Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 段: (53) 章: 尼萨仪
أَمۡ لَهُمۡ نَصِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُلۡكِ فَإِذٗا لَّا يُؤۡتُونَ ٱلنَّاسَ نَقِيرًا
Kodi ali ndi gawo la ufumu (wa Allah? Nchifukwa ninji akunyasidwa munthu wina akaninkhidwa utumiki)? Zikadatero ndiye kuti sakadawapatsa anthu ngakhale kochepa kwambiri monga khokho la tende.[128]
[128] Ndime 53-54 zikusonyeza kuti zonse zimene Ayuda ankawachitira Asilamu nchifukwa chadumbo basi. Ankawawidwa nawo mitima chifukwa choti Asilamu apeza chisomo cha Allah. Palibe chinthu chimene chimaletsa anthu kutsata choonadi kuposa dumbo. Ngati utamchitira dumbo munthu sungalole kutsata langizo lake lililonse ngakhale litakhala lopindulitsa pano pa dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro Dumbo ndi lomwe likuletsa anthu ambiri kutsata choonadi. Choncho tiyeni tipewe khalidwe limeneli kuti titsatire choonadi paliponse pamene chachokera. Ndikutinso tipeze mtendere m’mitima mwathu. Dziwani kuti dumbo nlomwe lidamchititsa Iblis kukhala wotembeleredwa.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (53) 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭