Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Ayah: (3) Surah: Surah An-Naṣr
فَسَبِّحۡ بِحَمۡدِ رَبِّكَ وَٱسۡتَغۡفِرۡهُۚ إِنَّهُۥ كَانَ تَوَّابَۢا
Pamenepo lemekeza Mbuye wako ndi kumtamanda ndiponso mpemphe chikhululuko, ndipo ndithu Iye ndiwolandira mochuluka kulapa (kwa anthu Ake).[496]
[496] Tanthauzo la kuuzidwa Mneneri Muhammad (s.a.w) kuti zikachitika zimene adalonjezedwa, amulemekeze Mbuye wake, amupemphe chikhululuko, chikhalirecho iye adali kuchita zimenezo, izi zimatanthauza kuti moyo wake wayandikira kutha, watsala pang’ono kumwalira. Choncho adalamulidwa kuonjezera mapemphero kuti aonjezere kulinganiza tsiku lake lomaliza. Imeneyi ndi imodzi mwa Surah zimene zidavumbulutsidwa kotsirizira kwa moyo wa Mtumiki (s.a.w). Pamene idavumbulutsidwa Surayi, ena mwa maswahaba (omutsatira) adazindikira chinsinsi cha Surayi; adali kulira poona kuti Mneneri (s.a.w) amwalira posachedwa. Pambuyo povumbulutsidwa Surayi, Mneneri (s.a.w) sadakhale moyo nthawi yaitali.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Ayah: (3) Surah: Surah An-Naṣr
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup