وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (22) سوره‌تی: سورەتی النساء
وَلَا تَنكِحُواْ مَا نَكَحَ ءَابَآؤُكُم مِّنَ ٱلنِّسَآءِ إِلَّا مَا قَدۡ سَلَفَۚ إِنَّهُۥ كَانَ فَٰحِشَةٗ وَمَقۡتٗا وَسَآءَ سَبِيلًا
Ndipo musakwatire akazi amene adakwatiwapo ndi atate anu, kupatula zomwe zidapita, (musabwerezenso kuzichita). Ndithudi, chinthu ichi nchauve ndipo nchodedwa ndiponso ndinjira yoipa.[117]
[117] Ndime iyi ndi zinzake zotsatira zikufotokoza za akazi omwe ngoletsedwa kuwakwatira pa Shariya ya Chisilamu. Ena mwa akaziwo ndi awa:-
1) Munthu sangakwatire mkazi yemwe bambo wake adamkwatirapo kapena yemwe adakwatiwapo ndi gogo wake wakuchimuna kapena kuchikazi. Koma osati amene adasiidwa ndimalume ake kapena m’bale watate wake. Amenewa akhoza kuwakwatira.
2) Mayi wako yemwe adakubereka ndi mayi wamayi wako.
3) Mwana wako wodziberekera wekha, kapena mwana amene mwana wako adabereka.
4) Tate wako wamkazi (zakhali) ndi alongo agogo ako.
5) Mayi wako wamng’ono (m’bale wamayi wako) ndi m’bale wamkazi wa agogo ako akuchikazi.
6) Mwana wa m’bale wako wobadwa naye bambo ndi mayi mmodzi kapena wobadwa naye mayi mmodzi kapena bambo mmodzi ndi ana onse akazi oberekedwa ndi mwanayo.
7) Mwana wamkazi wa mlongo wako (mfumukazi) wamayi ndi bambo mmodzi kapena wakumbali yabambo yokha kapenanso wakumbali yamayi yokha.
8) Mkazi yemwe adakuyamwitsapo ndi mayi ake amkaziyo kapena omwe adamuyamwitsaponso iye.
9) Mkazi yemwe unayamwa naye bere limodzi.
10) Mayi wamkazi wanu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (22) سوره‌تی: سورەتی النساء
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن