Check out the new design

Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Khalid Ibrahim Betala * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Āli 'Imrān   Ayah:
وَلِيُمَحِّصَ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَيَمۡحَقَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
(Izi) nkuti Allah awayeretse amene akhulupirira ndikuwathetseratu osakhulupirira.
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ حَسِبۡتُمۡ أَن تَدۡخُلُواْ ٱلۡجَنَّةَ وَلَمَّا يَعۡلَمِ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ جَٰهَدُواْ مِنكُمۡ وَيَعۡلَمَ ٱلصَّٰبِرِينَ
Kodi mukuganiza kuti mukalowa ku Munda wamtendere pomwe Allah asadawaonetsere poyera amene amenyera chipembedzo cha Allah mwa inu ndi kuwaonetseranso poyera opirira (pa nkhondo ya Allah)?
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَقَدۡ كُنتُمۡ تَمَنَّوۡنَ ٱلۡمَوۡتَ مِن قَبۡلِ أَن تَلۡقَوۡهُ فَقَدۡ رَأَيۡتُمُوهُ وَأَنتُمۡ تَنظُرُونَ
Ndithudi, mudali kuilakalaka imfa musanakumane nayo. Ndithudi tsopano mwaiona (ndikuphedwa kwa abale anu) inu mukupenya. [90]
[90] Pamene Asilamu adamva ubwino waukulu umene angaupeze akafera pa nkhondoyo monga “Shahidi”, aliyense wa iwo adakhumba akadafera pa nkhondo yoteroyo, kuti akapeze ulemelerowo. Choncho Asilamu makumi asanu ndi awiri (70) adaphedwa pa nkhondo ya Uhudi mwa anthu mazana asanu ndi awiri (700) omwe adaima mwamphamvu kulimbana ndi anthu osakhulupilira omwe adalipo zikwi zitatu (3,000).
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا مُحَمَّدٌ إِلَّا رَسُولٞ قَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِهِ ٱلرُّسُلُۚ أَفَإِيْن مَّاتَ أَوۡ قُتِلَ ٱنقَلَبۡتُمۡ عَلَىٰٓ أَعۡقَٰبِكُمۡۚ وَمَن يَنقَلِبۡ عَلَىٰ عَقِبَيۡهِ فَلَن يَضُرَّ ٱللَّهَ شَيۡـٔٗاۚ وَسَيَجۡزِي ٱللَّهُ ٱلشَّٰكِرِينَ
Muhammad (s.a.w) sali chinthu china koma Mtumiki chabe. Patsogolo pake adamuka atumiki ambiri. Kodi ngati atamwalira kapena kuphedwa, mungabwelerenso m’mbuyo? Ndipo amene abwelere m’mbuyo mwake savutitsa Allah ndi chilichonse; koma Allah adzalipira othokoza.[91]
[91] Apa akunena mwatsatanetsatane kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) ndi mtumiki basi yemwe ndimunthu monga alili anthu ena onse. Adafa monga momwe ena adafera. Koma ngakhale iye wafa anthu ena atsanzire chikhalidwe chake ndi zophunzitsa zake zomwe amaphunzitsa. Asabwelere m’mbuyo kusiya Chipembedzo poona kuti iye wafa.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا كَانَ لِنَفۡسٍ أَن تَمُوتَ إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِ كِتَٰبٗا مُّؤَجَّلٗاۗ وَمَن يُرِدۡ ثَوَابَ ٱلدُّنۡيَا نُؤۡتِهِۦ مِنۡهَا وَمَن يُرِدۡ ثَوَابَ ٱلۡأٓخِرَةِ نُؤۡتِهِۦ مِنۡهَاۚ وَسَنَجۡزِي ٱلشَّٰكِرِينَ
Munthu aliyense sangafe pokhapokha mwa chilolezo cha Allah, (ndi kukwanira) nthawi yake yolembedwa. Ndipo amene akufuna mphoto ya pa dziko la pansi, timpatsa pompo; ndipo amene akufuna Mphoto ya tsiku lachimaliziro tidzampatsa konko. Ndipo, tidzawalipira (zabwino) othokoza.[92]
[92] Apa akutilimbikitsa kuti tigwire ntchito yodzatipindulira pa tsiku lachiweruziro molimbika, tsiku lomwe ndilamoyo wosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
وَكَأَيِّن مِّن نَّبِيّٖ قَٰتَلَ مَعَهُۥ رِبِّيُّونَ كَثِيرٞ فَمَا وَهَنُواْ لِمَآ أَصَابَهُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَمَا ضَعُفُواْ وَمَا ٱسۡتَكَانُواْۗ وَٱللَّهُ يُحِبُّ ٱلصَّٰبِرِينَ
Ndi Aneneri angati adamenyana (ndi adani) pamodzi ndi anthu olungama ambiri, komatu sadataye mtima pa mavuto omwe adawagwera pa njira ya Allah; sadafooke ndipo sadagonjere (adani awo), ndipo Allah amakonda opirira.[93]
[93] Asilamu akuwauza kuti asataye mtima atawagonjetsa pa nkhondo iliyonse, kapena atawapeza masautso amtundu uliwonse. Chofunika nkupilira ndi kulimbana nawo mavutowo.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا كَانَ قَوۡلَهُمۡ إِلَّآ أَن قَالُواْ رَبَّنَا ٱغۡفِرۡ لَنَا ذُنُوبَنَا وَإِسۡرَافَنَا فِيٓ أَمۡرِنَا وَثَبِّتۡ أَقۡدَامَنَا وَٱنصُرۡنَا عَلَى ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡكَٰفِرِينَ
(Anthu olungamawa) kunena kwawo sikudali kwina koma ankati: “Mbuye wathu! Tikhululukireni machimo athu ndi kupyola malire kwathu m’zinthu zathu. Ndipo limbikitsani mapazi athu (panjira Yanu) ndipo tithandizeni ku anthu osakhulupirira.”
Tafsir berbahasa Arab:
فَـَٔاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ ثَوَابَ ٱلدُّنۡيَا وَحُسۡنَ ثَوَابِ ٱلۡأٓخِرَةِۗ وَٱللَّهُ يُحِبُّ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Choncho Allah adawapatsa mphoto ya pa dziko lapansi ndi mphoto yabwino ya tsiku lachimaliziro. Allah amakonda ochita zabwino.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Āli 'Imrān
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Khalid Ibrahim Betala - Daftar isi terjemahan

Terjemahan oleh Khalid Ibrahim Bitala.

Tutup