ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی آیه: (75) سوره: سوره نساء
وَمَا لَكُمۡ لَا تُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلرِّجَالِ وَٱلنِّسَآءِ وَٱلۡوِلۡدَٰنِ ٱلَّذِينَ يَقُولُونَ رَبَّنَآ أَخۡرِجۡنَا مِنۡ هَٰذِهِ ٱلۡقَرۡيَةِ ٱلظَّالِمِ أَهۡلُهَا وَٱجۡعَل لَّنَا مِن لَّدُنكَ وَلِيّٗا وَٱجۡعَل لَّنَا مِن لَّدُنكَ نَصِيرًا
Mwatani inu osamenyana pa njira ya Allah, ndi (kuwapulumutsa) omwe ali ofooka, aamuna ndi aakazi ndi ana, omwe akunena: “Mbuye wathu! Titulutseni m’mudzi uwu omwe anthu ake ndiopondereza; ndipo tipatseni mtetezi wochokera kwa Inu; ndiponso tipatseni mthandizi wochokera kwa Inu.”[133]
[133] Pamene Mtumiki (s.a.w) adasamuka ku Makka kukakhala ku Madina, Asilamu ena aamuna ndi aakazi adatsalira ku Makka chifukwa chakuti abale awo adawaletsa. Ndipo chifukwa chakufooka kwawo sadathe kuthawa mozemba namangokhala konko ku Makka akuwachitira zoipa zambiri ndi kumawanyoza. Choncho Asilamu adawauza kuti ngati kuzakhale kololezedwa kuchita nawo nkhondo Aquraish a m’Makka adzamenyane nawo Aquraishwo molimba kufikira adzawapulumutse. Asilamu adakwaniritsa lonjezolo. Adamenya nkhondo mpaka kugonjetsa mzinda wa Makka ndi kuwapulumutsa anzawo amene adali kupempha Allah kwa nthawi yaitali kuti awapulumutse ku anthu oipa.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی آیه: (75) سوره: سوره نساء
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن