ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی آیه: (1) سوره: سوره توبه

سوره توبه

بَرَآءَةٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦٓ إِلَى ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّم مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Uku ndikudzipatula kochokera kwa Allah ndi Mtumiki wake ku (mapangano) amene mudapangana nawo (kenako nkuswa mapangano awowo) a m’gulu la Amushirikina.[204]
[204] (Ndime 1-2) Omasulila Qur’an adati Arabu adali kuswa mapangano amene adamanga pamodzi ndi Mtumiki wa Allah. Potero, Allah adalamula Mtumiki Wake kuti awaponyere mapangano awo. Choncho, Mtumiki adatuma Abubakari (r.a) kukhala mtsogoleri wa anthu kumapemphero a Hajj. Ndipo adamtsatanso Ali (r.a) kumeneko ndi nkhani yokhayokhayo kuti akawawerengere anthu kuti Allah ndi Mtumiki Wake atulukamo m’mapangano okhalirana mwa mtendere ndi Amushirikina sadzaloledwa kuyandikira Nyumba Yopatulika chaka chotsatiracho, ndikutinso sadzaloledwa kuzungulira Nyumba yopatulikayo uku ali maliseche.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی آیه: (1) سوره: سوره توبه
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن