Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Aya: (53) Sura: Suratu Al'nisaa
أَمۡ لَهُمۡ نَصِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُلۡكِ فَإِذٗا لَّا يُؤۡتُونَ ٱلنَّاسَ نَقِيرًا
Kodi ali ndi gawo la ufumu (wa Allah? Nchifukwa ninji akunyasidwa munthu wina akaninkhidwa utumiki)? Zikadatero ndiye kuti sakadawapatsa anthu ngakhale kochepa kwambiri monga khokho la tende.[128]
[128] Ndime 53-54 zikusonyeza kuti zonse zimene Ayuda ankawachitira Asilamu nchifukwa chadumbo basi. Ankawawidwa nawo mitima chifukwa choti Asilamu apeza chisomo cha Allah. Palibe chinthu chimene chimaletsa anthu kutsata choonadi kuposa dumbo. Ngati utamchitira dumbo munthu sungalole kutsata langizo lake lililonse ngakhale litakhala lopindulitsa pano pa dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro Dumbo ndi lomwe likuletsa anthu ambiri kutsata choonadi. Choncho tiyeni tipewe khalidwe limeneli kuti titsatire choonadi paliponse pamene chachokera. Ndikutinso tipeze mtendere m’mitima mwathu. Dziwani kuti dumbo nlomwe lidamchititsa Iblis kukhala wotembeleredwa.
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Aya: (53) Sura: Suratu Al'nisaa
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassarar Maanonin Alurani mai girma zuwa Yaren shishiwa wanda Khalid Ibrahim Bitala kwafi na Shekarar 2020 Miladiyya

Rufewa