Check out the new design

કુરઆન મજીદના શબ્દોનું ભાષાંતર - ચિચેવા ભાષામાં અનુવાદ - ખાલિદ ઇબ્રાહિમ બૈતાલા * - ભાષાંતરોની અનુક્રમણિકા


શબ્દોનું ભાષાંતર સૂરહ: અત્ તગાબુન   આયત:

At-Tâghabun

يُسَبِّحُ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۖ لَهُ ٱلۡمُلۡكُ وَلَهُ ٱلۡحَمۡدُۖ وَهُوَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ
Zonse zakumwamba ndi zam’dziko lapansi zikulemekeza Allah (ndi kumyeretsa ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero Wake; ufumu Ngwake ndipo kutamandidwa kwabwino Nkwake. Ndipo Iye ali ndi mphamvu pa chilichonse.
અરબી તફસીરો:
هُوَ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ فَمِنكُمۡ كَافِرٞ وَمِنكُم مُّؤۡمِنٞۚ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٌ
Iye ndiamene adakulengani (nonsenu popanda kuchokera ku chilichonse) choncho mwa inu alipo wosakhulupirira ndiponso mwa inu alipo wokhulupirira. Ndipo Allah Ngopenya zonse zimene mukuchita (ndipo adzakulipirani nazo).
અરબી તફસીરો:
خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ بِٱلۡحَقِّ وَصَوَّرَكُمۡ فَأَحۡسَنَ صُوَرَكُمۡۖ وَإِلَيۡهِ ٱلۡمَصِيرُ
Adalenga thambo ndi nthaka mwachoonadi ndipo adakujambulani majambulidwe abwino; ndipo kobwerera nkwa Iye (pa tsiku lachiweruziro).
અરબી તફસીરો:
يَعۡلَمُ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَيَعۡلَمُ مَا تُسِرُّونَ وَمَا تُعۡلِنُونَۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ
(Allah) akudziwa za kumwamba ndi za m’dziko lapansi, ndiponso akudziwa zimene mukuzibisa ndi zimene mukuzilengeza (zochita ndi zoyankhula); Allah Ngodziwa za m’zifuwa.
અરબી તફસીરો:
أَلَمۡ يَأۡتِكُمۡ نَبَؤُاْ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَبۡلُ فَذَاقُواْ وَبَالَ أَمۡرِهِمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Kodi siidakufikeni nkhani ya omwe sadakhulupirire kale? Adalawa (zowawa) za zoipa za zinthu zawo (pa dziko lapansi). Ndipo chilango chowawa chidzakhala pa iwo (tsiku lachimaliziro).
અરબી તફસીરો:
ذَٰلِكَ بِأَنَّهُۥ كَانَت تَّأۡتِيهِمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ فَقَالُوٓاْ أَبَشَرٞ يَهۡدُونَنَا فَكَفَرُواْ وَتَوَلَّواْۖ وَّٱسۡتَغۡنَى ٱللَّهُۚ وَٱللَّهُ غَنِيٌّ حَمِيدٞ
Zimenezo nchifukwa chakuti atumiki awo amawadzera ndi zozizwitsa koma iwo amanena (mwachipongwe): “Ha! Anthu anzathu (onga ife) angationgole?” Choncho sadakhulupirire (utumiki wawo) ndipo adanyoza (choonadi) potero Allah adawasiya (ndi kupanda chikhulupiliro kwawo) ndipo Allah Ngokwanira ndiponso Ngoyamikidwa.
અરબી તફસીરો:
زَعَمَ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ أَن لَّن يُبۡعَثُواْۚ قُلۡ بَلَىٰ وَرَبِّي لَتُبۡعَثُنَّ ثُمَّ لَتُنَبَّؤُنَّ بِمَا عَمِلۡتُمۡۚ وَذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٞ
Amene sadakhulupirire akumazinamiza kuti sadzaukitsidwa ku imfa. Nena (kwa iwo iwe Mtumiki{s.a.w}): “Sizili choncho pali Mbuye wanga, ndithu mudzaukitsidwa ku imfa, ndipo mudzauzidwa zimene mumachita (pa dziko lapansi). Zimenezo kwa Allah nzosavuta (kuzichita).”
અરબી તફસીરો:
فَـَٔامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَٱلنُّورِ ٱلَّذِيٓ أَنزَلۡنَاۚ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٞ
Khulupirirani Allah ndi Mtumiki Wake, ndi dangalira limene talivumbulutsa (Qur’an). Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita.
અરબી તફસીરો:
يَوۡمَ يَجۡمَعُكُمۡ لِيَوۡمِ ٱلۡجَمۡعِۖ ذَٰلِكَ يَوۡمُ ٱلتَّغَابُنِۗ وَمَن يُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ وَيَعۡمَلۡ صَٰلِحٗا يُكَفِّرۡ عَنۡهُ سَيِّـَٔاتِهِۦ وَيُدۡخِلۡهُ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
(Kumbukirani) tsiku limene adzakusonkhanitsani chifukwa cha tsiku lakusonkhana (zolengedwa zonse), limenelo ndi tsiku lolephera; ndipo amene akhulupirira mwa Allah ndi kuchita zabwino, amfafanizira zoipa zake, ndipo akamulowetsa m’minda momwe pansi pake pakuyenda mitsinje; adzakhala m’menemo muyaya; kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.[365]
[365] Tsiku lolephera: Akafiri adzakhala olephera chifukwa cha kusakhulupilira kwawo. Nawonso Asilamu aulesi adzakhala olephera chifukwa cha kusakwaniritsa kwawo malamulo a Allah.
અરબી તફસીરો:
 
શબ્દોનું ભાષાંતર સૂરહ: અત્ તગાબુન
સૂરહ માટે અનુક્રમણિકા પેજ નંબર
 
કુરઆન મજીદના શબ્દોનું ભાષાંતર - ચિચેવા ભાષામાં અનુવાદ - ખાલિદ ઇબ્રાહિમ બૈતાલા - ભાષાંતરોની અનુક્રમણિકા

તેનું અનુવાદ ખાલીદ ઈબ્રાહીમ બૈતાલા દ્વારા કરવામાં આવ્યું.

બંધ કરો