क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद * - अनुवादों की सूची


अर्थों का अनुवाद सूरा: सूरा अल्-मसद   आयत:

सूरा अल्-मसद

تَبَّتۡ يَدَآ أَبِي لَهَبٖ وَتَبَّ
Aonongeka manja a Abi Lahab (omwe adali kuwagwiritsa ntchito pozunza Asilamu). Nayenso wawonongeka.[497]
[497] (Ndime 1-4) Pa chiyambi cha uneneri wa Muhammad (s.a.w) adalamulidwa kuti aulalikire uthenga wabwinowo kwa abale ake apafupi; adawasonkhanitsa ndipo adawalalikira ndi kuwachenjeza za chilango cha tsiku lachimaliziro. Koma Abu Lahab adali m’bale watate wa Mtumiki Muhammad (s.a.w) adakwiya ndipo adanena kuti: “Waonongeka iwe! Waonongeka iwe! Chimenechi ndi chimene watisonkhanitsira?’’ Pa chifukwa ichi idavumbulutsidwa Sura imeneyi. Allah adamubwezera Abu Lahab pamodzi ndi mkazi wake, Ummu Jamil, mawu otembelera. Ummu Jamil ankalimbikira kwambiri kumuzunza Mtumiki (s.a.w) ndi kuwakaikitsa amuna kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti Chisilamu chisafalikire madera ena. “Aonongeka manja a Abu Lahab’’ kumeneku ndi kutembelera komutembelera Abu Lahab kuti aonongeke m’malo moonongeka Mneneri (s.a.w). Pakuti amene amatembelera apayu ndi Mwini Allah, ndiye kuti matembelero adamufikiradi iye.
अरबी तफ़सीरें:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُ مَالُهُۥ وَمَا كَسَبَ
Chuma chake ndi ulemelero wake (umene adaupeza) sizidamthandize ku chilango cha Allah.
अरबी तफ़सीरें:
سَيَصۡلَىٰ نَارٗا ذَاتَ لَهَبٖ
Adzalowa ku Moto wa malawi.
अरबी तफ़सीरें:
وَٱمۡرَأَتُهُۥ حَمَّالَةَ ٱلۡحَطَبِ
Nayenso mkazi wake (adzalowa ku Moto) yemwe adali kusenza nkhuni (za minga pomutchera Mtumiki (s.a.w) komanso amanka nadanitsa pakati pa anthu).
अरबी तफ़सीरें:
فِي جِيدِهَا حَبۡلٞ مِّن مَّسَدِۭ
Mkhosi mwake mdzamangidwa chingwe chopiringidwa bwino cha mlaza (chomlanga nacho).[498]
[498] Uyu mkazi wa Abu Lahab adali wodanitsa. Ntchito yake idali kutapa mawu uku, kuwapititsa uku, ncholinga chofuna kusokoneza.
अरबी तफ़सीरें:
 
अर्थों का अनुवाद सूरा: सूरा अल्-मसद
सूरों की सूची पृष्ठ संख्या
 
क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - अनुवादों की सूची

पवित्र क़ुरआन के अर्थों का चेवा अनुवाद। अनुवाद ख़ालिद अबराहीम बेताला ने किया है। प्रति वर्ष 2020 ईसवी।

बंद करें