Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Sura: Suratu Al'nasr   Aya:

Suratu Al'nasr

إِذَا جَآءَ نَصۡرُ ٱللَّهِ وَٱلۡفَتۡحُ
Chikafika chipulumutso cha Allah ndi kugonjetsa (mzinda wa Makka kwa iwe ndi okutsatira),[494]
[494] Ili ndi lonjezo la Allah kwa Mneneri wake (Muhammad) (s.a.w) kuti amthandiza kumpulumutsa kwa adani ake amene adali kumuzunza ndi kufuna kumupha. Lonjezoli lidali lakuti iye adzaulamulira mzinda wa adaniwo momwe adamutulutsa.
Tafsiran larabci:
وَرَأَيۡتَ ٱلنَّاسَ يَدۡخُلُونَ فِي دِينِ ٱللَّهِ أَفۡوَاجٗا
Ndikuwaona anthu akulowa m’chipembedzo cha Allah ali magulumagulu,[495]
[495] Mneneri (s.a.w) pamene adalowa mu mzinda wa Makka ndi kugonjetsa adani ake monga momwe Allah adamulonjezera, a kafiri adali kubwera m’mafukomafuko kudzalowa m’chipembedzo cha Chisilamu.
Tafsiran larabci:
فَسَبِّحۡ بِحَمۡدِ رَبِّكَ وَٱسۡتَغۡفِرۡهُۚ إِنَّهُۥ كَانَ تَوَّابَۢا
Pamenepo lemekeza Mbuye wako ndi kumtamanda ndiponso mpemphe chikhululuko, ndipo ndithu Iye ndiwolandira mochuluka kulapa (kwa anthu Ake).[496]
[496] Tanthauzo la kuuzidwa Mneneri Muhammad (s.a.w) kuti zikachitika zimene adalonjezedwa, amulemekeze Mbuye wake, amupemphe chikhululuko, chikhalirecho iye adali kuchita zimenezo, izi zimatanthauza kuti moyo wake wayandikira kutha, watsala pang’ono kumwalira. Choncho adalamulidwa kuonjezera mapemphero kuti aonjezere kulinganiza tsiku lake lomaliza. Imeneyi ndi imodzi mwa Surah zimene zidavumbulutsidwa kotsirizira kwa moyo wa Mtumiki (s.a.w). Pamene idavumbulutsidwa Surayi, ena mwa maswahaba (omutsatira) adazindikira chinsinsi cha Surayi; adali kulira poona kuti Mneneri (s.a.w) amwalira posachedwa. Pambuyo povumbulutsidwa Surayi, Mneneri (s.a.w) sadakhale moyo nthawi yaitali.
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Sura: Suratu Al'nasr
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassarar Maanonin Alurani mai girma zuwa Yaren shishiwa wanda Khalid Ibrahim Bitala kwafi na Shekarar 2020 Miladiyya

Rufewa