Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Masad   Versículo:

Sura Al-Masad

تَبَّتۡ يَدَآ أَبِي لَهَبٖ وَتَبَّ
Aonongeka manja a Abi Lahab (omwe adali kuwagwiritsa ntchito pozunza Asilamu). Nayenso wawonongeka.[497]
[497] (Ndime 1-4) Pa chiyambi cha uneneri wa Muhammad (s.a.w) adalamulidwa kuti aulalikire uthenga wabwinowo kwa abale ake apafupi; adawasonkhanitsa ndipo adawalalikira ndi kuwachenjeza za chilango cha tsiku lachimaliziro. Koma Abu Lahab adali m’bale watate wa Mtumiki Muhammad (s.a.w) adakwiya ndipo adanena kuti: “Waonongeka iwe! Waonongeka iwe! Chimenechi ndi chimene watisonkhanitsira?’’ Pa chifukwa ichi idavumbulutsidwa Sura imeneyi. Allah adamubwezera Abu Lahab pamodzi ndi mkazi wake, Ummu Jamil, mawu otembelera. Ummu Jamil ankalimbikira kwambiri kumuzunza Mtumiki (s.a.w) ndi kuwakaikitsa amuna kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti Chisilamu chisafalikire madera ena. “Aonongeka manja a Abu Lahab’’ kumeneku ndi kutembelera komutembelera Abu Lahab kuti aonongeke m’malo moonongeka Mneneri (s.a.w). Pakuti amene amatembelera apayu ndi Mwini Allah, ndiye kuti matembelero adamufikiradi iye.
Las Exégesis Árabes:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُ مَالُهُۥ وَمَا كَسَبَ
Chuma chake ndi ulemelero wake (umene adaupeza) sizidamthandize ku chilango cha Allah.
Las Exégesis Árabes:
سَيَصۡلَىٰ نَارٗا ذَاتَ لَهَبٖ
Adzalowa ku Moto wa malawi.
Las Exégesis Árabes:
وَٱمۡرَأَتُهُۥ حَمَّالَةَ ٱلۡحَطَبِ
Nayenso mkazi wake (adzalowa ku Moto) yemwe adali kusenza nkhuni (za minga pomutchera Mtumiki (s.a.w) komanso amanka nadanitsa pakati pa anthu).
Las Exégesis Árabes:
فِي جِيدِهَا حَبۡلٞ مِّن مَّسَدِۭ
Mkhosi mwake mdzamangidwa chingwe chopiringidwa bwino cha mlaza (chomlanga nacho).[498]
[498] Uyu mkazi wa Abu Lahab adali wodanitsa. Ntchito yake idali kutapa mawu uku, kuwapititsa uku, ncholinga chofuna kusokoneza.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Masad
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar