Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Aya: (238) Sura: Suratu Al'bakara
حَٰفِظُواْ عَلَى ٱلصَّلَوَٰتِ وَٱلصَّلَوٰةِ ٱلۡوُسۡطَىٰ وَقُومُواْ لِلَّهِ قَٰنِتِينَ
Sungani mokwanira Swala makamaka Swala yapakatikati; ndipo imilirani modzichepetsa kwa Allah.[41]
[41] M’ndime iyi akulimbikitsa kuti Swala zonse anthu azipemphere muunyinji wawo osati munthu payekhapayekha makamaka Swala yapakatikati. Ena mwa maulama adati Swala yapakatikati ndi Swala ya Dhuhr. Imapempheredwa pakatikati pamasana, dzuwa litatentha kwambiri monga momwe zilili m’maiko a Arabu. Pa Swala ya Dhuhr anthu amavutika kwambiri kukapemphera m’misikiti chifukwa chakutentha kwa dzuwa. Choncho apa akuwalimbikitsa kuti azikapemphera m’misikiti ngakhale kuli kotentha. Pomwe ena akuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Fajiri (Subuh) imene imapempheredwa pakatikati panthawi. Simasana ndiponso siusiku. Apa mpanthawi pomwe tulo timakhala tamphamvu. Tero akuwalimbikitsa anthu kusiya tuloto nkupita ku misikiti nkukapemphera Swala ya (jama) yapagulu. Ndipo akutilimbikitsanso kuti tizipemphera mofatsira ndi modzichepetsa. Ndikuti tikamapemphera tizidziwa kuti taimilira pamaso pa Allah. Komanso ma hadith ena atchula zakuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Asr.
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Aya: (238) Sura: Suratu Al'bakara
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassarar Maanonin Alurani mai girma zuwa Yaren shishiwa wanda Khalid Ibrahim Bitala kwafi na Shekarar 2020 Miladiyya

Rufewa