وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی الأعراف   ئایه‌تی:

سورەتی الأعراف

الٓمٓصٓ
Alif-Lâm-Mîm-Sad.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
كِتَٰبٌ أُنزِلَ إِلَيۡكَ فَلَا يَكُن فِي صَدۡرِكَ حَرَجٞ مِّنۡهُ لِتُنذِرَ بِهِۦ وَذِكۡرَىٰ لِلۡمُؤۡمِنِينَ
(Iyi Qur’an ndi) buku (lopatulika) lomwe lavumbulutsidwa kwa iwe. Choncho chifuwa chako chisabanike ndi ilo (poopa kufikitsa mawu ake kwa anthu kuti angakuyese wabodza;) kuti uwachenjeze nalo (otsutsa) ndi kuti likhale chikumbutso kwa okhulupirira (kuti aonjezere chikhulupiliro chawo).[178]
[178] Apa akumuuza Mtumiki (s.a.w) kuti asaope kulengeza zimene Allah wamuululira. Asatekeseke ndi otsutsa ngakhale atachuluka chotani. Mlaliki aliyense akuuzidwanso chimodzimodzi. Anene choonadi kwa anthu ndipo asaope kudzudzulidwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱتَّبِعُواْ مَآ أُنزِلَ إِلَيۡكُم مِّن رَّبِّكُمۡ وَلَا تَتَّبِعُواْ مِن دُونِهِۦٓ أَوۡلِيَآءَۗ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Tsatirani zomwe zavumbulutsidwa kwa inu kuchokera kwa Mbuye wanu, ndipo musawatsatire omwe sali Allah powayesa atetezi (anu). Ndizochepa zimene mumazikumbukira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَكَم مِّن قَرۡيَةٍ أَهۡلَكۡنَٰهَا فَجَآءَهَا بَأۡسُنَا بَيَٰتًا أَوۡ هُمۡ قَآئِلُونَ
Ndimidzi yambiri imene tidaiononga ndipo chilango Chathu chidaidzera nthawi ya usiku, kapena usana iwo atagona tulo tamasana (akupumula monga momwe zinawachitikira anthu a Loti ndi anthu a Shuaib).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَمَا كَانَ دَعۡوَىٰهُمۡ إِذۡ جَآءَهُم بَأۡسُنَآ إِلَّآ أَن قَالُوٓاْ إِنَّا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
Ndipo sikunali kulira kwawo pamene chinawafika chilango chathu koma kunena (ndi kuvomereza): “Ndithudi, ife tinali ochita zoipa.” (Koma kuvomereza kwawoko sikunawapindulire kanthu).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَنَسۡـَٔلَنَّ ٱلَّذِينَ أُرۡسِلَ إِلَيۡهِمۡ وَلَنَسۡـَٔلَنَّ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Mtheradi tidzawafunsa (anthu) amene anatumiziridwa (atumiki), naonso atumikiwo tidzawafunsa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَنَقُصَّنَّ عَلَيۡهِم بِعِلۡمٖۖ وَمَا كُنَّا غَآئِبِينَ
Tsono tidzawauza mozindikira bwino-bwino (chilichonse chimene ankachita). Ndipo sitidali kutali (nawo pamene ankachita zochita zawo).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلۡوَزۡنُ يَوۡمَئِذٍ ٱلۡحَقُّۚ فَمَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Ndipo sikero (yoyezera zochita za anthu) tsiku limenelo idzakhala yoona (yopanda chinyengo). Choncho, amene idzalemere miyeso yake (ya zabwino), iwowo ndiwo opambana.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ فَأُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ خَسِرُوٓاْ أَنفُسَهُم بِمَا كَانُواْ بِـَٔايَٰتِنَا يَظۡلِمُونَ
Ndipo amene idzapepuke miyeso yawo (ya zinthu zawo zabwino), iwo ndi amene ataya pachabe moyo wawo chifukwa cha kuzichitira zosalungama zizindikiro Zathu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَقَدۡ مَكَّنَّٰكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَجَعَلۡنَا لَكُمۡ فِيهَا مَعَٰيِشَۗ قَلِيلٗا مَّا تَشۡكُرُونَ
Ndithudi tinakupatsani mphamvu yokhalira pa dziko, ndipo takupangirani m’menemo zinthu zofunika pa moyo wanu. Koma kuyamika kwanu mpang’ono.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَقَدۡ خَلَقۡنَٰكُمۡ ثُمَّ صَوَّرۡنَٰكُمۡ ثُمَّ قُلۡنَا لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ ٱسۡجُدُواْ لِأٓدَمَ فَسَجَدُوٓاْ إِلَّآ إِبۡلِيسَ لَمۡ يَكُن مِّنَ ٱلسَّٰجِدِينَ
Ndithudi, tinakulengani, kenako tidakukonzani (pokupatsani ziwalo) ndi kunena kwa angelo kuti: “Mgwadireni Adam.” Ndipo adamgwadira kupatula Iblis, sadali mwa ogwada.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ مَا مَنَعَكَ أَلَّا تَسۡجُدَ إِذۡ أَمَرۡتُكَۖ قَالَ أَنَا۠ خَيۡرٞ مِّنۡهُ خَلَقۡتَنِي مِن نَّارٖ وَخَلَقۡتَهُۥ مِن طِينٖ
(Allah) adati: “Nchiyani chakuletsa kumgwadira pamene ndakulamula?” (Satana) anati: “Ine ndine wabwino kuposa iye. Ine munandilenga ndi moto koma iye mudamulenga ndi dongo.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ فَٱهۡبِطۡ مِنۡهَا فَمَا يَكُونُ لَكَ أَن تَتَكَبَّرَ فِيهَا فَٱخۡرُجۡ إِنَّكَ مِنَ ٱلصَّٰغِرِينَ
(Allah) adati: “Choncho, choka m’menemo ndi kutsikira pansi. Sikofunika kwa iwe kudzitama m’menemo. Tuluka, ndithu iwe ndiwe mmodzi wa onyozeka.”[179]
[179] Allah anamtulutsa m’nyumba ya ulemelero Wake chifukwa cha kudzitama ndi kunyoza lamulo la Allah.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ أَنظِرۡنِيٓ إِلَىٰ يَوۡمِ يُبۡعَثُونَ
(Satana) adati: “Ndipatseni nthawi mpaka tsiku limene adzaukitsidwa (akapolo anu ku imfa).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ إِنَّكَ مِنَ ٱلۡمُنظَرِينَ
(Allah) adati: “Ndithudi iwe ndi mmodzi wa opatsidwa nthawi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ فَبِمَآ أَغۡوَيۡتَنِي لَأَقۡعُدَنَّ لَهُمۡ صِرَٰطَكَ ٱلۡمُسۡتَقِيمَ
Iye (chifukwa cha njiru yake yoopsa pa Adam) adati: “Tsono chifukwa chakuti mwandichita ine kukhala wopotoka, ndidzawakhalira (akapolo Anu ndi kuwabisalira) pa njira Yanu yoongoka (ndi cholinga chowasokeretsa).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ثُمَّ لَأٓتِيَنَّهُم مِّنۢ بَيۡنِ أَيۡدِيهِمۡ وَمِنۡ خَلۡفِهِمۡ وَعَنۡ أَيۡمَٰنِهِمۡ وَعَن شَمَآئِلِهِمۡۖ وَلَا تَجِدُ أَكۡثَرَهُمۡ شَٰكِرِينَ
Kenako ndidzawadzera (mbali ya) kutsogolo kwawo, m’mbuyo mwawo, kumbali yakumanja kwawo ndi kumanzere kwawo, mwakuti simudzapeza ambiri a iwo oyamika.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱخۡرُجۡ مِنۡهَا مَذۡءُومٗا مَّدۡحُورٗاۖ لَّمَن تَبِعَكَ مِنۡهُمۡ لَأَمۡلَأَنَّ جَهَنَّمَ مِنكُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Allah) adati: “Tuluka m’menemo, uli wonyozeka ndi wothamangitsidwa. Amene adzakutsata iwe mwa iwo, ndithudi, (ndikamponya ku Moto). Ndipo ndikaidzadzitsa Jahannam ndi inu nonse.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَيَٰٓـَٔادَمُ ٱسۡكُنۡ أَنتَ وَزَوۡجُكَ ٱلۡجَنَّةَ فَكُلَا مِنۡ حَيۡثُ شِئۡتُمَا وَلَا تَقۡرَبَا هَٰذِهِ ٱلشَّجَرَةَ فَتَكُونَا مِنَ ٱلظَّٰلِمِينَ
(Kenako Allah adanena kwa Adam) “E iwe Adam! Khala ndi mkazi wako m’Munda wamtendere (sangalalani ndi zomwe zili m’menemo), idyani paliponse pamene mwafuna. Koma mtego uwu musawuyandikire kuopera kuti mungakhale m’gulu la odzichitira okha zoipa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَوَسۡوَسَ لَهُمَا ٱلشَّيۡطَٰنُ لِيُبۡدِيَ لَهُمَا مَا وُۥرِيَ عَنۡهُمَا مِن سَوۡءَٰتِهِمَا وَقَالَ مَا نَهَىٰكُمَا رَبُّكُمَا عَنۡ هَٰذِهِ ٱلشَّجَرَةِ إِلَّآ أَن تَكُونَا مَلَكَيۡنِ أَوۡ تَكُونَا مِنَ ٱلۡخَٰلِدِينَ
Choncho satana adawanong’oneza (zoipa) kuti awaonetsere zomwe zidabisika kwa iwo za maliseche awo. Ndipo (satana) adati: “Mbuye wanu sadakuletseni mtengo uwu, koma pachifukwa chakuti mungasanduke angelo awiri, kapena kuti mungakhale okhala nthawi yaitali.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَاسَمَهُمَآ إِنِّي لَكُمَا لَمِنَ ٱلنَّٰصِحِينَ
Ndipo adawalumbilira onse awiri kuti: “Ndithudi, ine ndine mmodzi mwa olangiza (ndikukufunirani zabwino).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَدَلَّىٰهُمَا بِغُرُورٖۚ فَلَمَّا ذَاقَا ٱلشَّجَرَةَ بَدَتۡ لَهُمَا سَوۡءَٰتُهُمَا وَطَفِقَا يَخۡصِفَانِ عَلَيۡهِمَا مِن وَرَقِ ٱلۡجَنَّةِۖ وَنَادَىٰهُمَا رَبُّهُمَآ أَلَمۡ أَنۡهَكُمَا عَن تِلۡكُمَا ٱلشَّجَرَةِ وَأَقُل لَّكُمَآ إِنَّ ٱلشَّيۡطَٰنَ لَكُمَا عَدُوّٞ مُّبِينٞ
Tero adawakopa mwachinyengo. Ndipo pamene adalawa zipatso za mtengowo umaliseche wawo udaoneka kwa iwo nayamba kudziphatika masamba (a mitengo) a m’mundamo. Ndipo Mbuye wawo adawaitana (mowadzudzula) nati: “Kodi sindinakuletseni mtengowu ndi kukuuzani kuti satana ndi mdani wanu woonekeratu?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَا رَبَّنَا ظَلَمۡنَآ أَنفُسَنَا وَإِن لَّمۡ تَغۡفِرۡ لَنَا وَتَرۡحَمۡنَا لَنَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡخَٰسِرِينَ
Iwo (Adam ndi mkazi wake) adati (modzichepetsa): “E Mbuye wathu! Tadzichitira tokha zoipa, ngati simutikhululukira ndi kuchita nafe chifundo ndiye kuti tikhala mwa otaika.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱهۡبِطُواْ بَعۡضُكُمۡ لِبَعۡضٍ عَدُوّٞۖ وَلَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُسۡتَقَرّٞ وَمَتَٰعٌ إِلَىٰ حِينٖ
(Allah) adati: “Tsikani pansi uku pali chidani pakati panu. Ndipo padziko lapansi ndipokhala panu ndi kusangalala kwanu mpaka m’nthawi yoikidwayo.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ فِيهَا تَحۡيَوۡنَ وَفِيهَا تَمُوتُونَ وَمِنۡهَا تُخۡرَجُونَ
(Allah) adatinso: “Muzikakhala moyo pamenepo, ndipo muzikafa pamenepo; ndipo momwemo mudzatulutsidwa (mutauka kwa akufa).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ قَدۡ أَنزَلۡنَا عَلَيۡكُمۡ لِبَاسٗا يُوَٰرِي سَوۡءَٰتِكُمۡ وَرِيشٗاۖ وَلِبَاسُ ٱلتَّقۡوَىٰ ذَٰلِكَ خَيۡرٞۚ ذَٰلِكَ مِنۡ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ لَعَلَّهُمۡ يَذَّكَّرُونَ
E inu ana a Adam! Ndithu tatsitsa kwa inu chovala chobisa umaliseche wanu ndi chodzikongoletsera nacho. Koma chovala choopa nacho Allah (pakudziyeretsa ku zoletsedwa) chimenecho ndicho chabwino koposa. Zimenezo ndi zizindikiro za (chisomo cha) Allah kuti iwo akumbukire.[180]
[180] Allah akutiuza kuti tivale nsalu zomwe Allah adatipangira kuti zikongoletse matupi athu. Komatu akutilamulanso kuti tivale nsalu zokongoletsa mitima yathu; nsalu yomwe njotsatira nayo malamulo a Allah ndi kusiya zomwe Iye waletsa; ndi kuchita zokhazo zomwe Allah walamula. Nsalu imeneyi ndi “takuwa” (kuopa Allah). Sibwino kukongoletsa kunja kwa thupi kokha pomwe mu mtima mwadzaza zauve.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ لَا يَفۡتِنَنَّكُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ كَمَآ أَخۡرَجَ أَبَوَيۡكُم مِّنَ ٱلۡجَنَّةِ يَنزِعُ عَنۡهُمَا لِبَاسَهُمَا لِيُرِيَهُمَا سَوۡءَٰتِهِمَآۚ إِنَّهُۥ يَرَىٰكُمۡ هُوَ وَقَبِيلُهُۥ مِنۡ حَيۡثُ لَا تَرَوۡنَهُمۡۗ إِنَّا جَعَلۡنَا ٱلشَّيَٰطِينَ أَوۡلِيَآءَ لِلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ
E inu ana a Adam! Satana asakusokonezeni monga momwe adawatulutsira makolo anu m’Munda wamtendere ndi kuwavula onse awiri chovala chawo kuti awasonyeze umaliseche wawo. Ndithu iye ndi mtundu wake akukuonani pomwe inu simukuwaona. Ndithu asatana tawachita kukhala abwenzi a osakhulupirira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذَا فَعَلُواْ فَٰحِشَةٗ قَالُواْ وَجَدۡنَا عَلَيۡهَآ ءَابَآءَنَا وَٱللَّهُ أَمَرَنَا بِهَاۗ قُلۡ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَأۡمُرُ بِٱلۡفَحۡشَآءِۖ أَتَقُولُونَ عَلَى ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Ndipo (osakhulupirira) akachita chauve amanena: “(Ichi) tidawapeza nacho makolo athu (akuchichita), ndiponso Allah watilamula chimenechi.” Nena: “Ndithu Allah salamula zonyansa. Kodi mukumunenera Allah zomwe simukuzidziwa?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قُلۡ أَمَرَ رَبِّي بِٱلۡقِسۡطِۖ وَأَقِيمُواْ وُجُوهَكُمۡ عِندَ كُلِّ مَسۡجِدٖ وَٱدۡعُوهُ مُخۡلِصِينَ لَهُ ٱلدِّينَۚ كَمَا بَدَأَكُمۡ تَعُودُونَ
Nena: “Mbuye wanga walamula chilungamo; ndiponso (wandiuza kuti ndikuuzeni kuti) lungamitsani nkhope zanu (kwa Iye) m’nthawi ya Swala iliyonse, ndipo mpembedzeni Iye Yekha momuyeretsera chipembedzo monga Iye adakulengani pachiyambi, momwemonso mudzabwerera kwa Iye.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَرِيقًا هَدَىٰ وَفَرِيقًا حَقَّ عَلَيۡهِمُ ٱلضَّلَٰلَةُۚ إِنَّهُمُ ٱتَّخَذُواْ ٱلشَّيَٰطِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَيَحۡسَبُونَ أَنَّهُم مُّهۡتَدُونَ
Gulu lina waliongola, pomwe gulu lina patsimikizika pa ilo kusokera chifukwa chakuti iwo adasankha asatana kukhala atetezi (awo) kusiya Allah; ndipo akuganiza kuti iwo ngoongoka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ خُذُواْ زِينَتَكُمۡ عِندَ كُلِّ مَسۡجِدٖ وَكُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ وَلَا تُسۡرِفُوٓاْۚ إِنَّهُۥ لَا يُحِبُّ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
E inu ana a Adam! Tengani (valani) zovala zanu zabwino pamene mukukapemphera Swala iliyonse ndipo idyani ndi kumwa; koma musapyoze muyeso. Iye (Allah) sakonda opyoza muyeso (oononga).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قُلۡ مَنۡ حَرَّمَ زِينَةَ ٱللَّهِ ٱلَّتِيٓ أَخۡرَجَ لِعِبَادِهِۦ وَٱلطَّيِّبَٰتِ مِنَ ٱلرِّزۡقِۚ قُلۡ هِيَ لِلَّذِينَ ءَامَنُواْ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا خَالِصَةٗ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۗ كَذَٰلِكَ نُفَصِّلُ ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
Nena: “Ndani waletsa zokongoletsa za Allah (zovala), zomwe Iye (Allah) adawatulutsira akapolo Ake ndi zakudya zabwino?” Nena: “Zinthu zimenezo nzololedwa kwa amene akhulupirira (Asilamu) pamoyo wa pa dziko lapansi. (Zidzakhala) zawozawo tsiku la chimaliziro. M’menemo ndi momwe tikulongosolera Ayah (Zathu) kwa anthu ozindikira.”[181]
[181] Padali anthu ena omwe adali ndi chikhulupiliro choti kuvala nsanza ndi kudya zinthu zosakoma ndiko kumuopa Allah. Mpaka masiku ano alipobe anthu oganiza motere. Ndipo nchifukwa chake Allah akuvumbulutsa Ayah izi kuti kutero sindiko kumuopa Allah.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قُلۡ إِنَّمَا حَرَّمَ رَبِّيَ ٱلۡفَوَٰحِشَ مَا ظَهَرَ مِنۡهَا وَمَا بَطَنَ وَٱلۡإِثۡمَ وَٱلۡبَغۡيَ بِغَيۡرِ ٱلۡحَقِّ وَأَن تُشۡرِكُواْ بِٱللَّهِ مَا لَمۡ يُنَزِّلۡ بِهِۦ سُلۡطَٰنٗا وَأَن تَقُولُواْ عَلَى ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Nena (kwa iwo): “Ndithu Mbuye wanga waletsa zinthu zauve zoonekera ndi zobisika, ndi machimo, ndi kuwukira (atsogoleri) popanda choonadi, ndi kumphatikiza Allah ndi chomwe sadachitsitsire umboni (wakuti chiphatikizidwe ndi Iye); ndiponso (waletsa) kumunenera Allah zimene simukuzidziwa.”[182]
[182] Choipa nchoipa basi. Kaya kuchichita moonekera kapena mobisa, nchoipabe.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلِكُلِّ أُمَّةٍ أَجَلٞۖ فَإِذَا جَآءَ أَجَلُهُمۡ لَا يَسۡتَأۡخِرُونَ سَاعَةٗ وَلَا يَسۡتَقۡدِمُونَ
M’badwo ulionse uli ndi nthawi yakeyake (yofera). Ndipo nthawi yawo ikadza sangaichedwetse ngakhale ola limodzi, ndiponso sangaifulumizitse.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ إِمَّا يَأۡتِيَنَّكُمۡ رُسُلٞ مِّنكُمۡ يَقُصُّونَ عَلَيۡكُمۡ ءَايَٰتِي فَمَنِ ٱتَّقَىٰ وَأَصۡلَحَ فَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
E inu ana a Adam! Akakudzerani Atumiki ochokera mwa inu namakuuzani zivumbulutso Zanga, (avomereni), choncho omwe adzitchinjiriza ku zoletsedwa ndi kuchita zabwino, sipadzakhala mantha pa iwo ndiponso sadzadandaula.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَٱسۡتَكۡبَرُواْ عَنۡهَآ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Ndipo amene atsutsa zivumbulutso zathu nadzitukumula nazo, awo ndi anthu a ku Moto, adzakhala mmenemo nthawi yaitali.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَمَنۡ أَظۡلَمُ مِمَّنِ ٱفۡتَرَىٰ عَلَى ٱللَّهِ كَذِبًا أَوۡ كَذَّبَ بِـَٔايَٰتِهِۦٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ يَنَالُهُمۡ نَصِيبُهُم مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِۖ حَتَّىٰٓ إِذَا جَآءَتۡهُمۡ رُسُلُنَا يَتَوَفَّوۡنَهُمۡ قَالُوٓاْ أَيۡنَ مَا كُنتُمۡ تَدۡعُونَ مِن دُونِ ٱللَّهِۖ قَالُواْ ضَلُّواْ عَنَّا وَشَهِدُواْ عَلَىٰٓ أَنفُسِهِمۡ أَنَّهُمۡ كَانُواْ كَٰفِرِينَ
Kodi ndani woipitsitsa koposa munthu wopekera bodza Allah kapena wotsutsa zivumbulutso Zake? Iwo gawo (lachakudya chimene) adawalembera liwafika (pano pa dziko lapansi ngakhale kuti ngosakhulupirira mwa Allah). Kufikira pomwe adzawadzera atumiki Athu (angelo kudzatenga miyoyo yawo), nawapatsadi imfa uku akunena: “Kodi zili kuti zija munkazipembedza kusiya Allah?” Adzati: “Zatisowa.” Ndipo adzadzichitira okha umboni kuti iwo adali okana (Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱدۡخُلُواْ فِيٓ أُمَمٖ قَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِكُم مِّنَ ٱلۡجِنِّ وَٱلۡإِنسِ فِي ٱلنَّارِۖ كُلَّمَا دَخَلَتۡ أُمَّةٞ لَّعَنَتۡ أُخۡتَهَاۖ حَتَّىٰٓ إِذَا ٱدَّارَكُواْ فِيهَا جَمِيعٗا قَالَتۡ أُخۡرَىٰهُمۡ لِأُولَىٰهُمۡ رَبَّنَا هَٰٓؤُلَآءِ أَضَلُّونَا فَـَٔاتِهِمۡ عَذَابٗا ضِعۡفٗا مِّنَ ٱلنَّارِۖ قَالَ لِكُلّٖ ضِعۡفٞ وَلَٰكِن لَّا تَعۡلَمُونَ
(Allah) adzati (pa tsiku la chiweruziro): “Lowani ku Moto pamodzi ndi mibadwo imene idamuka kale (inu musanabwere) yochokera m’ziwanda ndi mu anthu. M’badwo uliwonse pamene uzikalowa, udzatembelera unzake, kufikira pamene onse adzasonkhana m’menemo. Adzanena apambuyo kwa oyambilira awo: “Mbuye wathu! Awa, adatisokeretsa. Apatseni chilango cha Moto chochuluka.” (Allah) adzanena: “Aliyense mwa inu akhala ndi chilango chochuluka; koma izi inu simukudziwa.”[183]
[183] Aliyense adzapeza chilango chachikulu. Ndipo awo amene adasokeretsedwa: (a) Adzapeza chilango chifukwa cholola kusokeretsedwa pomwe adapatsidwa nzeru zowazindikiritsa zabwino ndi zoipa. (b) Adzapeza chilango chifukwa chochita machimowo. Tsono amene adali kusokeretsa anzawo:
a) Adzapeza chilango chifukwa chakuchita kwawo machimo.
b) Adzapeza chilango chifukwa chakuwasokeretsa anthu omwe adawasokeretsa.
c) Adzapeza chilango chifukwa chakuyambitsa machimowo.
d) Adzapeza chilango chifukwa chowasiira anzawo odza m’mbuyo mwawo machimo powatsanzira iwo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَالَتۡ أُولَىٰهُمۡ لِأُخۡرَىٰهُمۡ فَمَا كَانَ لَكُمۡ عَلَيۡنَا مِن فَضۡلٖ فَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَ بِمَا كُنتُمۡ تَكۡسِبُونَ
Ndipo oyamba awo adzati kwa otsiriza awo: “Inunso mudalibe ubwino woposa ife; choncho, lawani chilango cha zomwe mudapeza (m’zochitachita zanu).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَٱسۡتَكۡبَرُواْ عَنۡهَا لَا تُفَتَّحُ لَهُمۡ أَبۡوَٰبُ ٱلسَّمَآءِ وَلَا يَدۡخُلُونَ ٱلۡجَنَّةَ حَتَّىٰ يَلِجَ ٱلۡجَمَلُ فِي سَمِّ ٱلۡخِيَاطِۚ وَكَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Ndithudi, amene akutsutsa zivumbulutso Zathu nadzitukumula nazo (pakukana kuzitsata), sadzatsekulidwa kwa iwo makomo a kumwamba, ndipo sadzalowa ku Munda wamtendere mpaka ngamira idzalowe pa bowo la singano. Umo ndimomwe timawalipirira anthu ochimwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
لَهُم مِّن جَهَنَّمَ مِهَادٞ وَمِن فَوۡقِهِمۡ غَوَاشٖۚ وَكَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلظَّٰلِمِينَ
Moto wa Jahannam ndi mphasa yawo; ndipo pamwamba pawo adzakhala ndi (chofunda cha Moto) chowaphimba. Umo ndimomwe Tikuwalipirira anthu osalungama.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَا نُكَلِّفُ نَفۡسًا إِلَّا وُسۡعَهَآ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَنَّةِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Ndipo amene akhulupirira ndikumachita zabwino, sitikakamiza munthu aliyense koma chimene angachithe, awo ndiwo anthu a ku Munda wamtendere. M’menemo iwo akakhala nthawi yaitali.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَنَزَعۡنَا مَا فِي صُدُورِهِم مِّنۡ غِلّٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهِمُ ٱلۡأَنۡهَٰرُۖ وَقَالُواْ ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ ٱلَّذِي هَدَىٰنَا لِهَٰذَا وَمَا كُنَّا لِنَهۡتَدِيَ لَوۡلَآ أَنۡ هَدَىٰنَا ٱللَّهُۖ لَقَدۡ جَآءَتۡ رُسُلُ رَبِّنَا بِٱلۡحَقِّۖ وَنُودُوٓاْ أَن تِلۡكُمُ ٱلۡجَنَّةُ أُورِثۡتُمُوهَا بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Ndipo tidzachotsa kusakondana (komwe kudali) m’mitima mwawo; (adzakhala okondana ngakhale pa dziko lapansi adali odana), uku pansi ndi patsogolo pawo mitsinje ikuyenda; ndipo adzanena (m’kuthokoza kwawo): “Kuyamikidwa konse nkwa Allah, Yemwe adatitsogolera ku ichi (chomwe chatidzetsera mtendere). Sitikadaongoka pakadapanda Allah kutiongola. Atumiki a Mbuye wathu adadza ndi choonadi.” Ndipo adzaitanidwa (ndi kuuzidwa kuti): “Uwu ndi Munda wamtendere umene mwapatsidwa chifukwa cha zomwe mudali kuchita.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَنَادَىٰٓ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَنَّةِ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ أَن قَدۡ وَجَدۡنَا مَا وَعَدَنَا رَبُّنَا حَقّٗا فَهَلۡ وَجَدتُّم مَّا وَعَدَ رَبُّكُمۡ حَقّٗاۖ قَالُواْ نَعَمۡۚ فَأَذَّنَ مُؤَذِّنُۢ بَيۡنَهُمۡ أَن لَّعۡنَةُ ٱللَّهِ عَلَى ٱلظَّٰلِمِينَ
Anthu a ku Munda wamtendere adzaitana anthu aku Moto (adzanena kuti): “Ndithudi ife tapeza zimene Mbuye wathu adatilonjeza kuti nzoona. Kodi nanunso mwapeza zomwe Mbuye wanu adakulonjezani kuti nzoona?” (Anthu a ku Moto) adzanena: “Inde.” Choncho wolengeza pakati pawo adzalengeza kuti: “Matembelero a Allah ali pa anthu ochita zoipa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِينَ يَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ وَيَبۡغُونَهَا عِوَجٗا وَهُم بِٱلۡأٓخِرَةِ كَٰفِرُونَ
“Omwe ankaletsa anthu kuyenda pa njira ya Allah nafuna kuikhotetsa njirayo (kuti ioneke yokhota pamaso pa anthu), omwenso sadakhulupirire za tsiku lachimaliziro.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَبَيۡنَهُمَا حِجَابٞۚ وَعَلَى ٱلۡأَعۡرَافِ رِجَالٞ يَعۡرِفُونَ كُلَّۢا بِسِيمَىٰهُمۡۚ وَنَادَوۡاْ أَصۡحَٰبَ ٱلۡجَنَّةِ أَن سَلَٰمٌ عَلَيۡكُمۡۚ لَمۡ يَدۡخُلُوهَا وَهُمۡ يَطۡمَعُونَ
Ndipo pakati pawo (pa anthu a ku Munda wamtendere ndi a ku Moto) padzakhala chotchinga. Ndipo pamwamba pachikweza padzakhala anthu ena (ofanana ntchito zawo zabwino ndi zoyipa) omwe akazindikira onse (a ku Jannah ndi ku Moto), ndi zizindikiro zawo. Ndipo akawaitana anthu a ku Jannah (kuti): “Salaamun Alayikum (mtendere ukhale pa inu).” Koma asanailowe uku ali ndi chikhulupiliro (kuti ailowa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَإِذَا صُرِفَتۡ أَبۡصَٰرُهُمۡ تِلۡقَآءَ أَصۡحَٰبِ ٱلنَّارِ قَالُواْ رَبَّنَا لَا تَجۡعَلۡنَا مَعَ ٱلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo maso awo akakatembenuzidwa (kuyang’ana) ku mbali ya anthu a ku Moto, adzanena: “Mbuye wathu musatiike pamodzi ndi anthu ochita zoipa. (Tikhululukireni zolakwa zathu. Tilowetseni ku Jannah).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَنَادَىٰٓ أَصۡحَٰبُ ٱلۡأَعۡرَافِ رِجَالٗا يَعۡرِفُونَهُم بِسِيمَىٰهُمۡ قَالُواْ مَآ أَغۡنَىٰ عَنكُمۡ جَمۡعُكُمۡ وَمَا كُنتُمۡ تَسۡتَكۡبِرُونَ
Ndipo anthu aja apachikweza adzawaitana anthu (a ku Moto), adzawadziwa ndi zizindikiro zawo, nati: “Sikudakuthandizeni kuchuluka kwanu kuja, ngakhale zija mudali kudzitama nazo.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَهَٰٓؤُلَآءِ ٱلَّذِينَ أَقۡسَمۡتُمۡ لَا يَنَالُهُمُ ٱللَّهُ بِرَحۡمَةٍۚ ٱدۡخُلُواْ ٱلۡجَنَّةَ لَا خَوۡفٌ عَلَيۡكُمۡ وَلَآ أَنتُمۡ تَحۡزَنُونَ
“Kodi awa siaja munkawalumbilira kuti Allah sangawaninkhe chifundo? (Taonani tsopano, auzidwa kuti): “Lowani ku Jannah. Palibe mantha pa inu, ndiponso simudandaula.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَنَادَىٰٓ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِ أَصۡحَٰبَ ٱلۡجَنَّةِ أَنۡ أَفِيضُواْ عَلَيۡنَا مِنَ ٱلۡمَآءِ أَوۡ مِمَّا رَزَقَكُمُ ٱللَّهُۚ قَالُوٓاْ إِنَّ ٱللَّهَ حَرَّمَهُمَا عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ
Naonso anthu a ku Moto adzaitana a ku Jannah (ndikuwauza kuti): “Tatipungulirani madzi kapena chinthu chimene Allah wakupatsani.” (Anthu a ku Jannah) adzanena kuti:“Ndithu Allah waletsa kupereka zonse ziwirizo kwa osakhulupirira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِينَ ٱتَّخَذُواْ دِينَهُمۡ لَهۡوٗا وَلَعِبٗا وَغَرَّتۡهُمُ ٱلۡحَيَوٰةُ ٱلدُّنۡيَاۚ فَٱلۡيَوۡمَ نَنسَىٰهُمۡ كَمَا نَسُواْ لِقَآءَ يَوۡمِهِمۡ هَٰذَا وَمَا كَانُواْ بِـَٔايَٰتِنَا يَجۡحَدُونَ
Omwe adachita chipembedzo chawo kukhala zinthu zopanda pake ndiponso masewero; ndipo udawanyenga moyo wa m’dziko. Choncho, lero Ifenso tiwaiwala (tiwaleka ku Moto) monga momwe adakuiwalira kukumana ndi tsiku lawo ili, ndi chifukwa chakukana kwawo zivumbulutso Zathu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَقَدۡ جِئۡنَٰهُم بِكِتَٰبٖ فَصَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ عِلۡمٍ هُدٗى وَرَحۡمَةٗ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ
Ndithudi, tawabweretsera buku lomwe talifotokoza mwanzeru, lomwe ndichiongoko ndi chifundo kwa anthu okhulupirira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّا تَأۡوِيلَهُۥۚ يَوۡمَ يَأۡتِي تَأۡوِيلُهُۥ يَقُولُ ٱلَّذِينَ نَسُوهُ مِن قَبۡلُ قَدۡ جَآءَتۡ رُسُلُ رَبِّنَا بِٱلۡحَقِّ فَهَل لَّنَا مِن شُفَعَآءَ فَيَشۡفَعُواْ لَنَآ أَوۡ نُرَدُّ فَنَعۡمَلَ غَيۡرَ ٱلَّذِي كُنَّا نَعۡمَلُۚ قَدۡ خَسِرُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ وَضَلَّ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يَفۡتَرُونَ
Kodi chiliponso chomwe akudikilira osati zotsatira zake (za bukulo)? Ndipo tsiku lakudza zotsatira zake, adzanena amene kale sadalilabadire: “Ha! Atumiki a Mbuye wathu adadzadi ndi choonadi (tsopano tikuvomereza). Kodi tingakhale nawo ife aomboli oti atiombole (kwa Mbuye wathu), kapena tingabwezedwe kuti tikachite (zabwino) osati zija tinkachita?” Zoonadi adziononga okha, ndipo zawasowa zabodza zomwe adali kupeka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ رَبَّكُمُ ٱللَّهُ ٱلَّذِي خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ فِي سِتَّةِ أَيَّامٖ ثُمَّ ٱسۡتَوَىٰ عَلَى ٱلۡعَرۡشِۖ يُغۡشِي ٱلَّيۡلَ ٱلنَّهَارَ يَطۡلُبُهُۥ حَثِيثٗا وَٱلشَّمۡسَ وَٱلۡقَمَرَ وَٱلنُّجُومَ مُسَخَّرَٰتِۭ بِأَمۡرِهِۦٓۗ أَلَا لَهُ ٱلۡخَلۡقُ وَٱلۡأَمۡرُۗ تَبَارَكَ ٱللَّهُ رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndithudi, Mbuye wanu ndi Allah Yemwe adalenga thambo ndi nthaka m’masiku asanu ndi limodzi. Kenako adakhazikika pa Arsh (Mpando Wake wachifumu). Amauchita usiku kuti uvindikire usana, zimatsatana mwamsangamsanga. Ndipo dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi nzofewetsedwa, (zikuyenda mogonjera) ndi Lamulo Lake. Dziwani kuti kulenga ndi kulamula Nkwake. Ndithudi, watukuka Allah Mbuye Wazolengedwa (zonse).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱدۡعُواْ رَبَّكُمۡ تَضَرُّعٗا وَخُفۡيَةًۚ إِنَّهُۥ لَا يُحِبُّ ٱلۡمُعۡتَدِينَ
Mpempheni Mbuye wanu modzichepetsa ndi mwakachetechete. Ndithu Iye sakonda opyola malire.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَا تُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ بَعۡدَ إِصۡلَٰحِهَا وَٱدۡعُوهُ خَوۡفٗا وَطَمَعًاۚ إِنَّ رَحۡمَتَ ٱللَّهِ قَرِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo musaononge pa dziko pambuyo popakonza. Mpempheni (Allah) mwamantha ndi mwakhumbo. Ndithu chifundo cha Allah chili pafupi kwa (anthu Ake ) ochita zabwino.[184]
[184] Chifundo cha Allah chimawafika anthu omwe amachitiranso chifundo anzawo. Ndipo amene sachitira anzawo chifundo sangapezenso chifundo cha Allah. Choncho tiyeni tilimbikire kuthandiza ofooka ndi osowa chithandizo. Ngati sititero ndiye kuti chifundo cha Allah chidzakhala kutali nafe.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَهُوَ ٱلَّذِي يُرۡسِلُ ٱلرِّيَٰحَ بُشۡرَۢا بَيۡنَ يَدَيۡ رَحۡمَتِهِۦۖ حَتَّىٰٓ إِذَآ أَقَلَّتۡ سَحَابٗا ثِقَالٗا سُقۡنَٰهُ لِبَلَدٖ مَّيِّتٖ فَأَنزَلۡنَا بِهِ ٱلۡمَآءَ فَأَخۡرَجۡنَا بِهِۦ مِن كُلِّ ٱلثَّمَرَٰتِۚ كَذَٰلِكَ نُخۡرِجُ ٱلۡمَوۡتَىٰ لَعَلَّكُمۡ تَذَكَّرُونَ
Ndipo Iye ndi Yemwe amatumiza mphepo kuti ikhale nkhani yosangalatsa patsogolo pa chifundo Chake (mvula), kufikira mphepoyo itasenza mitambo yolemera yomwe tikuitumiza ku dziko lakufa. Ndipo kupyolera mwa iyo tikutsitsa madzi ndipo ndimadzio tikutulutsa mitundu yonse ya zipatso. Momwemo ndimo tidzawaukitsira akufa. (Zonsezi) nkuti inu mukumbukire. [185]
[185] Mmene Allah amaiukitsira nthaka youma ndi madzi amvula, nameretsa mmera wosiyanasiyana, momwemonso ndimo adzawaukitsira akufa. Palibe chimene chingamkanike.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلۡبَلَدُ ٱلطَّيِّبُ يَخۡرُجُ نَبَاتُهُۥ بِإِذۡنِ رَبِّهِۦۖ وَٱلَّذِي خَبُثَ لَا يَخۡرُجُ إِلَّا نَكِدٗاۚ كَذَٰلِكَ نُصَرِّفُ ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يَشۡكُرُونَ
Ndipo m’nthaka yabwino umatuluka mmera wake (mwachangu) mwachilolezo cha Mbuye wake. Ndipo nthaka yomwe ili yoipa siitulutsa (mmera wake) koma movutikira. M’menemo ndi momwe Tikuchifotokozera chivumbulutso momveka kwa anthu oyamika.[186]
[186] Mmene ilili nthaka yopanda chonde pomeretsa mmera movutikira nchimodzimodzi ndi anthu oipa. Nkovuta kuwaika pa njira yabwino. Koma tisatope ndi kutaya mtima nawo. Tiyesetsebe kuwakokera ku njira yabwino.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
لَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا نُوحًا إِلَىٰ قَوۡمِهِۦ فَقَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥٓ إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
Ndithudi, tidamtumiza Nuh kwa anthu ake. (Iye) adati: “E inu anthu anga! Pembedzani Allah. Inu mulibe mulungu wina koma Iye. Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِهِۦٓ إِنَّا لَنَرَىٰكَ فِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Akuluakulu a mwa anthu ake adati: “Ndithu ife tikukuona kuti uli m’kusokera koonekera (potiletsa izi zomwe tidawapeza nazo makolo athu).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ يَٰقَوۡمِ لَيۡسَ بِي ضَلَٰلَةٞ وَلَٰكِنِّي رَسُولٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Iye) adati: “E anthu anga! Palibe kusokera mwa ine. Koma ine ndine Mtumiki wochokera kwa Mbuye wa zolengedwa!”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أُبَلِّغُكُمۡ رِسَٰلَٰتِ رَبِّي وَأَنصَحُ لَكُمۡ وَأَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
“Ndikufikitsa kwa inu uthenga wa Mbuye wanga. Ndiponso ndikukulangizani; ndipo ndikudziwa zochokera kwa Allah zomwe inu simukuzidziwa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَعَجِبۡتُمۡ أَن جَآءَكُمۡ ذِكۡرٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَلَىٰ رَجُلٖ مِّنكُمۡ لِيُنذِرَكُمۡ وَلِتَتَّقُواْ وَلَعَلَّكُمۡ تُرۡحَمُونَ
“Kodi mukudabwa kukudzerani ulaliki wochokera kwa Mbuye wanu kudzera mwa munthu wa mwa inu, (yemwe wadza) kuti akuchenjezeni ndi kuti muope (Allah), ndikutinso muchitiridwe chifundo?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَكَذَّبُوهُ فَأَنجَيۡنَٰهُ وَٱلَّذِينَ مَعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ وَأَغۡرَقۡنَا ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَآۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَوۡمًا عَمِينَ
Koma adamtsutsa. Choncho, tidampulumutsa iye ndi amene adali naye pamodzi m’chombo. Ndipo tidawamiza aja adatsutsa zizindikiro Zathu. Ndithudi, iwo adali anthu akhungu.[187]
[187] Nkhani ya Mneneri Nuh paliponse akuifotokoza motalikitsa. Koma m’sura iyi aifotokoza mwachidule. Ndipo Nuh ndimneneri wakale kwabasi. Iye adali kuwalalikira anthu a ku Iraq. Ndipo m’nthawi imeneyo pafupifupi dziko lonse lapansi chitukuko chidali ku Iraq monga momwe tikuwerengera m’mabuku ambiri yakale.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَإِلَىٰ عَادٍ أَخَاهُمۡ هُودٗاۚ قَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥٓۚ أَفَلَا تَتَّقُونَ
Ndipo kwa Âdi (tidaatumizira) m’bale wawo Hûd. Adati: “E inu Anthu anga! Mpembedzeni Allah. Mulibe mulungu wina koma Iye basi. Kodi simungaope?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦٓ إِنَّا لَنَرَىٰكَ فِي سَفَاهَةٖ وَإِنَّا لَنَظُنُّكَ مِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
Akuluakulu a mwa anthu ake omwe sadakhulupirire adanena: “Ife tili kukuona kuti uli mu uchidzete, ndipo ife tikukuganizira kuti ndiwe m’modzi wa a bodza.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ يَٰقَوۡمِ لَيۡسَ بِي سَفَاهَةٞ وَلَٰكِنِّي رَسُولٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Iye) adati: “E inu anthu anga! Palibe uchidzete mwa ine. Koma ine ndine Mtumiki wochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أُبَلِّغُكُمۡ رِسَٰلَٰتِ رَبِّي وَأَنَا۠ لَكُمۡ نَاصِحٌ أَمِينٌ
“Ndikufikitsa kwa inu uthenga wa Mbuye wanga. Ndipo ine ndine mlangizi wanu (wokufunirani zabwino), wokhulupirika.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَعَجِبۡتُمۡ أَن جَآءَكُمۡ ذِكۡرٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَلَىٰ رَجُلٖ مِّنكُمۡ لِيُنذِرَكُمۡۚ وَٱذۡكُرُوٓاْ إِذۡ جَعَلَكُمۡ خُلَفَآءَ مِنۢ بَعۡدِ قَوۡمِ نُوحٖ وَزَادَكُمۡ فِي ٱلۡخَلۡقِ بَصۜۡطَةٗۖ فَٱذۡكُرُوٓاْ ءَالَآءَ ٱللَّهِ لَعَلَّكُمۡ تُفۡلِحُونَ
“Kodi mukudabwa pokudzerani ulaliki kuchokera kwa Mbuye wanu kupyolera mwa munthu wochokera mwa inu kuti akuchenjezeni? Kumbukirani (mtendere wa Allah) pamene adakuikani kukhala amlowam’malo pambuyo pa anthu a Nuh, ndipo akuonjezerani m’kalengedwe kukhala a misinkhu itali-itali ndi amphamvu. Kumbukiraninso mtendere wa Allah (pothokoza) kuti mupambane.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُوٓاْ أَجِئۡتَنَا لِنَعۡبُدَ ٱللَّهَ وَحۡدَهُۥ وَنَذَرَ مَا كَانَ يَعۡبُدُ ءَابَآؤُنَا فَأۡتِنَا بِمَا تَعِدُنَآ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
Iwo adati: “Kodi watidzera kuti timpembedze Allah Yekha ndikusiya zomwe ankapembedza makolo athu? Tibweretsere chimene ukutilonjezacho ngati uli mmodzi mwa onena zoona.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ قَدۡ وَقَعَ عَلَيۡكُم مِّن رَّبِّكُمۡ رِجۡسٞ وَغَضَبٌۖ أَتُجَٰدِلُونَنِي فِيٓ أَسۡمَآءٖ سَمَّيۡتُمُوهَآ أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُم مَّا نَزَّلَ ٱللَّهُ بِهَا مِن سُلۡطَٰنٖۚ فَٱنتَظِرُوٓاْ إِنِّي مَعَكُم مِّنَ ٱلۡمُنتَظِرِينَ
(Iye) adati: “Palibe chikaiko, chilango ndi mkwiyo wochokera kwa Mbuye wanu zakugwerani. Kodi mukukangana nane pa za maina (a mafano) omwe mudawatcha inu ndi makolo anu, pomwe Allah sadatsitse umboni uliwonse pa milungu yanu yabodzayo? Choncho, dikirani. Inenso ndili pamodzi nanu mwa odikira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَٱلَّذِينَ مَعَهُۥ بِرَحۡمَةٖ مِّنَّا وَقَطَعۡنَا دَابِرَ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَاۖ وَمَا كَانُواْ مُؤۡمِنِينَ
Choncho tidampulumutsa pamodzi ndi amene adali naye mwa chifundo chathu, ndipo tidadula mizu ya omwe adatsutsa zivumbulutso Zathu. Ndipo sadali okhulupirira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِلَىٰ ثَمُودَ أَخَاهُمۡ صَٰلِحٗاۚ قَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥۖ قَدۡ جَآءَتۡكُم بَيِّنَةٞ مِّن رَّبِّكُمۡۖ هَٰذِهِۦ نَاقَةُ ٱللَّهِ لَكُمۡ ءَايَةٗۖ فَذَرُوهَا تَأۡكُلۡ فِيٓ أَرۡضِ ٱللَّهِۖ وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo kwa Asamudu tidamtumiza m’bale wawo Swaleh. Adati: “E inu anthu anga! Gwadirani Allah; inu mulibe mulungu wina koma Iye basi. Chizindikiro chochokera kwa Mbuye wanu chadza kwa inu. Iyi ndi ngamira ya Allah monga chisonyezo chanu (chizizwa chanu), choncho, isiyeni izidya m’dziko la Allah, ndipo musaikhudze ndi choipa kuopera kuti chingakugwereni chilango chowawa kwambiri.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱذۡكُرُوٓاْ إِذۡ جَعَلَكُمۡ خُلَفَآءَ مِنۢ بَعۡدِ عَادٖ وَبَوَّأَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ تَتَّخِذُونَ مِن سُهُولِهَا قُصُورٗا وَتَنۡحِتُونَ ٱلۡجِبَالَ بُيُوتٗاۖ فَٱذۡكُرُوٓاْ ءَالَآءَ ٱللَّهِ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo kumbukirani pamene (Allah) adakupangani kukhala amlowammalo pambuyo pa mtundu wa Âdi. Ndipo adakukhazikani pa dziko (mwa ubwino). Mukudzimangira nyumba zikuluzikulu mchigwa, ndiponso kusema ndi kuboola mapiri kukhala nyumba. Choncho kumbukirani mtendere wa Allah, ndipo musaononge pa dziko pofalitsa chisokonezo.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦ لِلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِمَنۡ ءَامَنَ مِنۡهُمۡ أَتَعۡلَمُونَ أَنَّ صَٰلِحٗا مُّرۡسَلٞ مِّن رَّبِّهِۦۚ قَالُوٓاْ إِنَّا بِمَآ أُرۡسِلَ بِهِۦ مُؤۡمِنُونَ
Adanena akuluakulu omwe adali odzitukumula mwa anthu ake kuuza omwe adaponderezedwa kwa amene adakhulupirira mwa iwo: “Kodi muli ndi chitsimikizo kuti Swalih ngotumizidwa ndi Mbuye Wake (wapatsidwa utumiki)?” (Iwo) Adati: “Ndithu ife tikukhulupirira zomwe watumidwa nazo (kuzifikitsa kwa ife).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُوٓاْ إِنَّا بِٱلَّذِيٓ ءَامَنتُم بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Omwe adadzitukumula adati: “Ndithu ife tikuzikana zomwe mwazikhulupirirazo.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَعَقَرُواْ ٱلنَّاقَةَ وَعَتَوۡاْ عَنۡ أَمۡرِ رَبِّهِمۡ وَقَالُواْ يَٰصَٰلِحُ ٱئۡتِنَا بِمَا تَعِدُنَآ إِن كُنتَ مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Choncho adaipha (adaizinga) ngamira ndi kunyoza lamulo la Mbuye wawo, nati: “E iwe Swaleh! Tibweletsere (chilango) chimene wakhala ukutilonjeza ngati ulidi mmodzi wa otumidwa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلرَّجۡفَةُ فَأَصۡبَحُواْ فِي دَارِهِمۡ جَٰثِمِينَ
Choncho, chivomerezi chidawagwira mwadzidzidzi, adapezeka ali akufa chigwadire m’nyumba zawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰقَوۡمِ لَقَدۡ أَبۡلَغۡتُكُمۡ رِسَالَةَ رَبِّي وَنَصَحۡتُ لَكُمۡ وَلَٰكِن لَّا تُحِبُّونَ ٱلنَّٰصِحِينَ
Tero, Swalih adawasiya (nkupita kwina kwake) uku akunena: “E anthu anga! Ndidafikitsadi uthenga wa Mbuye wanga kwa inu. Ndipo Ndidakuchenjezani ndi kukulangizani. Koma inu simufuna alangizi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلُوطًا إِذۡ قَالَ لِقَوۡمِهِۦٓ أَتَأۡتُونَ ٱلۡفَٰحِشَةَ مَا سَبَقَكُم بِهَا مِنۡ أَحَدٖ مِّنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Nayenso Luti (tidamtuma, ndipo kumbuka) pamene adati kwa anthu ake: “Kodi mukuchita chonyansa chomwe sadakutsogolereni aliyense kuchichita mwa anthu akale m’zolengedwa zonse?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّكُمۡ لَتَأۡتُونَ ٱلرِّجَالَ شَهۡوَةٗ مِّن دُونِ ٱلنِّسَآءِۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٞ مُّسۡرِفُونَ
“Ndithu inu mukuwadzera amuna mwa chilakolako kusiya akazi! Ndithudi, inu ndinu anthu olumpha malire.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا كَانَ جَوَابَ قَوۡمِهِۦٓ إِلَّآ أَن قَالُوٓاْ أَخۡرِجُوهُم مِّن قَرۡيَتِكُمۡۖ إِنَّهُمۡ أُنَاسٞ يَتَطَهَّرُونَ
Kuyankha kwa anthu ake sikudali kwa mtundu wina koma kuti: “Apirikitseni m’mudzi wanu. Ndithu iwowo ndi anthu odziyeretsa. (Choncho akhaliranji m’mudzi wa uve? Akakhale ndi anzawo ochita zaukhondo).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ إِلَّا ٱمۡرَأَتَهُۥ كَانَتۡ مِنَ ٱلۡغَٰبِرِينَ
Koma tidampulumutsa iye ndi banja lake, kupatula mkazi wake; adali m’gulu la otsalira m’mbuyo (adaonongeka).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَٱنظُرۡ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Ndipo tidatsakamula pa iwo chimvula (cha miyala). Choncho, taona mmene adaliri mapeto a anthu oipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِلَىٰ مَدۡيَنَ أَخَاهُمۡ شُعَيۡبٗاۚ قَالَ يَٰقَوۡمِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥۖ قَدۡ جَآءَتۡكُم بَيِّنَةٞ مِّن رَّبِّكُمۡۖ فَأَوۡفُواْ ٱلۡكَيۡلَ وَٱلۡمِيزَانَ وَلَا تَبۡخَسُواْ ٱلنَّاسَ أَشۡيَآءَهُمۡ وَلَا تُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ بَعۡدَ إِصۡلَٰحِهَاۚ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Nakonso kwa anthu aku Madiyan, (tidamtumiza) m’bale wawo Shuaib. Adati: “E inu anthu Anga! Gwadirani Allah. Mulibe mulungu wina koma Iye basi. Umboni owonekera wadza kuchokera kwa Mbuye wanu. Choncho pimani miyeso (yanu ya mbale) ndi masikelo mwachilungamo. Musawachepetsere anthu zinthu zawo; ndipo musaononge pa dziko pamhuyo polikonza. Kutero ndi kwabwino kwa inu ngati muli okhulupiriradi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَا تَقۡعُدُواْ بِكُلِّ صِرَٰطٖ تُوعِدُونَ وَتَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ مَنۡ ءَامَنَ بِهِۦ وَتَبۡغُونَهَا عِوَجٗاۚ وَٱذۡكُرُوٓاْ إِذۡ كُنتُمۡ قَلِيلٗا فَكَثَّرَكُمۡۖ وَٱنظُرُواْ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُفۡسِدِينَ
“Ndipo musamawakhalire anthu pa njira iliyonse mowabisalira ndi kumawaopseza, ndi kuwatsekereza kuyenda pa njira ya Allah amene amkhulupirira Iye, ndi kufuna kuikhotetsa njirayo (kuti anthu asaitsate). Ndipo kumbukirani pamene mudali ochepa nakuchulukitsani. Ndipo onani momwe adalili mapeto a owononga.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِن كَانَ طَآئِفَةٞ مِّنكُمۡ ءَامَنُواْ بِٱلَّذِيٓ أُرۡسِلۡتُ بِهِۦ وَطَآئِفَةٞ لَّمۡ يُؤۡمِنُواْ فَٱصۡبِرُواْ حَتَّىٰ يَحۡكُمَ ٱللَّهُ بَيۡنَنَاۚ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلۡحَٰكِمِينَ
“Ndipo ngati pali gulu la anthu mwa inu amene akhulupirira uthenga umene ndatumidwa nawo, ndi gulu la anthu limene silidakhulupirire, pirirani mpaka Allah aweruze pakati pathu. Iye Ngwabwino poweruza kuposa oweruza.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ قَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦ لَنُخۡرِجَنَّكَ يَٰشُعَيۡبُ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَكَ مِن قَرۡيَتِنَآ أَوۡ لَتَعُودُنَّ فِي مِلَّتِنَاۚ قَالَ أَوَلَوۡ كُنَّا كَٰرِهِينَ
۞ Akuluakulu omwe adadzikuza mwa anthu ake, adanena: “Tikupirikitsa, iwe Shuaib m’mudzi mwathu muno ndi amene akhulupirira pamodzi nawe, pokhapokha mutabwerera ku chipembedzo chathu.” (Iye) adati: “Kodi ngakhale kuti tikuchida?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَدِ ٱفۡتَرَيۡنَا عَلَى ٱللَّهِ كَذِبًا إِنۡ عُدۡنَا فِي مِلَّتِكُم بَعۡدَ إِذۡ نَجَّىٰنَا ٱللَّهُ مِنۡهَاۚ وَمَا يَكُونُ لَنَآ أَن نَّعُودَ فِيهَآ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُ رَبُّنَاۚ وَسِعَ رَبُّنَا كُلَّ شَيۡءٍ عِلۡمًاۚ عَلَى ٱللَّهِ تَوَكَّلۡنَاۚ رَبَّنَا ٱفۡتَحۡ بَيۡنَنَا وَبَيۡنَ قَوۡمِنَا بِٱلۡحَقِّ وَأَنتَ خَيۡرُ ٱلۡفَٰتِحِينَ
“Ngati titabwerera m’chipembedzo chanu pambuyo potipulumutsa Allah m’menemo, ndiye kuti tampekera Allah bodza. Sikungatheke kwa ife kubwerera m’chipembedzo chimenecho pokhapokha atafuna Allah, Mbuye wathu. Mbuye wathu Ngodziwa zonse. Ndipo kwa Allah Yekha ndiko tayadzamira. Mbuye wathu! Weruzani mwa choonadi pakati pathu ndi pakati pa anthu athu. Inu Ngabwino poweruza kuposa oweruza.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦ لَئِنِ ٱتَّبَعۡتُمۡ شُعَيۡبًا إِنَّكُمۡ إِذٗا لَّخَٰسِرُونَ
Ndipo akuluakulu mwa anthu ake omwe sadakhulupirire adati: “Ngati mutsatira Shuaib ndithudi pamenepo ndiye kuti mukhala otayika.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلرَّجۡفَةُ فَأَصۡبَحُواْ فِي دَارِهِمۡ جَٰثِمِينَ
Choncho chivomerezi chidawaononga mwadzidzidzi motero adapezeka akufa chigwadire mnyumba zawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ شُعَيۡبٗا كَأَن لَّمۡ يَغۡنَوۡاْ فِيهَاۚ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ شُعَيۡبٗا كَانُواْ هُمُ ٱلۡخَٰسِرِينَ
Amene adamutsutsa Shuaib adakhala ngati sadakhalepo m’mudzimo. Amene adamutsutsa Shuaib ndi omwe adali otayika.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰقَوۡمِ لَقَدۡ أَبۡلَغۡتُكُمۡ رِسَٰلَٰتِ رَبِّي وَنَصَحۡتُ لَكُمۡۖ فَكَيۡفَ ءَاسَىٰ عَلَىٰ قَوۡمٖ كَٰفِرِينَ
(Pamene nthawi yakuonongeka kwawo idayandikira, Shuaib adatuluka m’mudzimo pamodzi ndi aja adakhulupirira) nawasiya oipawo (kunka kutali) uku akunena: “E inu anthu anga! Ndinafikitsadi uthenga wa Mbuye wanga ndipo ndinakuchenjezani ndiye nchotani ndidandaule za anthu okanira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا فِي قَرۡيَةٖ مِّن نَّبِيٍّ إِلَّآ أَخَذۡنَآ أَهۡلَهَا بِٱلۡبَأۡسَآءِ وَٱلضَّرَّآءِ لَعَلَّهُمۡ يَضَّرَّعُونَ
Ndipo palibe pamene tidamtuma mneneri aliyense m’mudzi uliwonse (nkumukana) koma tinkawalanga eni mudziwo ndi masautso ndi mavuto kuti afatse (ndi kulambira Allah; koma ayi adakanika).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ثُمَّ بَدَّلۡنَا مَكَانَ ٱلسَّيِّئَةِ ٱلۡحَسَنَةَ حَتَّىٰ عَفَواْ وَّقَالُواْ قَدۡ مَسَّ ءَابَآءَنَا ٱلضَّرَّآءُ وَٱلسَّرَّآءُ فَأَخَذۡنَٰهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Kenako tinasintha pamalo pa choipa pobweretsapo chabwino, (tidawachotsera masautso ndi mavuto ngakhale sadali okhulupirira) mpaka anachuluka, ndi kuchulukanso chuma chawo; anayamba kunena kuti: “Masautso ndi mavuto adawakhudzaponso makolo athu. (Zoterezi sizachilendo kwa ife).” Choncho tidawaononga mwadzidzidzi asakudziwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَوۡ أَنَّ أَهۡلَ ٱلۡقُرَىٰٓ ءَامَنُواْ وَٱتَّقَوۡاْ لَفَتَحۡنَا عَلَيۡهِم بَرَكَٰتٖ مِّنَ ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِ وَلَٰكِن كَذَّبُواْ فَأَخَذۡنَٰهُم بِمَا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Chikhala kuti eni midziwo adakhulupirira naopa (Allah pamene aneneri adawadzera), tikadawatsekulira madalitso ochokera kumwamba ndi pansi. Koma adatsutsa (aneneri) ndipo tidawaononga chifukwa cha zoipa zomwe ankachita.[188]
[188] Apa tanthauzo lake nkuti akanapeza mtendere wambiri pompano padziko lapansi akadakhala kuti adali olungama.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَفَأَمِنَ أَهۡلُ ٱلۡقُرَىٰٓ أَن يَأۡتِيَهُم بَأۡسُنَا بَيَٰتٗا وَهُمۡ نَآئِمُونَ
Kodi anthu a m’mizinda (iyo momwe muli anthu oipa) ali ndi chitetezo cholimba kuti chilango chathu sichingawadzere usiku iwo ali mtulo?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَأَمِنَ أَهۡلُ ٱلۡقُرَىٰٓ أَن يَأۡتِيَهُم بَأۡسُنَا ضُحٗى وَهُمۡ يَلۡعَبُونَ
Kapena anthu a m’mizindayo ali ndi chitetezo cholimba kuti chilango Chathu sichingawafike masana uku iwo akusewera?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَفَأَمِنُواْ مَكۡرَ ٱللَّهِۚ فَلَا يَأۡمَنُ مَكۡرَ ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡقَوۡمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
Kodi akudziika pa chitetezo ku chilango cha Allah? Sangadziike pa chitetezo ku chilango cha Allah kupatula anthu otayika basi.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَلَمۡ يَهۡدِ لِلَّذِينَ يَرِثُونَ ٱلۡأَرۡضَ مِنۢ بَعۡدِ أَهۡلِهَآ أَن لَّوۡ نَشَآءُ أَصَبۡنَٰهُم بِذُنُوبِهِمۡۚ وَنَطۡبَعُ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ فَهُمۡ لَا يَسۡمَعُونَ
Kodi sadadziwe awa omwe alandira dziko molowa mmalo pambuyo pa eni dzikolo (anthu akale) kuti tikadafuna tikadawaika m’masautso chifukwa cha machimo awo ndi kuwadinda mitima yawo kotero iwo sakadamva (kanthu)?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
تِلۡكَ ٱلۡقُرَىٰ نَقُصُّ عَلَيۡكَ مِنۡ أَنۢبَآئِهَاۚ وَلَقَدۡ جَآءَتۡهُمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ فَمَا كَانُواْ لِيُؤۡمِنُواْ بِمَا كَذَّبُواْ مِن قَبۡلُۚ كَذَٰلِكَ يَطۡبَعُ ٱللَّهُ عَلَىٰ قُلُوبِ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Iyo ndi midzi (ikuluikulu) yomwe tikukusimbira iwe zina mwa nkhani zake. Ndithudi, adawadzera atumiki awo ndi zizindikiro (zoonekera poyera zosonyeza kuti iwo ndi atumiki a Allah). Koma sadali oti nkukhulupirira pa zomwe adazitsutsapo kale. Umo ndi mmene Allah amadindira ndi kuitseka mitima ya osakhulupirira (kotero kuti sangathandizike ndi malangizo a mtundu uliwonse).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا وَجَدۡنَا لِأَكۡثَرِهِم مِّنۡ عَهۡدٖۖ وَإِن وَجَدۡنَآ أَكۡثَرَهُمۡ لَفَٰسِقِينَ
Ndipo ambiri a iwo sitidawapeze akukwaniritsa lonjezo lililonse koma tidawapeza ambiri a iwo ali opandukira (chilamulo cha Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ثُمَّ بَعَثۡنَا مِنۢ بَعۡدِهِم مُّوسَىٰ بِـَٔايَٰتِنَآ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ وَمَلَإِيْهِۦ فَظَلَمُواْ بِهَاۖ فَٱنظُرۡ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُفۡسِدِينَ
Kenako pambuyo pawo (aneneriwo) tidamtumiza Mûsa pamodzi ndi zizindikiro Zathu kwa Farawo ndi nduna zake, koma adazikana (zizindikirozo). Choncho taona momwe adalili mathero aoononga.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَالَ مُوسَىٰ يَٰفِرۡعَوۡنُ إِنِّي رَسُولٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo Mûsa adati: “E iwe Farawo! Ndithu ine ndine mthenga wochokera kwa Mbuye wa zolengedwa zonse.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
حَقِيقٌ عَلَىٰٓ أَن لَّآ أَقُولَ عَلَى ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡحَقَّۚ قَدۡ جِئۡتُكُم بِبَيِّنَةٖ مِّن رَّبِّكُمۡ فَأَرۡسِلۡ مَعِيَ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“Ndikofunika kwa ine kuti ndisamnenere Allah chilichonse koma choonadi basi. Ndithu ndakudzerani ndi chizindikiro choonekera kuchokera kwa Mbuye wanu. Choncho, aleke ndinke nawo ana a Israyeli.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ إِن كُنتَ جِئۡتَ بِـَٔايَةٖ فَأۡتِ بِهَآ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Farawo) adati: “Ngati wadza ndi chizindikiro, bwera nacho (tichione), ngati iwe ulidi mmodzi wa onena zoona.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَلۡقَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ ثُعۡبَانٞ مُّبِينٞ
Choncho adaponya ndodo yake pansi. Mwadzidzidzi, idasanduka njoka yooneka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَنَزَعَ يَدَهُۥ فَإِذَا هِيَ بَيۡضَآءُ لِلنَّٰظِرِينَ
Ndipo adatulutsa dzanja lake pompo lidakhala loyera, lowala kwa oliona.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِ فِرۡعَوۡنَ إِنَّ هَٰذَا لَسَٰحِرٌ عَلِيمٞ
Nduna za mwa anthu a Farawo zidati: “Ndithu uyu ndi wamatsenga wodziwa (kwambiri zamatsenga).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يُرِيدُ أَن يُخۡرِجَكُم مِّنۡ أَرۡضِكُمۡۖ فَمَاذَا تَأۡمُرُونَ
“Akufuna kukusamutsani mdziko mwanu. Nanga mukulangiza zotani?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُوٓاْ أَرۡجِهۡ وَأَخَاهُ وَأَرۡسِلۡ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
(Iwo) adati (kwa Farawo): “Muleke pang’ono iye ndi m’bale wakeyu (usawaphe); ndipo tumiza osonkhanitsa m’mizinda kuti akusonkhanitsire (amatsenga onse akuluakulu).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَأۡتُوكَ بِكُلِّ سَٰحِرٍ عَلِيمٖ
“Kuti akubweretsere wamatsenga aliyense wodziwa kwambiri.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَجَآءَ ٱلسَّحَرَةُ فِرۡعَوۡنَ قَالُوٓاْ إِنَّ لَنَا لَأَجۡرًا إِن كُنَّا نَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Amatsenga adadza kwa Farawo; nati: “Kodi ife tipeza malipiro ngati titapambana?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ نَعَمۡ وَإِنَّكُمۡ لَمِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
(Farawo) adati: “Inde, ndipo mudzakhala mwa oyandikitsidwa (mudzakhala nduna zanga).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُواْ يَٰمُوسَىٰٓ إِمَّآ أَن تُلۡقِيَ وَإِمَّآ أَن نَّكُونَ نَحۡنُ ٱلۡمُلۡقِينَ
(Amatsenga) adati: “E iwe Mûsa! Kodi uyamba kuponya ndiwe (matsenga ako pamaso pa anthu), kapena ife tikhale oyambilira kuponya?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ أَلۡقُواْۖ فَلَمَّآ أَلۡقَوۡاْ سَحَرُوٓاْ أَعۡيُنَ ٱلنَّاسِ وَٱسۡتَرۡهَبُوهُمۡ وَجَآءُو بِسِحۡرٍ عَظِيمٖ
Mûsa adati: “Ponyani.” Choncho pamene adaponya adalodza maso a anthu ndikuwaopseza. Ndipo adadza ndi matsenga aakulu zedi.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنۡ أَلۡقِ عَصَاكَۖ فَإِذَا هِيَ تَلۡقَفُ مَا يَأۡفِكُونَ
Ndipo tidamzindikiritsa Mûsa ndi chivumbulutso (kuti): “Ponya ndodo yako.” Pompo iyo idameza zamatsengazo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَوَقَعَ ٱلۡحَقُّ وَبَطَلَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Choncho, choonadi chidatsimikizika, ndipo zidapita pachabe zomwe ankachita.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَغُلِبُواْ هُنَالِكَ وَٱنقَلَبُواْ صَٰغِرِينَ
Choncho adagonjetsedwa pamenepo, nakhala onyozeka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأُلۡقِيَ ٱلسَّحَرَةُ سَٰجِدِينَ
Ndipo amatsenga adadzigwetsa uku akulambira (Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Takhulupirira Mbuye wa zolengedwa zonse.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa Ndi Harun.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ ءَامَنتُم بِهِۦ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّ هَٰذَا لَمَكۡرٞ مَّكَرۡتُمُوهُ فِي ٱلۡمَدِينَةِ لِتُخۡرِجُواْ مِنۡهَآ أَهۡلَهَاۖ فَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Farawo adati: “Mwamkhulupirira chotani iye ndisanakupatseni chilolezo? Ndithu iyi ndi ndale yomwe mwaichita mu mzindamu (inu ndi Mûsa) kuti muwatulutsemo eni mzindawo. Koma posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ ثُمَّ لَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
“Ndithudi, nditseteka manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa; (kudula dzanja lakudzanjadzanja ndi mwendo wa kumanzere, kapena dzanja la kumanzere ndi mwendo wakudzanjadzanja). Kenako ndikupachikani nonsenu.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُوٓاْ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Iwo) adati: “Ndithu ife kwa Mbuye wathu ngobwerera.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا تَنقِمُ مِنَّآ إِلَّآ أَنۡ ءَامَنَّا بِـَٔايَٰتِ رَبِّنَا لَمَّا جَآءَتۡنَاۚ رَبَّنَآ أَفۡرِغۡ عَلَيۡنَا صَبۡرٗا وَتَوَفَّنَا مُسۡلِمِينَ
“Komatu palibe choipa chimene waona mwa ife kupatula kuti takhulupirira zizindikiro za Mbuye wathu pamene zatidzera. E Mbuye wathu! Titsanulireni chipiliro, ndipo tipatseni imfa uku tili Asilamu (ogonjera Inu).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِ فِرۡعَوۡنَ أَتَذَرُ مُوسَىٰ وَقَوۡمَهُۥ لِيُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَيَذَرَكَ وَءَالِهَتَكَۚ قَالَ سَنُقَتِّلُ أَبۡنَآءَهُمۡ وَنَسۡتَحۡيِۦ نِسَآءَهُمۡ وَإِنَّا فَوۡقَهُمۡ قَٰهِرُونَ
Ndipo nduna za mwa anthu a Farawo zidati (kwa Farawo): “Kodi umuleka Mûsa ndi anthu ake kuti abwere ndi chisokonezo m’dziko, ndi kuti akusiye iwe ndi milungu yako (yomwe adatilangiza makolo athu kuti tipembedze pamodzi ndi iwe)? (Farawo) Adati: “Tipha ana awo achimuna ndikuwasiya amoyo (ana awo) achikazi. Ndithudi ife pa iwo tili ndi mphamvu zowagonjetsera.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِ ٱسۡتَعِينُواْ بِٱللَّهِ وَٱصۡبِرُوٓاْۖ إِنَّ ٱلۡأَرۡضَ لِلَّهِ يُورِثُهَا مَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦۖ وَٱلۡعَٰقِبَةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Mûsa adauza anthu ake: “Pemphani chithandizo kwa Allah, ndipo pirirani. Ndithu dzikoli ndi la Allah; amalipereka kwa amene wamfuna mwa akapolo Ake. Ndipo mapeto abwino nga anthu olungama.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالُوٓاْ أُوذِينَا مِن قَبۡلِ أَن تَأۡتِيَنَا وَمِنۢ بَعۡدِ مَا جِئۡتَنَاۚ قَالَ عَسَىٰ رَبُّكُمۡ أَن يُهۡلِكَ عَدُوَّكُمۡ وَيَسۡتَخۡلِفَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَيَنظُرَ كَيۡفَ تَعۡمَلُونَ
(Iwo) adati: “Takhala tikuzunzidwa usanatidzere ndiponso (tsopano) pamene watidzera.” (Mûsa) adati: “Mwina Mbuye wanu amuononga mdani wanu ndipo akuchitani kukhala alowammalo m’dzikoli, ndi kuti aone mmene mungachitire.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَقَدۡ أَخَذۡنَآ ءَالَ فِرۡعَوۡنَ بِٱلسِّنِينَ وَنَقۡصٖ مِّنَ ٱلثَّمَرَٰتِ لَعَلَّهُمۡ يَذَّكَّرُونَ
Ndithu tidawakhaulitsa anthu a Farawo ndi chilala, ndi kuchepekedwa zokolola; kuti mwina angakumbukire.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَإِذَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡحَسَنَةُ قَالُواْ لَنَا هَٰذِهِۦۖ وَإِن تُصِبۡهُمۡ سَيِّئَةٞ يَطَّيَّرُواْ بِمُوسَىٰ وَمَن مَّعَهُۥٓۗ أَلَآ إِنَّمَا طَٰٓئِرُهُمۡ عِندَ ٱللَّهِ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
(Adali chonchi): Ubwino ukawadzera, amati: “Ubwinowu nchifukwa cha zochita zathu zabwino.” Ndipo choipa chikawadzera, amakankhira kwa Mûsa ndi amene adali naye. (Amati iye ndiye wadzetsa tsokalo chifukwa choisambula milungu yawo). Dziwani kuti tsoka lawo limachokera kwa Allah (chifukwa cha zochita zawo zoipa). Koma ambiri a iwo sazindikira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَالُواْ مَهۡمَا تَأۡتِنَا بِهِۦ مِنۡ ءَايَةٖ لِّتَسۡحَرَنَا بِهَا فَمَا نَحۡنُ لَكَ بِمُؤۡمِنِينَ
Ndipo adati (kwa Mûsa): “Chisonyezo chilichonse chimene ungatibweretsere kuti utilodze nacho (siupindula kanthu). Ifetu sitikukhulupirira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمُ ٱلطُّوفَانَ وَٱلۡجَرَادَ وَٱلۡقُمَّلَ وَٱلضَّفَادِعَ وَٱلدَّمَ ءَايَٰتٖ مُّفَصَّلَٰتٖ فَٱسۡتَكۡبَرُواْ وَكَانُواْ قَوۡمٗا مُّجۡرِمِينَ
Choncho, tidawatumizira chigumula, (mliri wa) dzombe, nsabwe, achule ndi magazi monga zizindikiro zosiyanasiyana. Koma adadzikuza; ndipo adali anthu oipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَمَّا وَقَعَ عَلَيۡهِمُ ٱلرِّجۡزُ قَالُواْ يَٰمُوسَى ٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ بِمَا عَهِدَ عِندَكَۖ لَئِن كَشَفۡتَ عَنَّا ٱلرِّجۡزَ لَنُؤۡمِنَنَّ لَكَ وَلَنُرۡسِلَنَّ مَعَكَ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Pamene chilango chidawakhudza, amati: “E iwe Mûsa! Tipemphere kwa Mbuye wako pa zomwe adakulonjeza. Ngati utichotsera chilangochi, ndithudi tikukhulupirira, ndipo tiwatumiza pamodzi nawe ana a Israyeli (kuti unke nawo kumene ukufuna).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَمَّا كَشَفۡنَا عَنۡهُمُ ٱلرِّجۡزَ إِلَىٰٓ أَجَلٍ هُم بَٰلِغُوهُ إِذَا هُمۡ يَنكُثُونَ
Koma pamene tidawachotsera chilangocho kufikira nthawi yawo yomwe iwo amayenera kuifika, pompo iwo adaswa lonjezo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَٱنتَقَمۡنَا مِنۡهُمۡ فَأَغۡرَقۡنَٰهُمۡ فِي ٱلۡيَمِّ بِأَنَّهُمۡ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَكَانُواْ عَنۡهَا غَٰفِلِينَ
Choncho, tidawabwezera chilango ndikuwamiza m’nyanja chifukwa chakuti iwo adatsutsa zizindikiro Zathu, ndipo sadali ozilabadira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأَوۡرَثۡنَا ٱلۡقَوۡمَ ٱلَّذِينَ كَانُواْ يُسۡتَضۡعَفُونَ مَشَٰرِقَ ٱلۡأَرۡضِ وَمَغَٰرِبَهَا ٱلَّتِي بَٰرَكۡنَا فِيهَاۖ وَتَمَّتۡ كَلِمَتُ رَبِّكَ ٱلۡحُسۡنَىٰ عَلَىٰ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ بِمَا صَبَرُواْۖ وَدَمَّرۡنَا مَا كَانَ يَصۡنَعُ فِرۡعَوۡنُ وَقَوۡمُهُۥ وَمَا كَانُواْ يَعۡرِشُونَ
Ndipo anthu omwe adali kuponderezedwa tidawachita kukhala amlowammalo a kuvuma kwa dziko ndi kuzambwe kwake, lomwe tidaikamo madalitso (ambiri). Ndipo mawu abwino a Mbuye wako adakwaniritsidwa kwa ana a Israyeli chifukwa cha kupirira kwawo (pa zomwe adakumana nazo). Ndipo tidazigumula ndi kuziononga zomwe Farawo ndi anthu ake ankapanga ndi zomwe ankamanga.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَجَٰوَزۡنَا بِبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ ٱلۡبَحۡرَ فَأَتَوۡاْ عَلَىٰ قَوۡمٖ يَعۡكُفُونَ عَلَىٰٓ أَصۡنَامٖ لَّهُمۡۚ قَالُواْ يَٰمُوسَى ٱجۡعَل لَّنَآ إِلَٰهٗا كَمَا لَهُمۡ ءَالِهَةٞۚ قَالَ إِنَّكُمۡ قَوۡمٞ تَجۡهَلُونَ
Ndipo tidawaolotsa ana a Israyeli pa nyanja (ndi kupulumuka ku masautso a Farawo), nadza kwa anthu omwe adali kupembedza mafano awo. (Iwo) adati: “E iwe Mûsa! Nafenso tipangire mulungu (wamafano) monga milungu yomwe ali nayo iwo.” (Mneneri Mûsa) adati: “Ndithudi, inu ndinu anthu osazindikira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ مُتَبَّرٞ مَّا هُمۡ فِيهِ وَبَٰطِلٞ مَّا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
“Ndithudi awa aonongedwa m’zomwe ali nazozi, ndiponso ndizachabe zomwe akhala akuchita.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ أَغَيۡرَ ٱللَّهِ أَبۡغِيكُمۡ إِلَٰهٗا وَهُوَ فَضَّلَكُمۡ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Kodi ndikufunireni mulungu wina kusiya Allah chikhalirecho Iye wakuchitirani zabwino zoposa pa zolengedwa zonse?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذۡ أَنجَيۡنَٰكُم مِّنۡ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ يَسُومُونَكُمۡ سُوٓءَ ٱلۡعَذَابِ يُقَتِّلُونَ أَبۡنَآءَكُمۡ وَيَسۡتَحۡيُونَ نِسَآءَكُمۡۚ وَفِي ذَٰلِكُم بَلَآءٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَظِيمٞ
Ndipo kumbukirani pamene tidakupulumutsani (m’manja) mwa anthu a Farawo omwe adali kukuzunzani ndi chilango choyipa ndipo anali kupha ana anu aamuna ndi kusiya ana anu aakazi. Pa ichi padali mayeso aakulu ochokera kwa Mbuye wanu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَوَٰعَدۡنَا مُوسَىٰ ثَلَٰثِينَ لَيۡلَةٗ وَأَتۡمَمۡنَٰهَا بِعَشۡرٖ فَتَمَّ مِيقَٰتُ رَبِّهِۦٓ أَرۡبَعِينَ لَيۡلَةٗۚ وَقَالَ مُوسَىٰ لِأَخِيهِ هَٰرُونَ ٱخۡلُفۡنِي فِي قَوۡمِي وَأَصۡلِحۡ وَلَا تَتَّبِعۡ سَبِيلَ ٱلۡمُفۡسِدِينَ
Ndipo tidamlonjeza Mûsa masiku makumi atatu (kuti achite mapemphero kuti kenako timpatse Taurat). Ndipo tidawakwaniritsa ndi masiku khumi; chomwecho lidakwanira pangano la Mbuye wake (lopita kukampatsa Tauratiyo) m’masiku makumi anayi. Ndipo Mûsa adati kwa m’bale wake Harun: “Lowa m’malo mwanga pa (kuwatsogolera) anthu angawa. Ndipo konza; usatsate njira ya oononga.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَمَّا جَآءَ مُوسَىٰ لِمِيقَٰتِنَا وَكَلَّمَهُۥ رَبُّهُۥ قَالَ رَبِّ أَرِنِيٓ أَنظُرۡ إِلَيۡكَۚ قَالَ لَن تَرَىٰنِي وَلَٰكِنِ ٱنظُرۡ إِلَى ٱلۡجَبَلِ فَإِنِ ٱسۡتَقَرَّ مَكَانَهُۥ فَسَوۡفَ تَرَىٰنِيۚ فَلَمَّا تَجَلَّىٰ رَبُّهُۥ لِلۡجَبَلِ جَعَلَهُۥ دَكّٗا وَخَرَّ مُوسَىٰ صَعِقٗاۚ فَلَمَّآ أَفَاقَ قَالَ سُبۡحَٰنَكَ تُبۡتُ إِلَيۡكَ وَأَنَا۠ أَوَّلُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Pamene Mûsa adafika kumalo achipangano Chathucho, ndipo Mbuye wake namulankhula, (Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Dzionetseni kwa ine kuti ndikuoneni.” Allah adati: “Sungathe kundiona; koma yang’ana phirilo (lomwe lili patsogolo pako). Ngati likhazikika pamalo pake (popanda kusweka), ukhoza kundiona.” Choncho Mbuye wake pamene adadzionetsa kwa phirilo, adalichita kukhala loswekasweka ndipo Mussa adagwa ndi kukomoka. Pamene adatsitsimuka adati: “(Ha! Ndikutsimikizadi kuti) Inu ndinu Wolemekezeka. Ndalapa kwa Inu, ndipo ndine woyamba mwa okhulupirira (izi).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ يَٰمُوسَىٰٓ إِنِّي ٱصۡطَفَيۡتُكَ عَلَى ٱلنَّاسِ بِرِسَٰلَٰتِي وَبِكَلَٰمِي فَخُذۡ مَآ ءَاتَيۡتُكَ وَكُن مِّنَ ٱلشَّٰكِرِينَ
(Allah) adati: “E iwe Mûsa! Ndithu Ine ndakusankha iwe mwa anthu onse, (kukusankhira) uthenga Wanga ndi kuyankhulana Nane. Choncho landira chimene ndakupatsa, ndipo khala m’modzi wa anthu othokoza.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَكَتَبۡنَا لَهُۥ فِي ٱلۡأَلۡوَاحِ مِن كُلِّ شَيۡءٖ مَّوۡعِظَةٗ وَتَفۡصِيلٗا لِّكُلِّ شَيۡءٖ فَخُذۡهَا بِقُوَّةٖ وَأۡمُرۡ قَوۡمَكَ يَأۡخُذُواْ بِأَحۡسَنِهَاۚ سَأُوْرِيكُمۡ دَارَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Ndipo tidamlembera m’mapale (m’masileti) maphunziro aulaliki wa mtundu uliwonse wofotokoza chinthu chilichonse: “Choncho, atenge mwa mphamvu ndi kuwalamulira anthu ako kuti awagwire mwa ubwino wake. Posachedwapa ndidzakusonyezani midzi ya oipa oswa malamulo athu (momwe idaonongekera. Ndipo ndikulowetsani inu m’menemo).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
سَأَصۡرِفُ عَنۡ ءَايَٰتِيَ ٱلَّذِينَ يَتَكَبَّرُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ بِغَيۡرِ ٱلۡحَقِّ وَإِن يَرَوۡاْ كُلَّ ءَايَةٖ لَّا يُؤۡمِنُواْ بِهَا وَإِن يَرَوۡاْ سَبِيلَ ٱلرُّشۡدِ لَا يَتَّخِذُوهُ سَبِيلٗا وَإِن يَرَوۡاْ سَبِيلَ ٱلۡغَيِّ يَتَّخِذُوهُ سَبِيلٗاۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَكَانُواْ عَنۡهَا غَٰفِلِينَ
Ndiwatembenuzira kuzilingalira zizindikiro Zanga awo omwe akudzitukumula pa dziko popanda choonadi, ndipo akaona chizindikiro chilichonse sachikhulupirira, ndipo akaona njira yolungama sakuiyesa njira (sakuitsata), koma akaona njira yosokera akuiyetsa njira (akuitsata). Zimenezo nchifukwa chakuti iwo adatsutsa zizindikiro Zathu ndipo anali osazilabadira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَلِقَآءِ ٱلۡأٓخِرَةِ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡۚ هَلۡ يُجۡزَوۡنَ إِلَّا مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo awo amene atsutsa zizindikiro Zathu ndi nkumano wa tsiku lachimaliziro, zochita zawo zaonongeka. Kodi adzalipidwa china kuposa zomwe adali kuchita?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱتَّخَذَ قَوۡمُ مُوسَىٰ مِنۢ بَعۡدِهِۦ مِنۡ حُلِيِّهِمۡ عِجۡلٗا جَسَدٗا لَّهُۥ خُوَارٌۚ أَلَمۡ يَرَوۡاْ أَنَّهُۥ لَا يُكَلِّمُهُمۡ وَلَا يَهۡدِيهِمۡ سَبِيلًاۘ ٱتَّخَذُوهُ وَكَانُواْ ظَٰلِمِينَ
Ndipo pambuyo pake (popita kukalandira Taurat), anthu a Mûsa adaumba (fano la) thole (mwana wa ng’ombe) kuchokera mu zodzikongoletsera zawo (zibangiri zawo za siliva ndi golide); yemwe adali ndi thupi ndi kumatuluka mawu (koma wopanda moyo). Kodi sakuona kuti ilo (fano lawolo) silikuwalankhula ndiponso silikuwaongolera njira (yabwino?) Koma adalipanga basi (kuti likhale mulungu wawo wa fano) potero adali kudzichitira okha zoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَمَّا سُقِطَ فِيٓ أَيۡدِيهِمۡ وَرَأَوۡاْ أَنَّهُمۡ قَدۡ ضَلُّواْ قَالُواْ لَئِن لَّمۡ يَرۡحَمۡنَا رَبُّنَا وَيَغۡفِرۡ لَنَا لَنَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡخَٰسِرِينَ
Pamene adazindikira kulakwa kwawo, (anadandaula kwambiri) naona kuti iwo asokera, anati: “Ngati Mbuye wathu satimvera chisoni ndi kutikhululukira, ndithudi, tikhala mwa otaika (oonongeka).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَمَّا رَجَعَ مُوسَىٰٓ إِلَىٰ قَوۡمِهِۦ غَضۡبَٰنَ أَسِفٗا قَالَ بِئۡسَمَا خَلَفۡتُمُونِي مِنۢ بَعۡدِيٓۖ أَعَجِلۡتُمۡ أَمۡرَ رَبِّكُمۡۖ وَأَلۡقَى ٱلۡأَلۡوَاحَ وَأَخَذَ بِرَأۡسِ أَخِيهِ يَجُرُّهُۥٓ إِلَيۡهِۚ قَالَ ٱبۡنَ أُمَّ إِنَّ ٱلۡقَوۡمَ ٱسۡتَضۡعَفُونِي وَكَادُواْ يَقۡتُلُونَنِي فَلَا تُشۡمِتۡ بِيَ ٱلۡأَعۡدَآءَ وَلَا تَجۡعَلۡنِي مَعَ ٱلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo pamene Mûsa adabwerera kwa anthu ake ali wokwiya, wodandaula (pomva zomwe zidachitikazo), adati: “Umlowam’malo wanu womwe mudandichitira pambuyo panga, ngoipa zedi. Kodi mudalifulumilira lamulo la Mbuye wanu; (mudachita zanuzanu musanadziwe chimene angakulamulireni Mulungu wanu)? Ndipo adawaponya pansi mapalewo (momwe mudalembedwa malamulo a chipembedzo chake). Nagwira mutu wa M’bale wake nkuukokera kwa iye. (kufuna kummenya chifukwa cha mkwiyo umene adali nawo. M’bale wakeyo) adati: “E iwe mwana wa mayi anga! Ndithu anthu (awa) adandiyesa wofooka, potero (sadamvere malangizo anga). Adatsala pang’ono kundipha. Choncho usawakondweretse adani (ndi chilango chako) pa ine, ndipo usandiike pamodzi ndi anthu oipa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قَالَ رَبِّ ٱغۡفِرۡ لِي وَلِأَخِي وَأَدۡخِلۡنَا فِي رَحۡمَتِكَۖ وَأَنتَ أَرۡحَمُ ٱلرَّٰحِمِينَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ndikhululukireni ine ndi m’bale wanga ndipo tilowetseni m’chifundo Chanu. Inu Ndinu Achifundo kuposa achifundo onse.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ٱتَّخَذُواْ ٱلۡعِجۡلَ سَيَنَالُهُمۡ غَضَبٞ مِّن رَّبِّهِمۡ وَذِلَّةٞ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۚ وَكَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُفۡتَرِينَ
Ndithu omwe adapanga (fano la ) Thole uwafika mkwiyo wa Mbuye wawo ndi kunyozeka pa moyo wa dziko lapansi. M’menemo ndi momwe timawalipirira anthu opeka (zinthu za chipembedzo).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ عَمِلُواْ ٱلسَّيِّـَٔاتِ ثُمَّ تَابُواْ مِنۢ بَعۡدِهَا وَءَامَنُوٓاْ إِنَّ رَبَّكَ مِنۢ بَعۡدِهَا لَغَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo omwe adachita zoipa, kenako nkulapa pambuyo pake nakhulupirira ndithu Mbuye wako pambuyo pakulapako, Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَمَّا سَكَتَ عَن مُّوسَى ٱلۡغَضَبُ أَخَذَ ٱلۡأَلۡوَاحَۖ وَفِي نُسۡخَتِهَا هُدٗى وَرَحۡمَةٞ لِّلَّذِينَ هُمۡ لِرَبِّهِمۡ يَرۡهَبُونَ
Pamene mkwiyo wa Mûsa udatotobwa, adatola mapale aja omwe m’malembo mwake mudali chiongoko ndi chifundo kwa omwe amaopa Mbuye wawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱخۡتَارَ مُوسَىٰ قَوۡمَهُۥ سَبۡعِينَ رَجُلٗا لِّمِيقَٰتِنَاۖ فَلَمَّآ أَخَذَتۡهُمُ ٱلرَّجۡفَةُ قَالَ رَبِّ لَوۡ شِئۡتَ أَهۡلَكۡتَهُم مِّن قَبۡلُ وَإِيَّٰيَۖ أَتُهۡلِكُنَا بِمَا فَعَلَ ٱلسُّفَهَآءُ مِنَّآۖ إِنۡ هِيَ إِلَّا فِتۡنَتُكَ تُضِلُّ بِهَا مَن تَشَآءُ وَتَهۡدِي مَن تَشَآءُۖ أَنتَ وَلِيُّنَا فَٱغۡفِرۡ لَنَا وَٱرۡحَمۡنَاۖ وَأَنتَ خَيۡرُ ٱلۡغَٰفِرِينَ
Ndipo Mûsa adasankha anthu ake makumi asanu ndi awiri (70 omwe adali amakhalidwe abwino) kuti akafike kumalo a chipangano chathu (chimene tidamuuza kuti akabwere nawo pa phiripo kuti akapemphe chikhululuko pa machimo awo omwe adachitidwa ndi anzawo oipa). Ndipo pamene chivomerezi chachikulu chidawafika (adatsala pang’ono kufa). (Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ngati mukadafuna mukadawaononga iwo ndi ine kale (pamaso pa anzawo onse kuti adzionere okha kuti amwalira ndi mphamvu za Allah, osati pakuwapha ine). Kodi mutiononga chifukwa cha zochita za mbuli zathu? Izi sichina koma ndi mayesero anu. Kupyolera m’mayeserowo mumamlekelera kusokera amene mwamfuna, ndi kumtsogolera amene mwamfuna. Inu ndiye Mtetezi wathu; choncho, tikhululukireni ndi kutimvera chifundo. Inu ndinu Abwino mwa okhululuka onse.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَٱكۡتُبۡ لَنَا فِي هَٰذِهِ ٱلدُّنۡيَا حَسَنَةٗ وَفِي ٱلۡأٓخِرَةِ إِنَّا هُدۡنَآ إِلَيۡكَۚ قَالَ عَذَابِيٓ أُصِيبُ بِهِۦ مَنۡ أَشَآءُۖ وَرَحۡمَتِي وَسِعَتۡ كُلَّ شَيۡءٖۚ فَسَأَكۡتُبُهَا لِلَّذِينَ يَتَّقُونَ وَيُؤۡتُونَ ٱلزَّكَوٰةَ وَٱلَّذِينَ هُم بِـَٔايَٰتِنَا يُؤۡمِنُونَ
“Ndipo tilembereni zabwino pa dziko lino lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro, ndithudi tibwerera kwa inu!” (Allah) adati: “Chilango changa ndichifikitsa kwa yemwe ndamfuna (mwa anthu oipa); ndipo chifundo Changa chakwanira pa chilichonse (pa abwino ndi oipa). Choncho ndiwalembera (kuti mtendere umenewu udzakhale wawowawo pa tsiku lachimaliziro) amene akupewa (zoletsedwa) ndi kumapereka Zakaat, ndi kumakhulupirira zizindikiro Zathu;”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِينَ يَتَّبِعُونَ ٱلرَّسُولَ ٱلنَّبِيَّ ٱلۡأُمِّيَّ ٱلَّذِي يَجِدُونَهُۥ مَكۡتُوبًا عِندَهُمۡ فِي ٱلتَّوۡرَىٰةِ وَٱلۡإِنجِيلِ يَأۡمُرُهُم بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَنۡهَىٰهُمۡ عَنِ ٱلۡمُنكَرِ وَيُحِلُّ لَهُمُ ٱلطَّيِّبَٰتِ وَيُحَرِّمُ عَلَيۡهِمُ ٱلۡخَبَٰٓئِثَ وَيَضَعُ عَنۡهُمۡ إِصۡرَهُمۡ وَٱلۡأَغۡلَٰلَ ٱلَّتِي كَانَتۡ عَلَيۡهِمۡۚ فَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ بِهِۦ وَعَزَّرُوهُ وَنَصَرُوهُ وَٱتَّبَعُواْ ٱلنُّورَ ٱلَّذِيٓ أُنزِلَ مَعَهُۥٓ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
“Omwe akutsata Mtumiki, mneneri wosatha kuwerenga ndi kulemba (ngakhale ali choncho, akuphunzitsa zophunzitsa zodabwitsa); yemwe akumpeza atalembedwa kwa iwo m’buku la Taurat ndi Injili. Akuwalamula zabwino ndi kuwaletsa zoipa, ndi kuwaloleza zabwino ndi kuwaletsa zodetsedwa (zoipa); ndi kuwatula mitolo yawo ndi magoli omwe adali pa iwo (malamulo ovuta kuwatsata). Choncho, amene amkhulupirira (Muhammad {s.a.w}) ndi kumamlemekeza ndi kumuthangata, natsata kuunika (Quran) komwe kudavumbulutsidwa pamodzi ndi iye, iwo ndiwo opambana.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ إِنِّي رَسُولُ ٱللَّهِ إِلَيۡكُمۡ جَمِيعًا ٱلَّذِي لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُۖ فَـَٔامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِ ٱلنَّبِيِّ ٱلۡأُمِّيِّ ٱلَّذِي يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَكَلِمَٰتِهِۦ وَٱتَّبِعُوهُ لَعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Nena: “E inu anthu! Ndithu ine ndine Mtumiki wa Allah kwa inu nonse. (Allah) Yemwe ali nawo ufumu wa kumwamba ndi pansi. Palibe wopembedzedwa mwa choonadi koma Iye. Amapatsa moyo ndi imfa. Choncho, khulupirirani mwa Allah ndi Mtumiki Wake yemwe ndi Mneneri wosadziwa kulemba ndi kuwerenga, yemwe akukhulupirira Allah ndi mawu Ake. Ndipo mtsatireni kuti muongoke.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمِن قَوۡمِ مُوسَىٰٓ أُمَّةٞ يَهۡدُونَ بِٱلۡحَقِّ وَبِهِۦ يَعۡدِلُونَ
Ndipo mwa anthu a Mûsa, mudali gulu lomwe linkatsogolera anzawo ku choonadi. Ndipo ndi choonadicho ankachita chilungamo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَطَّعۡنَٰهُمُ ٱثۡنَتَيۡ عَشۡرَةَ أَسۡبَاطًا أُمَمٗاۚ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ إِذِ ٱسۡتَسۡقَىٰهُ قَوۡمُهُۥٓ أَنِ ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡحَجَرَۖ فَٱنۢبَجَسَتۡ مِنۡهُ ٱثۡنَتَا عَشۡرَةَ عَيۡنٗاۖ قَدۡ عَلِمَ كُلُّ أُنَاسٖ مَّشۡرَبَهُمۡۚ وَظَلَّلۡنَا عَلَيۡهِمُ ٱلۡغَمَٰمَ وَأَنزَلۡنَا عَلَيۡهِمُ ٱلۡمَنَّ وَٱلسَّلۡوَىٰۖ كُلُواْ مِن طَيِّبَٰتِ مَا رَزَقۡنَٰكُمۡۚ وَمَا ظَلَمُونَا وَلَٰكِن كَانُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ يَظۡلِمُونَ
Ndipo tidawagawa iwo m’mafuko khumi ndi awiri (osiyanasiyana) monga mitundu ikuluikulu. Ndipo tidamuvumbulutsira Mûsa pamene anthu ake adampempha madzi, kuti: “Menya mwala ndi ndodo yakoyo.” Ndipo mudatuluka akasupe khumi ndi awiri mwakuti fuko lililonse lidadziwa malo ake omwera. Ndipo tidawaphimba ndi mthunzi wa mtambo, ndi kuwatumizira mana ndi salwa (mbalame). (Tidawauza): “Idyani zinthu zabwinozi zomwe takupatsani.” Komatu sadatichitire choipa (pamene adachita zamphulupulu), koma adadzichitira okha zoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذۡ قِيلَ لَهُمُ ٱسۡكُنُواْ هَٰذِهِ ٱلۡقَرۡيَةَ وَكُلُواْ مِنۡهَا حَيۡثُ شِئۡتُمۡ وَقُولُواْ حِطَّةٞ وَٱدۡخُلُواْ ٱلۡبَابَ سُجَّدٗا نَّغۡفِرۡ لَكُمۡ خَطِيٓـَٰٔتِكُمۡۚ سَنَزِيدُ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo pamene adauzidwa: “Khalani mu Mzinda uwu (Yerusalemu), ndipo idyani m’menemo paliponse pamene mwafuna, ndipo nenani (polowa mu mzindamo uku mutawerama): “Tifafanizireni machimo athu, (E Inu Mbuye wathu)!” Ndipo lowerani pa chipata (chake) modzichepetsa; tikukhululukirani zolakwa zanu ndipo tiwaonjezera zabwino ochita zabwino.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَبَدَّلَ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ مِنۡهُمۡ قَوۡلًا غَيۡرَ ٱلَّذِي قِيلَ لَهُمۡ فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ رِجۡزٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ بِمَا كَانُواْ يَظۡلِمُونَ
Koma aja amene adadzichitira okha zoipa, mwa iwo adasintha mawu ena kusiya omwe adauzidwa; choncho, tidawatumizira chilango chochokera kumwamba chifukwa chodzichitira okha zoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَسۡـَٔلۡهُمۡ عَنِ ٱلۡقَرۡيَةِ ٱلَّتِي كَانَتۡ حَاضِرَةَ ٱلۡبَحۡرِ إِذۡ يَعۡدُونَ فِي ٱلسَّبۡتِ إِذۡ تَأۡتِيهِمۡ حِيتَانُهُمۡ يَوۡمَ سَبۡتِهِمۡ شُرَّعٗا وَيَوۡمَ لَا يَسۡبِتُونَ لَا تَأۡتِيهِمۡۚ كَذَٰلِكَ نَبۡلُوهُم بِمَا كَانُواْ يَفۡسُقُونَ
Tawafunsani nkhani ya mudzi umene udali m’mphepete mwa nyanja; (anthu am’mudziwo) pamene adali kuswa (lamulo la) tsiku la Sabata (lomwe adauzidwa kuti pa tsikuli asamachite usodzi wa nsomba, koma m’malo mwake azichita mapemphero okha). Nsomba zawo zinkawadzera yandayanda patsiku la Sabata, koma patsiku lomwe silidali la Sabata sizidali kuwabwerera (yandayanda). Motero tidawayesa mayeso chifukwa chakuchimwa kwawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذۡ قَالَتۡ أُمَّةٞ مِّنۡهُمۡ لِمَ تَعِظُونَ قَوۡمًا ٱللَّهُ مُهۡلِكُهُمۡ أَوۡ مُعَذِّبُهُمۡ عَذَابٗا شَدِيدٗاۖ قَالُواْ مَعۡذِرَةً إِلَىٰ رَبِّكُمۡ وَلَعَلَّهُمۡ يَتَّقُونَ
Ndipo (akumbutse ) pamene gulu lina mwa iwo linkanena (kwa omwe amachenjeza amene adaswa kupatulika kwa tsiku la Sabata pamene adati): “Pali phindu lanji kuwachenjeza anthu omwe Allah awawononga kapena kuwalanga ndi chilango chaukali pompano pa dziko lapansi)? (Iwo) adati: “Kuti tidzakhale ndi chidandaulo kwa Mbuye wathu (ponena kuti tidawachenjeza koma sadatimvere) ndi kutinso mwina angaope (Allah nasiya kuswa lamulo Lake).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَمَّا نَسُواْ مَا ذُكِّرُواْ بِهِۦٓ أَنجَيۡنَا ٱلَّذِينَ يَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلسُّوٓءِ وَأَخَذۡنَا ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ بِعَذَابِۭ بَـِٔيسِۭ بِمَا كَانُواْ يَفۡسُقُونَ
Choncho, pamene sanalabadire zimene anauzidwa ndi kuchenjezedwa, tinawapulumutsa (anthu) omwe amaletsa zoipa, ndipo tidawakhaulitsa amene ankadzichitira okha zoipa ndi chilango choipa kwambiri chifukwa chakupandukila (kwawo) malamulo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَمَّا عَتَوۡاْ عَن مَّا نُهُواْ عَنۡهُ قُلۡنَا لَهُمۡ كُونُواْ قِرَدَةً خَٰسِـِٔينَ
Pamene anadzikweza pakusasiya zimene analetsedwazo tidawauza: “Khalani anyani, oyaluka (paliponse).”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذۡ تَأَذَّنَ رَبُّكَ لَيَبۡعَثَنَّ عَلَيۡهِمۡ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ مَن يَسُومُهُمۡ سُوٓءَ ٱلۡعَذَابِۗ إِنَّ رَبَّكَ لَسَرِيعُ ٱلۡعِقَابِ وَإِنَّهُۥ لَغَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo (akumbutse) pamene Mbuye wako analengeza (kuti) ndithu adzawatumizira iwo (Ayuda) anthu mpaka tsiku la Qiyâma, omwe adzawazunza ndi mazunzo oipa. Ndithu Mbuye wako ngofulumira kulanga, ndipo ndithu palibe chikaiko, Iye Ngokhululuka kwambiri, Ngwachifundo chambiri.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَقَطَّعۡنَٰهُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ أُمَمٗاۖ مِّنۡهُمُ ٱلصَّٰلِحُونَ وَمِنۡهُمۡ دُونَ ذَٰلِكَۖ وَبَلَوۡنَٰهُم بِٱلۡحَسَنَٰتِ وَٱلسَّيِّـَٔاتِ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo tidawalekanitsa pakati pawo (Ayuda), ndi kuwabalalitsa pa dziko lonse kukhala mafuko osiyanasiyana. Ena mwa iwo abwino (olungama) ndipo ena sali choncho (oipa). Tinawayesa mayeso a zabwino ndi zoipa kuti abwelere (koma ayi, sanabwelere).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَخَلَفَ مِنۢ بَعۡدِهِمۡ خَلۡفٞ وَرِثُواْ ٱلۡكِتَٰبَ يَأۡخُذُونَ عَرَضَ هَٰذَا ٱلۡأَدۡنَىٰ وَيَقُولُونَ سَيُغۡفَرُ لَنَا وَإِن يَأۡتِهِمۡ عَرَضٞ مِّثۡلُهُۥ يَأۡخُذُوهُۚ أَلَمۡ يُؤۡخَذۡ عَلَيۡهِم مِّيثَٰقُ ٱلۡكِتَٰبِ أَن لَّا يَقُولُواْ عَلَى ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡحَقَّ وَدَرَسُواْ مَا فِيهِۗ وَٱلدَّارُ ٱلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لِّلَّذِينَ يَتَّقُونَۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Choncho, anawatsatira pambuyo (anthu abwinowo), otsatira atsopano omwe analandira buku (la Allah nalowa mmalo mwa iwo koma popanda kulitsata ndi kulilingalira). Ankatenga zinthu zoletsedwa za pa dziko lapansi uku akunena: “Tidzakhululukidwa, (Allah adzatikhululukira).” Ngati zina zonga izo zitawapeza, amazitenganso. Kodi silidatengedwe pangano kwa iwo la m’buku kuti sadzamunenera Allah bodza koma zoona zokhazokha? (Nanga akuneneranji kuti Allah adzawakhululukira pomwe akupitiriza machimo)? Pomwe iwo aphunzira zomwe zili mmenemo. Komatu nyumba ya chimaliziro idzawakhalira bwino amene akuopa (Allah). Nanga bwanji simukuzindikira?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ يُمَسِّكُونَ بِٱلۡكِتَٰبِ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ إِنَّا لَا نُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُصۡلِحِينَ
Ndipo amene akugwirisitsa buku (la Allah potsata zophunzitsa zake) ndi kumapemphera Swala, (tidzawalipira zabwino). Ndithu Ife sitipititsa pachabe malipiro a ochita zabwino.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ وَإِذۡ نَتَقۡنَا ٱلۡجَبَلَ فَوۡقَهُمۡ كَأَنَّهُۥ ظُلَّةٞ وَظَنُّوٓاْ أَنَّهُۥ وَاقِعُۢ بِهِمۡ خُذُواْ مَآ ءَاتَيۡنَٰكُم بِقُوَّةٖ وَٱذۡكُرُواْ مَا فِيهِ لَعَلَّكُمۡ تَتَّقُونَ
Ndipo(akumbutse) pamene tidalizula phiri ndikulinyamula pamwamba pawo monga denga (kapena mtambo umene wawavindikira) natsimikiza kuti liwagwera, (tidawauza): “Landirani, mwamphamvu malamulo amene takupatsani, ndipo kumbukirani zomwe zili m’menemo (pozitsata ndi kuzichita); kuti inu muope.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذۡ أَخَذَ رَبُّكَ مِنۢ بَنِيٓ ءَادَمَ مِن ظُهُورِهِمۡ ذُرِّيَّتَهُمۡ وَأَشۡهَدَهُمۡ عَلَىٰٓ أَنفُسِهِمۡ أَلَسۡتُ بِرَبِّكُمۡۖ قَالُواْ بَلَىٰ شَهِدۡنَآۚ أَن تَقُولُواْ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ إِنَّا كُنَّا عَنۡ هَٰذَا غَٰفِلِينَ
Ndipo (kumbukirani) pamene Mbuye wako adawatulutsa ana a Adam m’misana ya atate awo ndi kuwachititsa umboni okha (powauza kuti): “Kodi Ine sindine Mbuye wanu?” Iwo adati: “Inde tikuikira umboni (kuti Inuyo ndiye Mbuye wathu).” (Allah adawauza kuti): “Kuopera kuti mungadzanene tsiku louka kwa akufa: “Ife sitidali kuzindikira chipanganochi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوۡ تَقُولُوٓاْ إِنَّمَآ أَشۡرَكَ ءَابَآؤُنَا مِن قَبۡلُ وَكُنَّا ذُرِّيَّةٗ مِّنۢ بَعۡدِهِمۡۖ أَفَتُهۡلِكُنَا بِمَا فَعَلَ ٱلۡمُبۡطِلُونَ
Kapena mungadzati: “Makolo athu ndi amene adapembedza mafano kale, ndipo ife tidali ana odza pambuyo pawo (choncho tidawatsatira pazimene ankachita). Kodi nanga mutiononga chifukwa cha zomwe adachita oipa?”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَكَذَٰلِكَ نُفَصِّلُ ٱلۡأٓيَٰتِ وَلَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
M’menemo ndi momwe tikulongosolera mokwanira zivumbulutso kuti mwina iwo angabwelere (kwa Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ ٱلَّذِيٓ ءَاتَيۡنَٰهُ ءَايَٰتِنَا فَٱنسَلَخَ مِنۡهَا فَأَتۡبَعَهُ ٱلشَّيۡطَٰنُ فَكَانَ مِنَ ٱلۡغَاوِينَ
Ndipo alakatulire nkhani za yemwe tidampatsa zizindikiro zathu nadzichotsa m’menemo (m’zizindikiromo), ndipo satana anamtsata, choncho adali m’gulu la osokera.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَوۡ شِئۡنَا لَرَفَعۡنَٰهُ بِهَا وَلَٰكِنَّهُۥٓ أَخۡلَدَ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ وَٱتَّبَعَ هَوَىٰهُۚ فَمَثَلُهُۥ كَمَثَلِ ٱلۡكَلۡبِ إِن تَحۡمِلۡ عَلَيۡهِ يَلۡهَثۡ أَوۡ تَتۡرُكۡهُ يَلۡهَثۚ ذَّٰلِكَ مَثَلُ ٱلۡقَوۡمِ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَاۚ فَٱقۡصُصِ ٱلۡقَصَصَ لَعَلَّهُمۡ يَتَفَكَّرُونَ
Ndipo tikadafuna tikadamtukula nazo (ulemelero wake). Koma iye adapendekera ku za mdziko natsatira zilakolako zake. Fanizo lake lili ngati galu. Ngati utamkalipira amathawa uku akutulutsa lirime lake kunja. Ngakhale utamsiya amatulutsabe kunja lirime lake. Umo ndi momwe liliri fanizo la anthu otsutsa zizindikiro Zathu. Choncho asimbire nkhani izi kuti angalingalire.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
سَآءَ مَثَلًا ٱلۡقَوۡمُ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَأَنفُسَهُمۡ كَانُواْ يَظۡلِمُونَ
Taonani kuipa fanizo la anthu omwe atsutsa zizindikiro Zathu ndi kudzichitira okha zoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
مَن يَهۡدِ ٱللَّهُ فَهُوَ ٱلۡمُهۡتَدِيۖ وَمَن يُضۡلِلۡ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
Amene Allah wamuongola ndiye woongoka. Ndipo amene wamulekelera kusokera (chifukwa chakusatsatira kwake malangizo a Allah), iwo ndiwo otaika (oonongeka).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَقَدۡ ذَرَأۡنَا لِجَهَنَّمَ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلۡجِنِّ وَٱلۡإِنسِۖ لَهُمۡ قُلُوبٞ لَّا يَفۡقَهُونَ بِهَا وَلَهُمۡ أَعۡيُنٞ لَّا يُبۡصِرُونَ بِهَا وَلَهُمۡ ءَاذَانٞ لَّا يَسۡمَعُونَ بِهَآۚ أُوْلَٰٓئِكَ كَٱلۡأَنۡعَٰمِ بَلۡ هُمۡ أَضَلُّۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡغَٰفِلُونَ
Ndithudi, ziwanda zambiri ndi anthu tidawalengera kukalowa ku (Moto wa) Jahannam. Mitima ali nayo koma sazindikira nayo kanthu; ndipo maso ali nawo koma sapenyera nawo (zodabwitsa za Allah); ndipo makutu ali nawo koma samvera nawo (zowapindulitsa). Iwo ali ngati ziweto, kapena iwo ndi osokera zedi kuposa Ziweto. Iwo ndi osalabadira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلِلَّهِ ٱلۡأَسۡمَآءُ ٱلۡحُسۡنَىٰ فَٱدۡعُوهُ بِهَاۖ وَذَرُواْ ٱلَّذِينَ يُلۡحِدُونَ فِيٓ أَسۡمَٰٓئِهِۦۚ سَيُجۡزَوۡنَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo Allah ali nawo maina abwino. Choncho, muitaneni ndi mainawo. Alekeni amene akupotoza maina Ake posachedwapa alipidwa zomwe akhala akuchita.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمِمَّنۡ خَلَقۡنَآ أُمَّةٞ يَهۡدُونَ بِٱلۡحَقِّ وَبِهِۦ يَعۡدِلُونَ
Ndipo mwa amene tidawalenga, alipo anthu oongolera (anzawo) ku choonadi. Ndipo kupyolera mchoonadicho akuchita chilungamo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا سَنَسۡتَدۡرِجُهُم مِّنۡ حَيۡثُ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo amene atsutsa zivumbulutso zathu, tiwalekelera pang’onopang’ono, kenako nkuwakhaulitsa kuchokera momwe iwo sakudziwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأُمۡلِي لَهُمۡۚ إِنَّ كَيۡدِي مَتِينٌ
Ndipo ndiwapatsa kanthawi. Ndithu kukhaulitsa kwanga nkokhwima.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَلَمۡ يَتَفَكَّرُواْۗ مَا بِصَاحِبِهِم مِّن جِنَّةٍۚ إِنۡ هُوَ إِلَّا نَذِيرٞ مُّبِينٌ
Kodi sadalingalire kuti munthu wawoyo (mneneri Muhammad {s.a.w}) alibe misala? Iye sali koma mchenjezi woonekera poyera.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَوَلَمۡ يَنظُرُواْ فِي مَلَكُوتِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا خَلَقَ ٱللَّهُ مِن شَيۡءٖ وَأَنۡ عَسَىٰٓ أَن يَكُونَ قَدِ ٱقۡتَرَبَ أَجَلُهُمۡۖ فَبِأَيِّ حَدِيثِۭ بَعۡدَهُۥ يُؤۡمِنُونَ
Kodi saona ufumu wa kumwamba ndi pansi, ndi zinthu zomwe Allah adalenga? Mwina mwake nthawi yawo yofera yayandikira. (Nanga adzalingalira liti zolengedwa za Allah)? Kodi ndi nkhani iti pambuyo pa iyi (Qur’an) imene adzaikhulupirira?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
مَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَلَا هَادِيَ لَهُۥۚ وَيَذَرُهُمۡ فِي طُغۡيَٰنِهِمۡ يَعۡمَهُونَ
Amene Allah wamulekelera kusokera, alibe muongoli. Ndipo Allah akuwasiya akuyumbayumba m’kusokera kwawo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلسَّاعَةِ أَيَّانَ مُرۡسَىٰهَاۖ قُلۡ إِنَّمَا عِلۡمُهَا عِندَ رَبِّيۖ لَا يُجَلِّيهَا لِوَقۡتِهَآ إِلَّا هُوَۚ ثَقُلَتۡ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ لَا تَأۡتِيكُمۡ إِلَّا بَغۡتَةٗۗ يَسۡـَٔلُونَكَ كَأَنَّكَ حَفِيٌّ عَنۡهَاۖ قُلۡ إِنَّمَا عِلۡمُهَا عِندَ ٱللَّهِ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Akukufunsa za nthawi (ya Qiyâma) kuti idzakhalako liti? Nena: “Kudziwika kwa nthawi yake kuli kwa Mbuye wanga. palibe amene angaionetse poyera nthawi yake koma Iye. Nkovuta kwambiri kumwamba ndi pansi (kuizindikira nthawi yake). Siidzakudzerani koma mwadzidzidzi.” Akukufunsa ngati kuti iwe ukudziwa bwino za nthawiyo. Nena: “Kudziwika kwa nthawi yake kuli kwa Allah. Koma anthu ambiri sadziwa.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
قُل لَّآ أَمۡلِكُ لِنَفۡسِي نَفۡعٗا وَلَا ضَرًّا إِلَّا مَا شَآءَ ٱللَّهُۚ وَلَوۡ كُنتُ أَعۡلَمُ ٱلۡغَيۡبَ لَٱسۡتَكۡثَرۡتُ مِنَ ٱلۡخَيۡرِ وَمَا مَسَّنِيَ ٱلسُّوٓءُۚ إِنۡ أَنَا۠ إِلَّا نَذِيرٞ وَبَشِيرٞ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ
Nena: “Ine ndekha ndilibe mphamvu yodzibweretsera chabwino kapena kudzichotsera choipa, koma chimene Allah wafuna. Ndikadakhala kuti ndikudziwa za mseri, ndikadadzichulukitsira zabwino, ndipo choipa sichikadandikhudza. Ine sindili chilichonse koma mchenjezi ndi wouza anthu okhulupirira nkhani zabwino.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
۞ هُوَ ٱلَّذِي خَلَقَكُم مِّن نَّفۡسٖ وَٰحِدَةٖ وَجَعَلَ مِنۡهَا زَوۡجَهَا لِيَسۡكُنَ إِلَيۡهَاۖ فَلَمَّا تَغَشَّىٰهَا حَمَلَتۡ حَمۡلًا خَفِيفٗا فَمَرَّتۡ بِهِۦۖ فَلَمَّآ أَثۡقَلَت دَّعَوَا ٱللَّهَ رَبَّهُمَا لَئِنۡ ءَاتَيۡتَنَا صَٰلِحٗا لَّنَكُونَنَّ مِنَ ٱلشَّٰكِرِينَ
Iye ndi Yemwe adakulengani kuchokera mwa munthu mmodzi, napanga mwa iye mkazi wake kuti adzikhala naye. Pamene adamkumbatira, adakhala ndi pakati popepuka nayenda napo (mosalemedwa). Koma pamene (pakatipo) padalemera (patangotsala pang’ono kuti abereke) anampempha Allah, Mbuye wawo (kuti): “Ngati mutipatsa mwana wabwino, ndithu tidzakhala mwa othokoza kwambiri.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلَمَّآ ءَاتَىٰهُمَا صَٰلِحٗا جَعَلَا لَهُۥ شُرَكَآءَ فِيمَآ ءَاتَىٰهُمَاۚ فَتَعَٰلَى ٱللَّهُ عَمَّا يُشۡرِكُونَ
Choncho, pamene adawapatsa mwana wabwino (yemwe adapempha) adamchitira Allah anzake (mafano) pa chimene adawapatsacho. Koma Allah watukuka kuzimene akumphatikiza nazozo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَيُشۡرِكُونَ مَا لَا يَخۡلُقُ شَيۡـٔٗا وَهُمۡ يُخۡلَقُونَ
Kodi akumphatikiza (Allah) ndi zinthu zomwe sizilenga chilichonse pomwe izo zikulengedwa?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَا يَسۡتَطِيعُونَ لَهُمۡ نَصۡرٗا وَلَآ أَنفُسَهُمۡ يَنصُرُونَ
Ndipo sizingathe kuwathandiza ngakhale kudzithandiza zokha (podzibweretsera zabwino ndi kudzichotsera zoipa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِن تَدۡعُوهُمۡ إِلَى ٱلۡهُدَىٰ لَا يَتَّبِعُوكُمۡۚ سَوَآءٌ عَلَيۡكُمۡ أَدَعَوۡتُمُوهُمۡ أَمۡ أَنتُمۡ صَٰمِتُونَ
Ngati (milungu yamafanoyo) mutaiitanira ku chiongoko, siingakutsatireni (chifukwa chakuti siimva kapena kuzindikira chilichonse). Nchimodzimodzi kwa inu kuiitana kapena kukhala chete (palibe chimene ingadziwe).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ ٱلَّذِينَ تَدۡعُونَ مِن دُونِ ٱللَّهِ عِبَادٌ أَمۡثَالُكُمۡۖ فَٱدۡعُوهُمۡ فَلۡيَسۡتَجِيبُواْ لَكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Ndithu amene mukuwapembedza kusiya Allah, ndi akapolo monga inu. (Koma inu muposa iwo). Choncho aitaneni ndipo akuyankheni ngati inu mulidi owona (pa zimene mukunenazi).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
أَلَهُمۡ أَرۡجُلٞ يَمۡشُونَ بِهَآۖ أَمۡ لَهُمۡ أَيۡدٖ يَبۡطِشُونَ بِهَآۖ أَمۡ لَهُمۡ أَعۡيُنٞ يُبۡصِرُونَ بِهَآۖ أَمۡ لَهُمۡ ءَاذَانٞ يَسۡمَعُونَ بِهَاۗ قُلِ ٱدۡعُواْ شُرَكَآءَكُمۡ ثُمَّ كِيدُونِ فَلَا تُنظِرُونِ
Kodi iwo ali nayo miyendo yoyendera? Kapena ali nawo manja ogwilira. Kapena ali nawo maso openyera? Kapena ali nawo makutu omvelera? Nena: “Aitaneni aphatikizi anuwo, ndipo kenako ndichitireni chiwembu ndipo musandipatse nthawi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ وَلِـِّۧيَ ٱللَّهُ ٱلَّذِي نَزَّلَ ٱلۡكِتَٰبَۖ وَهُوَ يَتَوَلَّى ٱلصَّٰلِحِينَ
“Ndithu Mtetezi wanga ndi Allah, Yemwe wavumbulutsa buku (ili lopatulika). Ndipo Iye amawateteza ochita zabwino.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلَّذِينَ تَدۡعُونَ مِن دُونِهِۦ لَا يَسۡتَطِيعُونَ نَصۡرَكُمۡ وَلَآ أَنفُسَهُمۡ يَنصُرُونَ
“Ndipo omwe mukuwapembedza kusiya Iye (Allah,) sangathe kukupulumutsani ndiponso sangathe kudzipulumutsa okha.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِن تَدۡعُوهُمۡ إِلَى ٱلۡهُدَىٰ لَا يَسۡمَعُواْۖ وَتَرَىٰهُمۡ يَنظُرُونَ إِلَيۡكَ وَهُمۡ لَا يُبۡصِرُونَ
Ngati mutawaitanira ku chiwongoko, sangamve; koma uwaona akukuyang’ana koma pomwe iwo sakuona.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
خُذِ ٱلۡعَفۡوَ وَأۡمُرۡ بِٱلۡعُرۡفِ وَأَعۡرِضۡ عَنِ ٱلۡجَٰهِلِينَ
Khala ndi khalidwe lokhululuka, lamula zabwino ndipo dzipatule ku mbuli.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِمَّا يَنزَغَنَّكَ مِنَ ٱلشَّيۡطَٰنِ نَزۡغٞ فَٱسۡتَعِذۡ بِٱللَّهِۚ إِنَّهُۥ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
Ndipo ngati manong’onong’o a satana atakuvutitsa, dzitchinjirize ndi Allah. Ndithu Iye Ngwakumva, Ngodziwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْ إِذَا مَسَّهُمۡ طَٰٓئِفٞ مِّنَ ٱلشَّيۡطَٰنِ تَذَكَّرُواْ فَإِذَا هُم مُّبۡصِرُونَ
Ndithu amene akuopa (Allah), udyerekezi wa satana ukawakhudza amakumbukira (Allah), nkuona (njira yotulukira muudyerekezi wakewo).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِخۡوَٰنُهُمۡ يَمُدُّونَهُمۡ فِي ٱلۡغَيِّ ثُمَّ لَا يُقۡصِرُونَ
Koma anzawo (omwe ali oipa) amawalimbikitsa m’machimo, ndipo kenako saleka (kupitiriza machimowo).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذَا لَمۡ تَأۡتِهِم بِـَٔايَةٖ قَالُواْ لَوۡلَا ٱجۡتَبَيۡتَهَاۚ قُلۡ إِنَّمَآ أَتَّبِعُ مَا يُوحَىٰٓ إِلَيَّ مِن رَّبِّيۚ هَٰذَا بَصَآئِرُ مِن رَّبِّكُمۡ وَهُدٗى وَرَحۡمَةٞ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ
Ngati siudawabweretsere chozizwitsa, akunena: “Bwanji wosachibweretsa pa iwe wekha? Nena: “Ndithudi ndikutsatira zimene zikuvumbulitsidwa kwa ine kuchokera kwa Mbuye wanga. (Sindichita chinthu mwa ine ndekha). Iyi (Qur’an) ndi umboni (waukulu pa zoyankhula zanga) kuchokera kwa Mbuye wanu. (Izo) ndi chiongoko ndi chifundo kwa anthu okhulupirira.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِذَا قُرِئَ ٱلۡقُرۡءَانُ فَٱسۡتَمِعُواْ لَهُۥ وَأَنصِتُواْ لَعَلَّكُمۡ تُرۡحَمُونَ
Ndipo Qur’an ikamawerengedwa, mvetserani (mwatcheru) ndi kukhala chete, kuti muchitiridwe chifundo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱذۡكُر رَّبَّكَ فِي نَفۡسِكَ تَضَرُّعٗا وَخِيفَةٗ وَدُونَ ٱلۡجَهۡرِ مِنَ ٱلۡقَوۡلِ بِٱلۡغُدُوِّ وَٱلۡأٓصَالِ وَلَا تَكُن مِّنَ ٱلۡغَٰفِلِينَ
Ndipo mtchule Mbuye wako mu mtima mwako modzichepetsa, mwa mantha ndi mosakweza mawu m’mawa ndi madzulo; ndipo usakhale mwa osalabadila (malamulo a Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ ٱلَّذِينَ عِندَ رَبِّكَ لَا يَسۡتَكۡبِرُونَ عَنۡ عِبَادَتِهِۦ وَيُسَبِّحُونَهُۥ وَلَهُۥ يَسۡجُدُونَۤ۩
Ndithu amene ali kwa Mbuye wako, (angelo), sadzitukumula posiya kumpembedza (Mbuye wawo, koma iwo) amam’lemekeza ndi kumlambira.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی الأعراف
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن