Check out the new design

Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: An-Nachl   Aja (Korano eilutė):
وَٱللَّهُ أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَحۡيَا بِهِ ٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ مَوۡتِهَآۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّقَوۡمٖ يَسۡمَعُونَ
Ndipo Allah watsitsa madzi kuchokera ku mitambo, ndipo akuipatsa moyo nthaka ndi madziwo (pomeretsa mbewu) pambuyo poti nthakayo idali yakufa; ndithu m’zimenezo muli chisonyezo (chosonyeza kukhoza kwa Allah) kwa anthu amene amamva.
Tafsyrai arabų kalba:
وَإِنَّ لَكُمۡ فِي ٱلۡأَنۡعَٰمِ لَعِبۡرَةٗۖ نُّسۡقِيكُم مِّمَّا فِي بُطُونِهِۦ مِنۢ بَيۡنِ فَرۡثٖ وَدَمٖ لَّبَنًا خَالِصٗا سَآئِغٗا لِّلشَّٰرِبِينَ
Palibe chikaiko, m’ziweto muli phunziro ndi lingaliro kwa inu. Timakumwetsani zomwe zili m’mimba mwa izo, (zomwe zimatuluka) pakati pa ndowe ndi magazi, (omwe ndi) mkaka woyera, wabwino wokoma kwa oumwa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَمِن ثَمَرَٰتِ ٱلنَّخِيلِ وَٱلۡأَعۡنَٰبِ تَتَّخِذُونَ مِنۡهُ سَكَرٗا وَرِزۡقًا حَسَنًاۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّقَوۡمٖ يَعۡقِلُونَ
Ndipo kuchokera ku zipatso za tende ndi mphesa, mumakonza zakumwa zoledzeretsa (zomwe nzoletsedwa) ndikupezanso rizq labwino (m’zipatsozo); ndithudi m’zimenezo muli lingaliro kwa anthu oganiza mwanzeru.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَوۡحَىٰ رَبُّكَ إِلَى ٱلنَّحۡلِ أَنِ ٱتَّخِذِي مِنَ ٱلۡجِبَالِ بُيُوتٗا وَمِنَ ٱلشَّجَرِ وَمِمَّا يَعۡرِشُونَ
Ndipo Mbuye wako adaizindikiritsa njuchi kuti: “Dzikonzere nyumba m’mapiri, m’mitengo, ndi (m’ming’oma) imene (anthu) amakonza.”
Tafsyrai arabų kalba:
ثُمَّ كُلِي مِن كُلِّ ٱلثَّمَرَٰتِ فَٱسۡلُكِي سُبُلَ رَبِّكِ ذُلُلٗاۚ يَخۡرُجُ مِنۢ بُطُونِهَا شَرَابٞ مُّخۡتَلِفٌ أَلۡوَٰنُهُۥ فِيهِ شِفَآءٞ لِّلنَّاسِۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّقَوۡمٖ يَتَفَكَّرُونَ
“Tsono idya zipatso zamtundu uliwonse ndikuyenda m’njira za Mbuye wako zimene wazifewetsa (kuziyenda).” Chimatuluka m’mimba mwake chakumwa cha utoto wosiyanasiyana (uchi), mwa icho muli kuchilitsa kwa anthu (kumatenda ochuluka), ndithu m’zimenezo muli zizindikiro kwa anthu oganiza (zinthu) mwakuya.
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱللَّهُ خَلَقَكُمۡ ثُمَّ يَتَوَفَّىٰكُمۡۚ وَمِنكُم مَّن يُرَدُّ إِلَىٰٓ أَرۡذَلِ ٱلۡعُمُرِ لِكَيۡ لَا يَعۡلَمَ بَعۡدَ عِلۡمٖ شَيۡـًٔاۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلِيمٞ قَدِيرٞ
Ndipo Allah adakulengani, kenako akukupatsani imfa (nthawi ya moyo wanu ikatha); ndipo mwa inu alipo ena amene akubwezedwa ku moyo wonyozeka (waukalamba wogwa nkumina) kotero kuti asadziwe kanthu pambuyo pakudziwa (zambiri); ndithudi Allah Ngodziwa kwambiri Wokhoza (chilichonse chimene wafuna kuti chichitike).
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱللَّهُ فَضَّلَ بَعۡضَكُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ فِي ٱلرِّزۡقِۚ فَمَا ٱلَّذِينَ فُضِّلُواْ بِرَآدِّي رِزۡقِهِمۡ عَلَىٰ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ فَهُمۡ فِيهِ سَوَآءٌۚ أَفَبِنِعۡمَةِ ٱللَّهِ يَجۡحَدُونَ
Ndipo Allah wapereka zopereka Zake mochuluka kwa ena kuposa ena; ndipo amene apatsidwa mochulukawo sangagawire zopatsidwa zawo omwe manja awo adzanjadzanja apeza (akapolo awo) kuti akhale ofanana pa zopatsidwazo, (nanga bwanji inu mukuti Allah ngofanana ndi akapolo Ake pomwe inu simufuna kufanana ndi akapolo anu?) Nanga kodi mtendere wa Allah akuukana?
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱللَّهُ جَعَلَ لَكُم مِّنۡ أَنفُسِكُمۡ أَزۡوَٰجٗا وَجَعَلَ لَكُم مِّنۡ أَزۡوَٰجِكُم بَنِينَ وَحَفَدَةٗ وَرَزَقَكُم مِّنَ ٱلطَّيِّبَٰتِۚ أَفَبِٱلۡبَٰطِلِ يُؤۡمِنُونَ وَبِنِعۡمَتِ ٱللَّهِ هُمۡ يَكۡفُرُونَ
Ndiponso Allah adakulengerani akazi a mtundu wanu, ndipo adakupangirani ana ndi zidzukulu kuchokera mwa akazi anuwo; ndipo adakupatsani zinthu zabwinozabwino, kodi akukhulupirira zachabe, ndi kuchikana chisomo cha Allah?
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: An-Nachl
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala - Vertimų turinys

Išvertė Khalid Ibrahim Bitala.

Uždaryti