Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Aja (Korano eilutė): (53) Sūra: Sūra Al-Ahzab
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَدۡخُلُواْ بُيُوتَ ٱلنَّبِيِّ إِلَّآ أَن يُؤۡذَنَ لَكُمۡ إِلَىٰ طَعَامٍ غَيۡرَ نَٰظِرِينَ إِنَىٰهُ وَلَٰكِنۡ إِذَا دُعِيتُمۡ فَٱدۡخُلُواْ فَإِذَا طَعِمۡتُمۡ فَٱنتَشِرُواْ وَلَا مُسۡتَـٔۡنِسِينَ لِحَدِيثٍۚ إِنَّ ذَٰلِكُمۡ كَانَ يُؤۡذِي ٱلنَّبِيَّ فَيَسۡتَحۡيِۦ مِنكُمۡۖ وَٱللَّهُ لَا يَسۡتَحۡيِۦ مِنَ ٱلۡحَقِّۚ وَإِذَا سَأَلۡتُمُوهُنَّ مَتَٰعٗا فَسۡـَٔلُوهُنَّ مِن وَرَآءِ حِجَابٖۚ ذَٰلِكُمۡ أَطۡهَرُ لِقُلُوبِكُمۡ وَقُلُوبِهِنَّۚ وَمَا كَانَ لَكُمۡ أَن تُؤۡذُواْ رَسُولَ ٱللَّهِ وَلَآ أَن تَنكِحُوٓاْ أَزۡوَٰجَهُۥ مِنۢ بَعۡدِهِۦٓ أَبَدًاۚ إِنَّ ذَٰلِكُمۡ كَانَ عِندَ ٱللَّهِ عَظِيمًا
E inu amene mwakhulupirira! Musalowe m’nyumba za Mneneri pokhapokha chilolezo chitaperekedwa kwa inu kukadya, osati kukhala nkuyembekezera kupsa kwa chakudya. Koma mukaitanidwa, lowani. Ndipo mukamaliza kudya, balalikani; ndiponso musakambe nkhani zocheza. Chifukwa kutero kumavutitsa Mneneri. Ndipo iye amakuchitirani manyazi (kuti akutulutseni); koma Allah alibe manyazi ponena choona. Ndipo inu mukamawafunsa (akazi ake) za ziwiya, afunseni uku muli kuseri kwa Chotsekereza. Zimenezo ndi zoyera zedi ku mitima yanu ndi mitima yawo. Sikoyenera kwa inu kumvutitsa Mtumiki wa Allah, ndiponso nkosayenera kwa inu kukwatira akazi ake pambuyo pa imfa yake mpaka muyaya. Ndithu kutero ndi tchimo lalikulu kwa Allah.[330]
[330] Anasi (r.a) adanena kuti ndime iyi idatsika chifukwa cha anthu ena omwe ankangocheza m’nyumba ya Mtumiki (s.a.w), osatulukamo. Izi zidali motere: Pamene Mtumiki (s.a.w) adakwatira Zainabu Binti Jahashi, adachita phwando la chakudya ndipo adaitana anthu. Pamene adatha kudya ena a iwo adangokhala nkumacheza m’nyumba ya Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Pamenepo nkuti mkazi wake atayang’anitsa nkhope yake ku khoma la nyumba. Zoterezi zidamuvuta Mtumiki (s.a.w) kuti awatulutse m’nyumbamo. Apa mpamene Allah adavumbulutsa ndimeyi.
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Aja (Korano eilutė): (53) Sūra: Sūra Al-Ahzab
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti