Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (238) Sourate: AL-BAQARAH
حَٰفِظُواْ عَلَى ٱلصَّلَوَٰتِ وَٱلصَّلَوٰةِ ٱلۡوُسۡطَىٰ وَقُومُواْ لِلَّهِ قَٰنِتِينَ
Sungani mokwanira Swala makamaka Swala yapakatikati; ndipo imilirani modzichepetsa kwa Allah.[41]
[41] M’ndime iyi akulimbikitsa kuti Swala zonse anthu azipemphere muunyinji wawo osati munthu payekhapayekha makamaka Swala yapakatikati. Ena mwa maulama adati Swala yapakatikati ndi Swala ya Dhuhr. Imapempheredwa pakatikati pamasana, dzuwa litatentha kwambiri monga momwe zilili m’maiko a Arabu. Pa Swala ya Dhuhr anthu amavutika kwambiri kukapemphera m’misikiti chifukwa chakutentha kwa dzuwa. Choncho apa akuwalimbikitsa kuti azikapemphera m’misikiti ngakhale kuli kotentha. Pomwe ena akuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Fajiri (Subuh) imene imapempheredwa pakatikati panthawi. Simasana ndiponso siusiku. Apa mpanthawi pomwe tulo timakhala tamphamvu. Tero akuwalimbikitsa anthu kusiya tuloto nkupita ku misikiti nkukapemphera Swala ya (jama) yapagulu. Ndipo akutilimbikitsanso kuti tizipemphera mofatsira ndi modzichepetsa. Ndikuti tikamapemphera tizidziwa kuti taimilira pamaso pa Allah. Komanso ma hadith ena atchula zakuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Asr.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (238) Sourate: AL-BAQARAH
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture