Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Kaafiroon   Versículo:

Sura Al-Kaafiroon

قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡكَٰفِرُونَ
Nena (iwe Mtumiki) (s.a.w): E inu anthu osakhulupirira![493]
[493] (Ndime 1-6) Osakhulupilira a mu mzinda wa Makka pamene adaona kuti atopa, sangathe kuzimitsa dangalira la Usilamu ndipo adamuona Mneneri (s.a.w) tsiku lililonse akuonjezera khama pa ntchito yake, chipembedzo nacho chikunkerankera mtsogolo, adapempha Muhammad (s.a.w) kuti pakhale chimvano pakati pa iwo ndi iye choti amupembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w) chaka chimodzi pamodzi naye, nayenso pa chaka chinacho asakanikirane nawo popembedza milungu yawo chaka chimodzinso. Kumeneku ndiko kuti chaka, apembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w), nayenso apembedze milungu yawo chaka chinacho. Apa ndipo pamene idavumbulutsidwa Surayi. Cholinga chake ndi ichi: Inu muli ndi milungu yanu, inenso ndili ndi Mulungu wanga. Sizingatheke kusakanikirana pakati pa milungu yanu yonama ndi Mulungu wanga woona, ngakhalenso ndi mapemphero anu onama ndi mapemphero anga owona. Inu muli ndi chipembedzo ndichikhulupiliro chanu, inenso ndili ndi chipembedzo ndi chikhulupiliro changa.
Las Exégesis Árabes:
لَآ أَعۡبُدُ مَا تَعۡبُدُونَ
Sindipembedza chimene inu mukuchipembedza (kusiya Allah).
Las Exégesis Árabes:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Inunso simumpembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Las Exégesis Árabes:
وَلَآ أَنَا۠ عَابِدٞ مَّا عَبَدتُّمۡ
Ndiponso ine sindidzapembedza chimene inu mwakhala mukuchipembedza (chifukwa inu ndinu ophatikiza Allah ndi zinthu zina).
Las Exégesis Árabes:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Ndipo inu simudzampembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Las Exégesis Árabes:
لَكُمۡ دِينُكُمۡ وَلِيَ دِينِ
Inu muli ndi chipembedzo chanu (chimene mukuchikhulupirira), inenso ndili ndi chipembedzo changa (chimene Allah wandisankhira).
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Kaafiroon
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar