Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (2) Sura: At-Tahrîm
قَدۡ فَرَضَ ٱللَّهُ لَكُمۡ تَحِلَّةَ أَيۡمَٰنِكُمۡۚ وَٱللَّهُ مَوۡلَىٰكُمۡۖ وَهُوَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
Ndithu Allah wakhazikitsa kamasulidwe kakulumbira kwanu, ndipo Allah ndiye Mtetezi wanu, Iye Ngodziwa kwambiri ndiponso Ngwanzeru zakuya (pa malamulo amene wawakhazikitsa kwa inu).[368]
[368] Mkazi ndimkazi basi. Mtumiki adanena m’Mahadisi kuti sipadapezeke mkazi amene ali wokwanira pa chinthu chilichonse kuyambira pamene dziko lidayamba mpaka kutha kwake kupatula akazi anayi basi. Iwowa ndi awa: Mayi Fatuma, Mayi Khadija, Mayi Mariya ndi mayi Asiya (mkazi wa Farawo). Kusakwanira kwa akazi pa chilichonse kumapezekanso ngakhale mwa akazi a Mtumiki, amamsautsa Mtumiki pomuchitira nsanje ngakhale kuti iwo amapemphera kwambiri, kawirikawiri makamaka amayi awiri awa Mayi Aisha ndi Mayi Hafsa monga momwe zilili m’ndime 4 ya sura iyi. Allah wawakalipira kwambiri m’ndime 5 ya sura yomweyi ndi m’ndime 28 ya surat Ahzab. Koma adalapa mwachangu ndipo Allah adawayanja monga zilili m’ndime 52 ya Sûrat Ahzab.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (2) Sura: At-Tahrîm
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi