Ndi omwe akupereka chuma chawo modzionetsera kwa anthu ndipo sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Ndiponso yemwe satana angakhale bwenzi lake, ndithudi ali ndi bwenzi loipa.
Kodi pakadakhala vuto lanji kwa iwo ngati akadakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro napereka zina mwa zomwe Allah wawapatsa? Ndipo Allah ali Wodziwa bwino za iwo.
Kodi sukuwaona omwe adapatsidwa gawo la (nzeru zozindikira) buku (la Allah, omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu), akudzisankhira kusokera ndiponso akufuna mutasokera kusiya njira (yabwino).[125]
[125] (Ndime 44-46) Apa akutchula kuipa kwina kwa Ayuda ndi Akhrisitu. Iwo adali kusintha mawu omwe adali m’mabuku a Taurat ndi Injil, makamaka mawu amene adali kusonyeza za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Kapena adali kuwatanthauzira m’njira zina zogwirizana ndi zolinga zawo. Pamene adali kudza kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) makamaka Ayuda, akawalalikira mawu achipembedzo, ankati: “Tamva, titsatira,” pomwe m’mitima mwawo akuti “Sititsatira zonse zomwe ukunena. Koma tikungokunyenga chabe.” Amati akadza nkumva momwe maswahaba amanenera ndi Mtumiki (s.a.w), Mtumiki akawalalikira, amati: “Ismaa ghayra musma’” monga mwa chizolowezi cha Arabu akauzidwa mawu ofunika. Tanthuzo lake nkuti, “Imva siumvanso choipa kuchokera kwa ife ngati Allah afuna.” Naonso Ayuda adali kumnenera Mtumiki mawu omwewa, koma m’mitima mwawo akulinga tanthauzo lina. M’mitima mwawo amalinga kuti, “Siumva zabwino kuchokera kwa ife ngati Allah afuna, koma zokusowetsa mtendere zokhazokha.” Ndipo amati akabweranso Ayudawo nkumva maswahaba akumuuza Mtumiki kuti; “Raa’ina”. Kutanthauza kuti, “Tiyang’ane ndi diso lachifundo,” iwonso amayankhula mawu omwewa, koma mokhotetsa pang’ono mpaka kusinthika tanthauzo lake. M’chiyankhulo cha chiyuda limatanthauza kuti “E iwe mbutuma!” Ndipo iwo m’kunena kwawo amalinga tanthauzo limeneli. Choncho Asilamu anawauza kuti azigwiritsira ntchito mawu oti “Undhurna.” Ndipo mawuwa tanthauzo lake ndilofanana. Koma mawu awa Ayuda sakadatha kuwakhotetsa.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
Hasil pencarian:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".