Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Ayah: (255) Surah: Surah Al-Baqarah
ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلۡحَيُّ ٱلۡقَيُّومُۚ لَا تَأۡخُذُهُۥ سِنَةٞ وَلَا نَوۡمٞۚ لَّهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ مَن ذَا ٱلَّذِي يَشۡفَعُ عِندَهُۥٓ إِلَّا بِإِذۡنِهِۦۚ يَعۡلَمُ مَا بَيۡنَ أَيۡدِيهِمۡ وَمَا خَلۡفَهُمۡۖ وَلَا يُحِيطُونَ بِشَيۡءٖ مِّنۡ عِلۡمِهِۦٓ إِلَّا بِمَا شَآءَۚ وَسِعَ كُرۡسِيُّهُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَۖ وَلَا يَـُٔودُهُۥ حِفۡظُهُمَاۚ وَهُوَ ٱلۡعَلِيُّ ٱلۡعَظِيمُ
Allah palibe wopembedzedwa wina koma Iye, Wamoyo wamuyaya, Woimira ndi Woteteza chilichonse. Kusinza sikumgwira ngakhale tulo. Zonse za kumwamba ndi za pansi nza Iye. Kodi ndani angathe kuombola kwa Iye popanda chilolezo chake? Akudziwa za patsogolo ndi zomwe zili pambuyo pawo ndipo zolengedwazo sizidziwa chilichonse pa zomwe zili m’kudziwa Kwake kupatula chimene wafuna. Mpando wake wachifumu wakwanira kumwamba ndi pansi ndipo sizimamvuta kuzisunga zimenezo. Ndipo Iye (Yekha) Njemwe ali Wapamwambamwamba, Ngwamkulu kwabasi, (Ngolemekezeka kwambiri).[48]
[48] Ndime iyi ikutchedwa Ayat Kursii; ndime yolemekezeka kwambiri. Kwa msilamu aliyense nkofunika kuizindikira bwinobwino ndimeyi kuti azindikire kuti palibe yemwe angamuike patsogolo kapena pambuyo koma lye Allah wapamwambamwamba. Mu hadisi zambiri za Mtumiki akutilimbikitsa kuiwerenga ndimeyi m’malo awa:-
a) tikatha kuchita salamu pa Swala iliyonse ya Faradh
b) tisanagone
c) pamene tikutuluka m’nyumba
d) polowa m’nyumba
e) tikadzazidwa ndi mantha poopa chinthu chomwe tikuchiona ndi chomwe sitikuchiona
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Ayah: (255) Surah: Surah Al-Baqarah
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup