Check out the new design

Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fassara da harshan Shishiyo - Khalid Ibrahim Bitala * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Sura: Al'safat   Aya:
فَكَذَّبُوهُ فَإِنَّهُمۡ لَمُحۡضَرُونَ
Koma adamtsutsa; ndithu iwo adzaonekera (ku Moto).
Tafsiran larabci:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Kupatula akapolo a Allah amene ayeretsedwa (ndi Allah).
Tafsiran larabci:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
Tafsiran larabci:
سَلَٰمٌ عَلَىٰٓ إِلۡ يَاسِينَ
Mtendere ukhale pa Iliyasiin!
Tafsiran larabci:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umo ndi mmene Ife timawalipirira ochita zabwino.
Tafsiran larabci:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye ndimmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
Tafsiran larabci:
وَإِنَّ لُوطٗا لَّمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndithu Luti ndi mmodzi wa atumiki.
Tafsiran larabci:
إِذۡ نَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
(Kumbuka) pamene tidampulumutsa iye ndi anthu ake onse.
Tafsiran larabci:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yachikazi; idali mwa otsalira.
Tafsiran larabci:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawaononga enawo (omwe adali oipa).
Tafsiran larabci:
وَإِنَّكُمۡ لَتَمُرُّونَ عَلَيۡهِم مُّصۡبِحِينَ
Ndithu inu (a mumzinda wa Makka) mumadutsa pa malo pawopo m’mawa,
Tafsiran larabci:
وَبِٱلَّيۡلِۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Ndi usiku. Kodi bwanji simuzindikira?
Tafsiran larabci:
وَإِنَّ يُونُسَ لَمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndithu Yunusu ndi mmodzi wa atumiki.
Tafsiran larabci:
إِذۡ أَبَقَ إِلَى ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
(Kumbuka) pamene adathawira m’chombo chodzazidwa (ndi katundu).
Tafsiran larabci:
فَسَاهَمَ فَكَانَ مِنَ ٱلۡمُدۡحَضِينَ
Choncho adachita mayere, ndipo adali m’gulu la omgwera (mayerewo).
Tafsiran larabci:
فَٱلۡتَقَمَهُ ٱلۡحُوتُ وَهُوَ مُلِيمٞ
Choncho nsomba idammeza uku ali wodzudzulidwa.
Tafsiran larabci:
فَلَوۡلَآ أَنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلۡمُسَبِّحِينَ
Kukadapanda kuti iye adali m’modzi mwa otamanda ndi kulemekeza Allah).
Tafsiran larabci:
لَلَبِثَ فِي بَطۡنِهِۦٓ إِلَىٰ يَوۡمِ يُبۡعَثُونَ
Akadakhala m’mimba mwake mpaka tsiku loukitsidwa (zolengedwa ku imfa).
Tafsiran larabci:
۞ فَنَبَذۡنَٰهُ بِٱلۡعَرَآءِ وَهُوَ سَقِيمٞ
Koma tidamponya pa gombe uku ali wodwala.
Tafsiran larabci:
وَأَنۢبَتۡنَا عَلَيۡهِ شَجَرَةٗ مِّن يَقۡطِينٖ
Ndipo tidammeretsera mmera wa mtundu wa nkhaka.
Tafsiran larabci:
وَأَرۡسَلۡنَٰهُ إِلَىٰ مِاْئَةِ أَلۡفٍ أَوۡ يَزِيدُونَ
Ndipo (atachira) tidamtuma ku anthu okwana zikwi zana limodzi (100,000) kapena kupambana apa.
Tafsiran larabci:
فَـَٔامَنُواْ فَمَتَّعۡنَٰهُمۡ إِلَىٰ حِينٖ
Ndipo adakhulupirira (ndi kuvomereza ulaliki wake); choncho tidawapatsa chisangalalo kufikira nthawi (ya imfa yawo).
Tafsiran larabci:
فَٱسۡتَفۡتِهِمۡ أَلِرَبِّكَ ٱلۡبَنَاتُ وَلَهُمُ ٱلۡبَنُونَ
Choncho afunse: “Kodi Mbuye wako ndiye woyenera ana aakazi, ndipo iwo aamuna? (Pomwe iwo akabereka mwana wamkazi amanyansidwa naye)!”
Tafsiran larabci:
أَمۡ خَلَقۡنَا ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ إِنَٰثٗا وَهُمۡ شَٰهِدُونَ
Kapena kuti tidalenga angelo kukhala akazi, iwo akuona?
Tafsiran larabci:
أَلَآ إِنَّهُم مِّنۡ إِفۡكِهِمۡ لَيَقُولُونَ
Chenjera ndi bodza lawolo, ndithu iwo akunena:
Tafsiran larabci:
وَلَدَ ٱللَّهُ وَإِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
“Allah wabereka.” Ndithu iwo ndi abodza.
Tafsiran larabci:
أَصۡطَفَى ٱلۡبَنَاتِ عَلَى ٱلۡبَنِينَ
Kodi Iye adasankha ana aakazi kusiya aamuna?
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Sura: Al'safat
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fassara da harshan Shishiyo - Khalid Ibrahim Bitala - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassararta Khalid Ibrahim Bitala.

Rufewa