Check out the new design

Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Saba’   Aja (Korano eilutė):

Saba’

ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ ٱلَّذِي لَهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَهُ ٱلۡحَمۡدُ فِي ٱلۡأٓخِرَةِۚ وَهُوَ ٱلۡحَكِيمُ ٱلۡخَبِيرُ
Kuyamikidwa konse ndikwa Allah Yemwe zakumwamba ndi zapansi nzake. Ndipo kutamandidwa konse pa tsiku la chimaliziro Nkwake. ndiponso Iye Ngwanzeru zakuya, Ngodziwa chilichonse.
Tafsyrai arabų kalba:
يَعۡلَمُ مَا يَلِجُ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَمَا يَخۡرُجُ مِنۡهَا وَمَا يَنزِلُ مِنَ ٱلسَّمَآءِ وَمَا يَعۡرُجُ فِيهَاۚ وَهُوَ ٱلرَّحِيمُ ٱلۡغَفُورُ
Akudziwa zimene zikulowa m’nthaka ndi zimene zikutulukamo; ndi zimene zikutsika kumwamba ndi zimene zikukwera kumeneko. Ndipo Iye Ngwachifundo kwabasi, Ngokhululuka kwambiri.[332]
[332] M’ndime iyi Allah akutidziwitsa kuti akudziwa zonse zimene zikulowa m’nthaka monga madzi, mitembo ndi zina zotero. Ndipo akudziwanso zimene zikutuluka m’menemo - monga mmera tizirombo, miyala yamtengo wapatali ndi madzi. Ndi zomwe zikutsika kumwamba monga mvula, matalala, mphenzi, madalitso, angelo Ake ndi mabuku Ake. Ndipo akudziwanso zimene zikukwera kumwamba - monga ntchito za akapolo Ake ndi zina zotero.
Tafsyrai arabų kalba:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَا تَأۡتِينَا ٱلسَّاعَةُۖ قُلۡ بَلَىٰ وَرَبِّي لَتَأۡتِيَنَّكُمۡ عَٰلِمِ ٱلۡغَيۡبِۖ لَا يَعۡزُبُ عَنۡهُ مِثۡقَالُ ذَرَّةٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَلَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَآ أَصۡغَرُ مِن ذَٰلِكَ وَلَآ أَكۡبَرُ إِلَّا فِي كِتَٰبٖ مُّبِينٖ
Ndipo osakhulupirira adanena: “Siizatidzera nthawi (Qiyâma).” Nena: “Iyayi! Ndikulumbira Mbuye wanga, ndithu ikudzerani. (Mbuye wanga) Wodziwa zobisika (zonse), sichingabisike kwa Iye cholemera ngati nyelere; chakumwamba, chapansi, ngakhale chochepa kuposa chimenecho; ngakhalenso chokulirapo, koma (zonsezo) zili m’buku (Lake) losonyeza poyera (chilichonse).”
Tafsyrai arabų kalba:
لِّيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِۚ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُم مَّغۡفِرَةٞ وَرِزۡقٞ كَرِيمٞ
Kuti adzawalipire amene akhulupirira ndi kuchita zabwino; iwo adzapeza chikhululuko ndi zopatsidwa zaulemu.
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلَّذِينَ سَعَوۡ فِيٓ ءَايَٰتِنَا مُعَٰجِزِينَ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ عَذَابٞ مِّن رِّجۡزٍ أَلِيمٞ
Koma amene alimbika kutsutsana ndi Ayah Zathu pomaganiza kuti atigonjetsa, pa iwo pali chilango chopweteka.
Tafsyrai arabų kalba:
وَيَرَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡعِلۡمَ ٱلَّذِيٓ أُنزِلَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَ هُوَ ٱلۡحَقَّ وَيَهۡدِيٓ إِلَىٰ صِرَٰطِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَمِيدِ
Koma amene apatsidwa (dalitso la) kudziwa akuzindikira kuti zimene zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako nzoona, ndipo zikuongolera ku njira ya Mwini mphamvu zoposa, Wotamandidwa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ هَلۡ نَدُلُّكُمۡ عَلَىٰ رَجُلٖ يُنَبِّئُكُمۡ إِذَا مُزِّقۡتُمۡ كُلَّ مُمَزَّقٍ إِنَّكُمۡ لَفِي خَلۡقٖ جَدِيدٍ
Ndipo osakhulupirira akunena (pouzana pakati pawo mwachipongwe): “Kodi Tikusonyezeni za munthu yemwe akukuuzani kuti (m’kadzafa) ndi kudukaduka m’dzakhala m’kalengedwe katsopano?”
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Saba’
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala - Vertimų turinys

Išvertė Khalid Ibrahim Bitala.

Uždaryti