Check out the new design

Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Khalid Ibrahim Betala * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Fāṭir   Ayah:
وَمَا يَسۡتَوِي ٱلۡأَعۡمَىٰ وَٱلۡبَصِيرُ
Ndipo wakhungu ndi wopenya ngosafanana, (woyenda pa njira ya choona ndi wosokera ngosafanana).
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا ٱلظُّلُمَٰتُ وَلَا ٱلنُّورُ
Ngakhale mdima ndi kuunika (nzosafanana).
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا ٱلظِّلُّ وَلَا ٱلۡحَرُورُ
Ngakhale mthunzi ndi kutentha (nzosafanana).
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا يَسۡتَوِي ٱلۡأَحۡيَآءُ وَلَا ٱلۡأَمۡوَٰتُۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُسۡمِعُ مَن يَشَآءُۖ وَمَآ أَنتَ بِمُسۡمِعٖ مَّن فِي ٱلۡقُبُورِ
Ndipo amoyo ndi akufa safanana (amene mitima yawo ili ndi moyo pokhala ndi chikhulupiliro, ndi amene mitima yawo ili yakufa posakhala ndi chikhulupiliro, ngosafanana). Ndithu Allah akumumveretsa amene wam’funa; koma iwe sungathe kumumveretsa amene ali m’manda.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنۡ أَنتَ إِلَّا نَذِيرٌ
Iwe sindiwe chinthu china, koma ndiwe mchenjezi.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَٰكَ بِٱلۡحَقِّ بَشِيرٗا وَنَذِيرٗاۚ وَإِن مِّنۡ أُمَّةٍ إِلَّا خَلَا فِيهَا نَذِيرٞ
Ndithu Ife takutuma mwachoona kuti unene nkhani yabwino (yokalowa ku Munda wamtendere kwa amene akhulupirira), ndi kuti uchenjeze (za chilango cha Moto kwa amene sadakhulupirire). Ndipo palibe m’badwo uliwonse koma mchenjezi adapitamo.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِن يُكَذِّبُوكَ فَقَدۡ كَذَّبَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ جَآءَتۡهُمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ وَبِٱلزُّبُرِ وَبِٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُنِيرِ
Ndipo ngati angakutsutse (sichachilendo), ndithu amene adali patsogolo pawo adatsutsanso. Aneneri awo adawadzera ndi zizindikiro zoonekera poyera, ndi malemba ndi buku lounikira (njira yabwino).
Tafsir berbahasa Arab:
ثُمَّ أَخَذۡتُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۖ فَكَيۡفَ كَانَ نَكِيرِ
Kenako ndidawalanga (ndidawaononga) amene adatsutsa. Nanga chidali bwanji chilango Changa (pa iwo).
Tafsir berbahasa Arab:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَخۡرَجۡنَا بِهِۦ ثَمَرَٰتٖ مُّخۡتَلِفًا أَلۡوَٰنُهَاۚ وَمِنَ ٱلۡجِبَالِ جُدَدُۢ بِيضٞ وَحُمۡرٞ مُّخۡتَلِفٌ أَلۡوَٰنُهَا وَغَرَابِيبُ سُودٞ
Kodi sudaone kuti Allah amatsitsa madzi kuchokera ku mitambo? Choncho kupyolera m’madziwo tatulutsa zipatso zautoto wosiyanasiyana (zakuda, zofiira, zachikasu, zobiriwira, pomwe madzi ake ndiamodzi omwewo). Ndipo m’mapiri muli timizere; toyera ndi tofiira tosiyana utoto wake, ndi (tina) takuda kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمِنَ ٱلنَّاسِ وَٱلدَّوَآبِّ وَٱلۡأَنۡعَٰمِ مُخۡتَلِفٌ أَلۡوَٰنُهُۥ كَذَٰلِكَۗ إِنَّمَا يَخۡشَى ٱللَّهَ مِنۡ عِبَادِهِ ٱلۡعُلَمَٰٓؤُاْۗ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ غَفُورٌ
Ndipo mwa anthu ndi nyama zokwawa, ndi ziweto, nchimodzimodzinso; nzosiyana maonekedwe ake (utoto wake). Ndithu odziwa ndi amene amamuopa Allah mwa akapolo Ake. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngokhululuka kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَتۡلُونَ كِتَٰبَ ٱللَّهِ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَأَنفَقُواْ مِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ سِرّٗا وَعَلَانِيَةٗ يَرۡجُونَ تِجَٰرَةٗ لَّن تَبُورَ
Ndithu amene akuwerenga buku la Allah uku nkumapemphera Swala moyenera napereka m’zimene tawapatsa mwanseri ndi moonetsera, iwo akuyembekezera malonda osaonongeka.
Tafsir berbahasa Arab:
لِيُوَفِّيَهُمۡ أُجُورَهُمۡ وَيَزِيدَهُم مِّن فَضۡلِهِۦٓۚ إِنَّهُۥ غَفُورٞ شَكُورٞ
Kuti akawakwaniritsire malipiro awo ndi kuwaonjezera zabwino Zake; ndithu Iye Ngokhululuka kwabasi; Ngothokoza kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Fāṭir
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Khalid Ibrahim Betala - Daftar isi terjemahan

Terjemahan oleh Khalid Ibrahim Bitala.

Tutup