Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Az-Zaarijaat   Aja (Korano eilutė):

Sūra Az-Zaarijaat

وَٱلذَّٰرِيَٰتِ ذَرۡوٗا
. Ndikulumbilira mphepo imene ikubalalitsa mitambo ya mvula.
Tafsyrai arabų kalba:
فَٱلۡحَٰمِلَٰتِ وِقۡرٗا
Ndi imene imasenza mitolo yolemera (ya madzi).
Tafsyrai arabų kalba:
فَٱلۡجَٰرِيَٰتِ يُسۡرٗا
Ndi kuyenda (nawo madziwo) mwaubwino.
Tafsyrai arabų kalba:
فَٱلۡمُقَسِّمَٰتِ أَمۡرًا
Ndi awo amene amagawa rizq (limene Allah amalipereka kwa amene wamfuna).
Tafsyrai arabų kalba:
إِنَّمَا تُوعَدُونَ لَصَادِقٞ
Ndithu zimene mukulonjezedwa nzoonadi, (zidzachitika).
Tafsyrai arabų kalba:
وَإِنَّ ٱلدِّينَ لَوَٰقِعٞ
Ndipo, ndithu malipiro (pa zochita zanu) adzapezekadi.
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلۡحُبُكِ
Ndikulumbilira thambo lomwe njira zake zambiri nzoikidwa mwaluso.
Tafsyrai arabų kalba:
إِنَّكُمۡ لَفِي قَوۡلٖ مُّخۡتَلِفٖ
Ndithu inu muli m’mau otsutsana, (pa zimene mukunena).
Tafsyrai arabų kalba:
يُؤۡفَكُ عَنۡهُ مَنۡ أُفِكَ
(Kupyolera m’mawu amenewa) akuchotsedwa ku icho (chikhulupiliro chalonjezo loona) amene adachotsedwa (ku chikhulupilirocho).
Tafsyrai arabų kalba:
قُتِلَ ٱلۡخَرَّٰصُونَ
Aonongeka abodza (amene akunena za tsiku lachiweruziro mongoganizira.)
Tafsyrai arabų kalba:
ٱلَّذِينَ هُمۡ فِي غَمۡرَةٖ سَاهُونَ
Iwo amene akubira mu umbuli, osalabadira (za tsiku lachimaliziro).
Tafsyrai arabų kalba:
يَسۡـَٔلُونَ أَيَّانَ يَوۡمُ ٱلدِّينِ
Akufunsa (mwachipongwe ponena kuti) “Lidzakhala liti tsiku lamalipiro?”
Tafsyrai arabų kalba:
يَوۡمَ هُمۡ عَلَى ٱلنَّارِ يُفۡتَنُونَ
(Limenelo ndi) tsiku lomwe iwo adzalangidwa ku Moto.
Tafsyrai arabų kalba:
ذُوقُواْ فِتۡنَتَكُمۡ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تَسۡتَعۡجِلُونَ
(Adzawauza kuti): “Lawani chilango chanu ichi chimene munkachifulumizitsa (kuti chikufikeni).”
Tafsyrai arabų kalba:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
Ndithu oopa (Allah) adzakhala (akusangalala) m’minda ndi mu akasupe okongola,
Tafsyrai arabų kalba:
ءَاخِذِينَ مَآ ءَاتَىٰهُمۡ رَبُّهُمۡۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَبۡلَ ذَٰلِكَ مُحۡسِنِينَ
Uku akulandira zimene wawapatsa Mbuye wawo (malipiro aulemu); ndithu iwo ankachita zabwino asanapeze izi.
Tafsyrai arabų kalba:
كَانُواْ قَلِيلٗا مِّنَ ٱلَّيۡلِ مَا يَهۡجَعُونَ
Nthawi yausiku amagona pang’ono. (Amadzuka nachita mapemphero mochulukitsa).
Tafsyrai arabų kalba:
وَبِٱلۡأَسۡحَارِ هُمۡ يَسۡتَغۡفِرُونَ
Ndipo kum’bandakucha, iwo amapempha chikhululuko,
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
Ndipo m’chuma chawo mudali gawo (lodziwika) la opempha ndi osapempha (mwa osauka).
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِي ٱلۡأَرۡضِ ءَايَٰتٞ لِّلۡمُوقِنِينَ
M’nthaka muli zizindikiro kwa otsimikiza, (zosonyeza kuti Allah alipo).
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِيٓ أَنفُسِكُمۡۚ أَفَلَا تُبۡصِرُونَ
Ndi mwa inu nomwe; kodi simuona?
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِي ٱلسَّمَآءِ رِزۡقُكُمۡ وَمَا تُوعَدُونَ
Ndipo kumwamba kuli zokuthandizani (pa moyo wanu), ndi zimene mukulonjezedwa.
Tafsyrai arabų kalba:
فَوَرَبِّ ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِ إِنَّهُۥ لَحَقّٞ مِّثۡلَ مَآ أَنَّكُمۡ تَنطِقُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kumwamba ndi pansi, ndithu zimenezo ndi zoona monga kulili kuyankhula kwanu.
Tafsyrai arabų kalba:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ضَيۡفِ إِبۡرَٰهِيمَ ٱلۡمُكۡرَمِينَ
Kodi yakufika nkhani ya alendo a Ibrahim; (angelo) olemekezeka?
Tafsyrai arabų kalba:
إِذۡ دَخَلُواْ عَلَيۡهِ فَقَالُواْ سَلَٰمٗاۖ قَالَ سَلَٰمٞ قَوۡمٞ مُّنكَرُونَ
Pamene adalowa kwa iye ndi kunena kuti: “Salaam,” (“Mtendere”)! Iye adayankha: “Salaam,” (“Mtendere) inu ndinu anthu osadziwika (achilendo).”
Tafsyrai arabų kalba:
فَرَاغَ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ فَجَآءَ بِعِجۡلٖ سَمِينٖ
Adatembenukira kwa akunyumba ake (mwakachetechete), ndipo adadza ndi nyama ya mwana wa ng’ombe yonona (yowotcha).
Tafsyrai arabų kalba:
فَقَرَّبَهُۥٓ إِلَيۡهِمۡ قَالَ أَلَا تَأۡكُلُونَ
Naipereka kwa iwo (koma sadadye); iye adanena (modabwa): “Kodi bwanji simukudya?”
Tafsyrai arabų kalba:
فَأَوۡجَسَ مِنۡهُمۡ خِيفَةٗۖ قَالُواْ لَا تَخَفۡۖ وَبَشَّرُوهُ بِغُلَٰمٍ عَلِيمٖ
Mumtima mwake adadzazidwa mantha ndi iwo. Iwo adati: “Usaope,” ndipo adamuuza nkhani yabwino ya kubala mwana wodziwa.
Tafsyrai arabų kalba:
فَأَقۡبَلَتِ ٱمۡرَأَتُهُۥ فِي صَرَّةٖ فَصَكَّتۡ وَجۡهَهَا وَقَالَتۡ عَجُوزٌ عَقِيمٞ
Adadza mkazi wake ndi mkuwe (pamene adamva nkhani yabwino ija). Adadzimenya kunkhope (ndi dzanja lake kusonyeza kudabwa ndi kusatheka). Ndipo adati: (“Ine ndine) nkhalamba (ndiponso) chumba; (ndingabereke bwanji)?”
Tafsyrai arabų kalba:
قَالُواْ كَذَٰلِكِ قَالَ رَبُّكِۖ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡحَكِيمُ ٱلۡعَلِيمُ
Iwo adati: “Momwemo, Mbuye wako wanena. Iye Ngwanzeru zakuya (pa chilichonse chimene akulamula); Ngodziwa; (palibe chimene chingabisike kwa Iye).
Tafsyrai arabų kalba:
۞ قَالَ فَمَا خَطۡبُكُمۡ أَيُّهَا ٱلۡمُرۡسَلُونَ
۞ (Ibrahim) adati: “Kodi nkhani yanu ndiyotani E inu otumidwa?”
Tafsyrai arabų kalba:
قَالُوٓاْ إِنَّآ أُرۡسِلۡنَآ إِلَىٰ قَوۡمٖ مُّجۡرِمِينَ
Iwo adati: “Tatumizidwa kwa anthu oipa.”
Tafsyrai arabų kalba:
لِنُرۡسِلَ عَلَيۡهِمۡ حِجَارَةٗ مِّن طِينٖ
“Kuti tiwagende ndi miyala yotenthedwa kuchokera kudongo.”
Tafsyrai arabų kalba:
مُّسَوَّمَةً عِندَ رَبِّكَ لِلۡمُسۡرِفِينَ
“Yoikidwa chizindikiro cha aliyense wochimwa kuchokera kwa Mbuye wako.”
Tafsyrai arabų kalba:
فَأَخۡرَجۡنَا مَن كَانَ فِيهَا مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Tidawatulutsa okhulupirira omwe adali m’mudzimo.
Tafsyrai arabų kalba:
فَمَا وَجَدۡنَا فِيهَا غَيۡرَ بَيۡتٖ مِّنَ ٱلۡمُسۡلِمِينَ
Sitidapeze mmenemo (okhulupirira ambiri) kupatula mnyumba imodzi ya Asilamu.
Tafsyrai arabų kalba:
وَتَرَكۡنَا فِيهَآ ءَايَةٗ لِّلَّذِينَ يَخَافُونَ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَلِيمَ
Ndipo tidasiya pamenepo chizindikiro (chosonyeza kuonongeka kwa eni mudziwo kuti chikhale lingaliro) kwa amene akuopa chilango chopweteka.
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِي مُوسَىٰٓ إِذۡ أَرۡسَلۡنَٰهُ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ بِسُلۡطَٰنٖ مُّبِينٖ
M’nkhani ya Mûsa (muli phunziro) pamene tidamtuma kwa Farawo uku atalimbikitsidwa ndi chisonyezo choonekera.
Tafsyrai arabų kalba:
فَتَوَلَّىٰ بِرُكۡنِهِۦ وَقَالَ سَٰحِرٌ أَوۡ مَجۡنُونٞ
Koma Farawo adanyoza (kukhulupirira Mûsa) chifukwa chotama nyonga zake, ndipo adati: “Uyu ndi wamatsenga kapena wamisala.”
Tafsyrai arabų kalba:
فَأَخَذۡنَٰهُ وَجُنُودَهُۥ فَنَبَذۡنَٰهُمۡ فِي ٱلۡيَمِّ وَهُوَ مُلِيمٞ
Tidamlanga pamodzi ndi khamu lake la nkhondo ndi kuwaponya mnyanja; iye ali wodzudzulidwa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِي عَادٍ إِذۡ أَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمُ ٱلرِّيحَ ٱلۡعَقِيمَ
Ndipo m’nkhani ya Âdi (muli phunziro) pamene tidawatumizira chimphepo (chamkuntho) chopanda chabwino mkati mwake.
Tafsyrai arabų kalba:
مَا تَذَرُ مِن شَيۡءٍ أَتَتۡ عَلَيۡهِ إِلَّا جَعَلَتۡهُ كَٱلرَّمِيمِ
Chomwe sichisiya chinthu chimene chachidutsa koma kuchichita monga chofumbwa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَفِي ثَمُودَ إِذۡ قِيلَ لَهُمۡ تَمَتَّعُواْ حَتَّىٰ حِينٖ
Ndipo m’nkhani ya Samudu (muli chisonyezo) pamene kudanenedwa kwa iwo kuti: “Sangalalani (mnyumba zanu) mpaka nthawi yaikika.”
Tafsyrai arabų kalba:
فَعَتَوۡاْ عَنۡ أَمۡرِ رَبِّهِمۡ فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلصَّٰعِقَةُ وَهُمۡ يَنظُرُونَ
Koma adadzikweza (ponyozera) lamulo la Mbuye wawo. Choncho chiphokoso chidawaononga uku akupenya.
Tafsyrai arabų kalba:
فَمَا ٱسۡتَطَٰعُواْ مِن قِيَامٖ وَمَا كَانُواْ مُنتَصِرِينَ
Sadathe kuimilira ndi (kuthawa) ndiponso sadali wodzipulumutsa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَقَوۡمَ نُوحٖ مِّن قَبۡلُۖ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَوۡمٗا فَٰسِقِينَ
Naonso anthu a Nuh (tidawaononga) kale chifukwa iwo adali anthu otuluka mchilamulo (cha Allah).
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلسَّمَآءَ بَنَيۡنَٰهَا بِأَيۡيْدٖ وَإِنَّا لَمُوسِعُونَ
Thambo tidalimanga mwamphamvu (ndi luntha); ndipo tingathe kuchita zochuluka (kuposa zimenezi.)
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلۡأَرۡضَ فَرَشۡنَٰهَا فَنِعۡمَ ٱلۡمَٰهِدُونَ
Ndipo nthaka tidaiyala; taonani kukonza bwino Ife amene tidakonza nthaka!
Tafsyrai arabų kalba:
وَمِن كُلِّ شَيۡءٍ خَلَقۡنَا زَوۡجَيۡنِ لَعَلَّكُمۡ تَذَكَّرُونَ
Ndipo m’chinthu chilichonse talenga ziwiriziwiri kuti inu mulingalire (ndi kukhulupirira mphamvu Zathu).
Tafsyrai arabų kalba:
فَفِرُّوٓاْ إِلَى ٱللَّهِۖ إِنِّي لَكُم مِّنۡهُ نَذِيرٞ مُّبِينٞ
Thawirani kwa Allah. Ine ndine mchenjezi woonekera kwa inu wochokera kwa Iye.
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَا تَجۡعَلُواْ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَۖ إِنِّي لَكُم مِّنۡهُ نَذِيرٞ مُّبِينٞ
Ndipo musadzipangire mulungu wina wompembedza ndi kumuphatikiza ndi Allah. Ndithu ine ndine mchenjezi woonekera poyera kwa inu wochokera kwa Iye.
Tafsyrai arabų kalba:
كَذَٰلِكَ مَآ أَتَى ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِم مِّن رَّسُولٍ إِلَّا قَالُواْ سَاحِرٌ أَوۡ مَجۡنُونٌ
Momwemo (ndimo idalili mibadwo yakale pamodzi ndi aneneri awo); palibe Mthenga amene adawadzera anthu akale, anthu akowa kulibe, popanda kumnena kuti: “Ndiwamatsenga kapena wamisala.”
Tafsyrai arabų kalba:
أَتَوَاصَوۡاْ بِهِۦۚ بَلۡ هُمۡ قَوۡمٞ طَاغُونَ
Kodi adalangizana za mawuwa pakati pawo? Iyayi, koma iwo ndianthu opyola malire.
Tafsyrai arabų kalba:
فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ فَمَآ أَنتَ بِمَلُومٖ
Choncho apatukire iwo (amakani), iwe suli wodzudzulidwa (pakuleka kwawo kuyankha kuitana).
Tafsyrai arabų kalba:
وَذَكِّرۡ فَإِنَّ ٱلذِّكۡرَىٰ تَنفَعُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Kumbutsa. Ndithu kukumbutsa kumawathandiza okhulupirira.
Tafsyrai arabų kalba:
وَمَا خَلَقۡتُ ٱلۡجِنَّ وَٱلۡإِنسَ إِلَّا لِيَعۡبُدُونِ
Sindidalenge ziwanda (majini) ndi anthu koma kuti azindipembedza.
Tafsyrai arabų kalba:
مَآ أُرِيدُ مِنۡهُم مِّن رِّزۡقٖ وَمَآ أُرِيدُ أَن يُطۡعِمُونِ
Sindifuna kwa iwo chithandizo ndiponso sindifuna kuti azindidyetsa.
Tafsyrai arabų kalba:
إِنَّ ٱللَّهَ هُوَ ٱلرَّزَّاقُ ذُو ٱلۡقُوَّةِ ٱلۡمَتِينُ
Ndithu Allah ndi Amene amapereka rizq; Iye ndi Mwini mphamvu zoposa; Wolimba, (salaphera kanthu).
Tafsyrai arabų kalba:
فَإِنَّ لِلَّذِينَ ظَلَمُواْ ذَنُوبٗا مِّثۡلَ ذَنُوبِ أَصۡحَٰبِهِمۡ فَلَا يَسۡتَعۡجِلُونِ
Ndithu amene adzichitira okha chinyengo (pokana ndi kutsutsa) ali nalo gawo la chilango monga gawo la anzawo (a mibadwo yakale); choncho asandifulumizitse (kutsitsa chilango nthawi yake isanafike)!
Tafsyrai arabų kalba:
فَوَيۡلٞ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن يَوۡمِهِمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Kuonongeka kuli pa amene atsutsa za tsiku lawo limene alonjezedwa.
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Az-Zaarijaat
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti