Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (35) Sura: Al ‘Imrân
إِذۡ قَالَتِ ٱمۡرَأَتُ عِمۡرَٰنَ رَبِّ إِنِّي نَذَرۡتُ لَكَ مَا فِي بَطۡنِي مُحَرَّرٗا فَتَقَبَّلۡ مِنِّيٓۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
(Kumbukirani) pamene adanena mkazi wa Imran (mayi wa Mariya), m’mapemphero ake): “Mbuye wanga! Ndapereka kwa Inu chimene chili m’mimba mwanga monga “waqf” (wotumikira m’kachisi Wanu). Tero landirani ichi kwa ine. Ndithudi, Inu ndinu Akumva, Wodziwa.”[67]
[67] (Ndime 35-36) Mkazi wa Imran pamene adali ndi pakati, ankaganiza kuti adzabereka mwana wa mwamuna. Ndipo adalonjeza kwa Allah kuti mwanayo adzampereka kuti akhale wotumikira ku msikiti wa Baiti Limakadasi (Yelusalemu), ndi kutinso adzatumikire pa zinthu zina za chipembedzo. Ntchito yake idzangokhala yokhayo. Koma mmalomwake adabereka mwana wamkazi. Ndipo kuti adzakhale mwana wabwino nkutinso adzabereke ana abwino, adamutcha dzina loti Mariya (wotumikira Allah). Tero mayi Mariya adali mayi wabwino. Ndipo nayenso adabala mwana wabwino yemwe ndi mneneri Isa (Yesu). Mariya ndi mayi wolemekezeka kwabasi.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (35) Sura: Al ‘Imrân
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi