وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (113) سوره‌تی: سورەتی النساء
وَلَوۡلَا فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ وَرَحۡمَتُهُۥ لَهَمَّت طَّآئِفَةٞ مِّنۡهُمۡ أَن يُضِلُّوكَ وَمَا يُضِلُّونَ إِلَّآ أَنفُسَهُمۡۖ وَمَا يَضُرُّونَكَ مِن شَيۡءٖۚ وَأَنزَلَ ٱللَّهُ عَلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَعَلَّمَكَ مَا لَمۡ تَكُن تَعۡلَمُۚ وَكَانَ فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ عَظِيمٗا
Ndipo pakadapanda ubwino wa Allah ndi chisoni chake pa iwe, ndithudi, gulu limodzi la iwo likadalinga kukusokeretsa. Ndipo iwo palibe yemwe akadamsokeretsa koma iwo okha basi. Ndipo sangathe kukuvutitsa ndi chilichonse. Ndipo Allah wakuvumbulutsira buku, kudzanso luntha. Ndipo wakuphunzitsa zomwe sudali kuzidziwa. Ndipo ubwino wa Allah umene uli pa iwe ngwaukulu zedi.[147]
[147] Apa Allah akunena kuti palibe chisomo chimene Allah wapatsa munthu chachikulu ndi chopindulitsa kuposa luntha. Chilichonse chabwino cha pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro chimapezeka chifukwa cha kudziwa zinthu. Qur’an yonse ndi hadisi za Mtumiki zikulimbikitsa zakufunafuna luntha lodziwira zinthu zakuti zimkonzere munthu za dziko lapansi ndi za tsiku lachimaliziro, kotero kuti Qur’an ndi hadisizo zikunena kuti munthu apite kunja kunka nafunafuna maphunziro.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (113) سوره‌تی: سورەتی النساء
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن