Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura An-Nasr   Versículo:

Sura An-Nasr

إِذَا جَآءَ نَصۡرُ ٱللَّهِ وَٱلۡفَتۡحُ
Chikafika chipulumutso cha Allah ndi kugonjetsa (mzinda wa Makka kwa iwe ndi okutsatira),[494]
[494] Ili ndi lonjezo la Allah kwa Mneneri wake (Muhammad) (s.a.w) kuti amthandiza kumpulumutsa kwa adani ake amene adali kumuzunza ndi kufuna kumupha. Lonjezoli lidali lakuti iye adzaulamulira mzinda wa adaniwo momwe adamutulutsa.
Las Exégesis Árabes:
وَرَأَيۡتَ ٱلنَّاسَ يَدۡخُلُونَ فِي دِينِ ٱللَّهِ أَفۡوَاجٗا
Ndikuwaona anthu akulowa m’chipembedzo cha Allah ali magulumagulu,[495]
[495] Mneneri (s.a.w) pamene adalowa mu mzinda wa Makka ndi kugonjetsa adani ake monga momwe Allah adamulonjezera, a kafiri adali kubwera m’mafukomafuko kudzalowa m’chipembedzo cha Chisilamu.
Las Exégesis Árabes:
فَسَبِّحۡ بِحَمۡدِ رَبِّكَ وَٱسۡتَغۡفِرۡهُۚ إِنَّهُۥ كَانَ تَوَّابَۢا
Pamenepo lemekeza Mbuye wako ndi kumtamanda ndiponso mpemphe chikhululuko, ndipo ndithu Iye ndiwolandira mochuluka kulapa (kwa anthu Ake).[496]
[496] Tanthauzo la kuuzidwa Mneneri Muhammad (s.a.w) kuti zikachitika zimene adalonjezedwa, amulemekeze Mbuye wake, amupemphe chikhululuko, chikhalirecho iye adali kuchita zimenezo, izi zimatanthauza kuti moyo wake wayandikira kutha, watsala pang’ono kumwalira. Choncho adalamulidwa kuonjezera mapemphero kuti aonjezere kulinganiza tsiku lake lomaliza. Imeneyi ndi imodzi mwa Surah zimene zidavumbulutsidwa kotsirizira kwa moyo wa Mtumiki (s.a.w). Pamene idavumbulutsidwa Surayi, ena mwa maswahaba (omutsatira) adazindikira chinsinsi cha Surayi; adali kulira poona kuti Mneneri (s.a.w) amwalira posachedwa. Pambuyo povumbulutsidwa Surayi, Mneneri (s.a.w) sadakhale moyo nthawi yaitali.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura An-Nasr
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar