolichita tsiku ndi tsiku popanda kulabadira chilichonse. Kulapa kwa uchimo wotero Allah sangakulandire. Ndipo mmalo mwake akamulanga ndi chilango chaukali.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی آیه: (17) سوره: سوره نساء
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن