وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (9) سوره‌تی: سورەتی طه
وَهَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ
Ndipo kodi yakufika nkhani ya Mûsa? (Yomwe njododometsa)?[273]
[273] Ibun Abbas adati: “Izi zidali choncho Musa pamene adakwaniritsa chipangano cha nthawi imene adapangana ndi m’neneri Shuaibu chakuti amuwetere mbuzi kwa zaka 8 kapena 10, adachoka ulendo kubwerera kwawo ku Iguputo pamodzi ndi banja lake; ndipo adasokera njira. Udali usiku wamdima wozizira. Adayesa kupekesa moto kuti awothe koma adalephera. Ndipo ali choncho, adangoona moto chapatali kumbali yakumanja kwa njira. Pamene adauona adauganizira kuti ndi moto weniweni, pomwe udali moto woyera wakuunika kwa Allah. Udali kuyaka mu mtengo wamasamba obiriwira. Ndipo adangomva Mbuye wake akumuitana: “E iwe Musa! Ine ndine Mbuye wako. Ndikukuyankhula; vula nsapato zako.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (9) سوره‌تی: سورەتی طه
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن