Check out the new design

വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ * - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക


പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: ത്തൗബഃ   ആയത്ത്:
قَٰتِلُوهُمۡ يُعَذِّبۡهُمُ ٱللَّهُ بِأَيۡدِيكُمۡ وَيُخۡزِهِمۡ وَيَنصُرۡكُمۡ عَلَيۡهِمۡ وَيَشۡفِ صُدُورَ قَوۡمٖ مُّؤۡمِنِينَ
Menyanani nao; Allah awalanga kupyolera m’manja anu, ndipo awasambula ndi kukupulumutsani kwa iwo ndi kuchiritsa kuwawidwa (komwe kudali) m’mitima mwa anthu okhulupirira (chifukwa cha masautso omwe adawapeza kwa iwo).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَيُذۡهِبۡ غَيۡظَ قُلُوبِهِمۡۗ وَيَتُوبُ ٱللَّهُ عَلَىٰ مَن يَشَآءُۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٌ
Ndi kuchotsa mkwiyo wa m’mitima mwawo (Asilamu). Ndi kuti Allah Alandire kulapa kwa amene wamfuna. Ndipo Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
أَمۡ حَسِبۡتُمۡ أَن تُتۡرَكُواْ وَلَمَّا يَعۡلَمِ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ جَٰهَدُواْ مِنكُمۡ وَلَمۡ يَتَّخِذُواْ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَلَا رَسُولِهِۦ وَلَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَلِيجَةٗۚ وَٱللَّهُ خَبِيرُۢ بِمَا تَعۡمَلُونَ
Kodi mukuganiza kuti mungosiidwa chabe Allah asanawaonetsere poyera amene amenyera chipembedzo mwa inu ndi amene sachita ubwenzi (ndi wina wake) kupatula Allah ndi Mtumiki wake ndi okhulupirira? Ndipo Allah Ngodziwa zonse zimene muchita.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
مَا كَانَ لِلۡمُشۡرِكِينَ أَن يَعۡمُرُواْ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ شَٰهِدِينَ عَلَىٰٓ أَنفُسِهِم بِٱلۡكُفۡرِۚ أُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ وَفِي ٱلنَّارِ هُمۡ خَٰلِدُونَ
Nkosayenera kwa Amushirikina kukhala (ndi udindo) woyang’anira Misikiti ya Allah pomwe iwo akudzichitira okha umboni kuti ngosakhulupirira. Awo (ndi omwe) zochita zawo zabwino zapita pachabe. Ndipo iwo ku Moto adzakhala nthawi yaitali.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
إِنَّمَا يَعۡمُرُ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ مَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَأَقَامَ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَى ٱلزَّكَوٰةَ وَلَمۡ يَخۡشَ إِلَّا ٱللَّهَۖ فَعَسَىٰٓ أُوْلَٰٓئِكَ أَن يَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu oyang’anira Misikiti ya Allah ndi kuiyendera ndi amene akhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, ndi kumapemphera Swala ndi kupereka chopereka (Zakaat) ndipo saopa aliyense koma Allah yekha. Choncho, iwowo ndi amene akuyembekezeka kukhala mwa oongoka.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
۞ أَجَعَلۡتُمۡ سِقَايَةَ ٱلۡحَآجِّ وَعِمَارَةَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ كَمَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَجَٰهَدَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۚ لَا يَسۡتَوُۥنَ عِندَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi kumwetsa madzi (anthu) ochita Hajj ndi kusunga Msikiti Wopatulika mukukuyesa kuti nkofanana ndi yemwe wakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, ndi kumenya nkhondo pa njira Ya Allah? Sangakhale ofanana kwa Allah. Ndipo Allah saongola anthu ochita zolakwa.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَهَاجَرُواْ وَجَٰهَدُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ أَعۡظَمُ دَرَجَةً عِندَ ٱللَّهِۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡفَآئِزُونَ
Amene akhulupirira, ndi kusamuka, ndi kumenya nkhondo pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi matupi awo, ali ndi ulemelero waukulu kwa Allah. Iwowo ndiwo opambana.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
 
പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: ത്തൗബഃ
സൂറത്തുകളുടെ സൂചിക പേജ് നമ്പർ
 
വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക

ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബേത്താല അതു വിവർത്തനം ചെയ്തു.

അടക്കുക