وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (154) سوره‌تی: سورەتی النساء
وَرَفَعۡنَا فَوۡقَهُمُ ٱلطُّورَ بِمِيثَٰقِهِمۡ وَقُلۡنَا لَهُمُ ٱدۡخُلُواْ ٱلۡبَابَ سُجَّدٗا وَقُلۡنَا لَهُمۡ لَا تَعۡدُواْ فِي ٱلسَّبۡتِ وَأَخَذۡنَا مِنۡهُم مِّيثَٰقًا غَلِيظٗا
Ndipo tidatukula phiri la Al-Tur pamwamba pawo (Ayudawo) polandira pangano lawo; tidati kwa iwo: “Lowani pachipata (cha dziko ili la Sham) mutawerama.” Tidatinso kwa iwo: “Musalumphe malire pa nkhani ya Sabata.” Ndipo tidalandira kwa iwo pangano lokhwima.[154]
[154] (Ndime 154-156) Allah akupitiriza kufotokoza zoipa zawo. Ndipo zina mwa izo ndiizi: (a) Adakana kutsatira malamulo am’Taurat. Ndipo Allah adazula phiri naliimitsa pamwamba pa mitu yawo nawauza kuti: “Ngati simulola kulonjeza kuti mdzatsata zomwe zili m’Taurat, likusinjani phiri ili. (b) Adakana kulowera pachipata kudziko la Shamu (Kenani) monga momwe Allah adawalangizira. Ndipo adalowa monga momwe iwo amafunira. Shamu ndi dziko lomwe Allah adawapatsa kuti akalowemo ndi kukhazikika pambuyo posamuka ku Eguputo (Egypt). Koma iwo sadathokoze chisomochi potsata zomwe Allah adawauza. (c) Pambuyo polowa m’dzikolo adawauza kuti alemekeze tsiku la Sabata kuti likhale tsiku lamapemphero okhaokha. Lisakhale tsiku logwira ntchito. Koma iwo adachitachita ndale zawo mpaka lidasanduka tsiku logwira ntchito. (d) Ena mwa aneneri awo pamene adawaletsa iwo machitidwe amenewa mwaukali adawapha. (e) Mneneri Muhammad pamene adawafotokozera zizindikiro zomwe zinali m’mabuku mwawo zimene zimasonyeza utumiki wake sadamulabadire. Nanena kuti :“Mitima yathu yakutidwa. Siikumvetsa chilichonse chimene ukunena”. (f) Mneneri Isa (Yesu) pamene adawafotokozera za utumiki wake ndi kuwasonyeza zozizwitsa ndi zonse zomwe zidachitika m’kubadwa kwake, iwo adati Mariya adatenga pakati m’njira yachiwerewere pomwe iwo amadziwa kuti akungonama. (g) Adakonza chiwembu kuti aphe Isa (Yesu). Koma Allah adachiononga chiwembu chawocho pomuveka munthu wina nkhope ya Isa (Yesu) amene adali wamkulu wawo yemwe ankafunisitsa kupha Isa (Yesu). Tero adampachika mnzawoyo pamtanda. Pambuyo pake, akuluakulu aChiyuda adazindikira zonse zomwe zidachitikazi. Ndipo adangonyozera ngati kuti sichidachitike chilichonse chododometsa chifukwa choopa kuti anthu angawaukire. M’malomwake ankangodzidzudzula okha m’mtima mwawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (154) سوره‌تی: سورەتی النساء
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن